-
Kodi Dzina Lanu Lili M’buku la Moyo?Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
10. Kodi Yesu anaona zinthu ziti zolimbikitsa mumpingo wa ku Sade, ndipo zimenezi ziyenera kutikhudza motani?
10 Mawu otsatira amene Yesu anauza mpingo wa ku Sade anali olimbikitsa kwambiri. Iye anati: “Ngakhale zili choncho, uli ndi mayina angapo mu Sade a anthu amene sanaipitse malaya awo akunja. Amenewa adzayenda ndi ine atavala malaya oyera, chifukwa ndi oyenerera. Choncho amene wapambana pa nkhondo adzavekedwa malaya akunja oyera. Ndipo sindidzafafaniza dzina lake m’buku la moyo, koma ndidzavomereza dzina lake pamaso pa Atate wanga, ndi pamaso pa angelo ake.” (Chivumbulutso 3:4, 5) Mawu amenewatu ndi osangalatsa ndipo akutilimbikitsa kuti tipitirizebe kukhala anthu okhulupirika. Ngati akulu atayamba kulekerera zinthu zoipa mumpingo, mpingo wonse ungathe kugona tulo tofa nato mwauzimu. Komabe, Akhristu ena mumpingomo angayesetse molimba mtima kuti apitirizebe kukhala oyera ndiponso osadetsedwa n’cholinga choti akhalebe ndi dzina labwino pamaso pa Yehova.—Miyambo 22:1.
-
-
Kodi Dzina Lanu Lili M’buku la Moyo?Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
13. Mofanana ndi Akhristu a ku Sade, kodi Akhristu odzozedwa amene “sanaipitse malaya awo akunja” amalandira madalitso otani?
13 Akhristu a ku Sade amene anali okhulupirika mpaka mapeto ndipo sanadetse chizindikiro chawo chachikhristu, analandira madalitso amene ankayembekezera. Ufumu wa Yesu, yemwe ndi Mesiya, utayamba mu 1914, iwo anayamba kuukitsidwa n’kupatsidwa moyo wauzimu. Komanso popeza iwo anapambana pa nkhondo, anavekedwa malaya oyera akunja monga chizindikiro choti ndi opanda uchimo komanso olungama. Iwo analandira madalitso amene adzasangalale nawo kosatha chifukwa anayenda mumsewu wopanikiza wopita ku moyo.—Mateyu 7:14; onaninso Chivumbulutso 6:9-11.
Mayina Awo Adzakhala M’buku la Moyo Kwamuyaya
14. Kodi ‘buku la moyo’ n’chiyani ndipo m’bukuli mumalembedwa mayina a ndani?
14 Kodi ‘buku la moyo’ n’chiyani ndipo ndi anthu otani amene mayina awo sadzafafanizidwa m’bukuli? Buku, kapena kuti mpukutu wa moyo, likutanthauza m’ndandanda wa atumiki a Yehova amene ali oyenerera kudzalandira mphoto ya moyo wosatha. (Malaki 3:16) Mayina a m’buku la moyo amene buku la Chivumbulutso likutchula, ndi a Akhristu odzozedwa. Koma m’buku la moyoli mulinso mayina a anthu amene ali oyenerera kudzalandira moyo wosatha padziko lapansi. Ngakhale zili choncho, mayina akhoza ‘kufafanizidwa’ m’buku la moyo limeneli. (Ekisodo 32:32, 33) Komabe, Akhristu odzozedwa amene mayina awo amakhalabe m’bukuli mpaka imfa yawo, amalandira moyo umene sungafe kumwamba. (Chivumbulutso 2:10) Mayina amenewa ndi amene Yesu amawavomereza pamaso pa Atate wake ndiponso pamaso pa angelo. Imeneyitu ndi mphoto yamtengo wapatali kwambiri.
15. Kodi anthu a m’khamu lalikulu ayenera kuchita chiyani kuti mayina awo asadzafafanizidwe m’buku la moyo?
15 Anthu a m’khamu lalikulu, amenenso mayina awo alembedwa m’buku la moyo, adzatuluka m’chisautso chachikulu ali ndi moyo. Iwo akadzakhalabe okhulupirika mu ulamuliro wonse wa Yesu wa zaka 1,000, ndiponso akadzapirira chiyeso chomaliza, adzalandira moyo wosatha m’Paradaiso padziko lapansi. (Danieli 12:1; Chivumbulutso 7:9, 14; 20:15; 21:4) Zimenezi zikadzachitika, ndiye kuti mayina awo sadzafafanizidwanso m’buku la moyo. Popeza mwadziwa uthenga umene unatumizidwa kudzera mwa mzimu woyera, simuyenera kuzengereza kuchita zimene Yesu akutipempha mobwerezabwereza kuti: “Amene ali ndi makutu amve zimene mzimu ukunena ku mipingo.”—Chivumbulutso 3:6.
-