-
Ufumu wa Mulungu WabadwaMapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
17, 18. (a) Kodi Yohane analemba kuti Satana ataponyedwa kudziko lapansi, kumwamba kunachitika zotani? (b) Kodi mawu ofuula amene Yohane anamva ayenera kuti anali a ndani?
17 Yohane analemba kuti Satana ataponyedwa kudziko lapansi, kumwamba kunali chisangalalo chachikulu. Iye anati: “Ndipo ndinamva mawu ofuula kumwamba, akuti: ‘Tsopano chipulumutso, mphamvu, ufumu wa Mulungu wathu, ndi ulamuliro wa Khristu wake zafika, chifukwa woneneza abale athu waponyedwa pansi. Iyeyo anali kuwaneneza usana ndi usiku pamaso pa Mulungu wathu. Iwo anamugonjetsa chifukwa cha magazi a Mwanawankhosa, ndiponso chifukwa cha mawu a umboni wawo. Ndipo iwo sanaone kuti miyoyo yawo ndi yofunika, ngakhale pamene anali pa ngozi yoti akhoza kufa. Pa chifukwa chimenechi, kondwerani kumwamba inu ndi inu okhala kumeneko!’”—Chivumbulutso 12:10-12a.
-
-
Ufumu wa Mulungu WabadwaMapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
20. Kodi Akhristu okhulupirika agonjetsa bwanji Satana?
20 Akhristu odzozedwa, amene amaonedwa kuti ndi olungama “chifukwa cha magazi a Mwanawankhosa,” akupitiriza kuchitira umboni za Mulungu ndi za Yesu Khristu ngakhale kuti akuzunzidwa. Kwa zaka zoposa 120, Akhristu odzozedwawa akhala akufotokoza nkhani zofunika kwambiri zimene zikukhudzana ndi kutha kwa Nthawi za Akunja mu 1914. (Luka 21:24, Buku Lopatulika Ndilo Mau a Mulungu) Ndipo panopa a khamu lalikulu akutumikira nawo limodzi mokhulupirika. Anthu onsewa ‘sachita mantha ndi amene amapha thupi koma sangaphe moyo.’ Zinthu zimene Mboni za Yehova zakhala zikuchita zasonyeza bwino mfundo imeneyi mobwerezabwereza m’nthawi yathu ino. Ndi mawu awo ndiponso ndi khalidwe lawo labwino lachikhristu, iwo agonjetsa Satana, ndipo asonyeza mobwerezabwereza kuti iye ndi wabodza. (Mateyu 10:28; Miyambo 27:11; Chivumbulutso 7:9) Akhristu odzozedwa akaukitsidwa n’kupita kumwamba, amasangalala kwambiri chifukwa kulibenso Satana woti azineneza abale awo. Inodi ndi nthawi yoti khamu lonse la angelo livomereze mosangalala mawu ofuula, akuti: “Kondwerani kumwamba inu ndi inu okhala kumeneko!”
-