Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Baibulo Ndi Buku Lochokera kwa Mulungu
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 2. Kodi munthu aliyense akhoza kupeza Baibulo?

      Anthu a ‘m’dziko lililonse, fuko lililonse, chilankhulo chilichonse ndi mtundu uliwonse’ akhoza kupeza uthenga wabwino wa m’Baibulo. (Werengani Chivumbulutso 14:6.) Mulungu anaonetsetsa kuti Baibulo lizipezeka m’zilankhulo zambiri kuposa buku lina lililonse. Pafupifupi munthu aliyense akhoza kupeza Baibulo ndipo zilibe kanthu kuti amakhala kuti kapena amalankhula chilankhulo chiti.

  • Kodi Angelo Ndi Ndani, Nanga Amachita Zotani?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • Mngelo akutsogolera a Mboni za Yehova awiri pamene akulalikira kunyumba ndi nyumba.

      4. Angelo amathandiza anthu kuphunzira zokhudza Yehova

      Angelo a Mulungu salalikira mwachindunji kwa anthu. M’malomwake amatsogolera atumiki a Mulungu kwa anthu amene akufuna kuphunzira. Werengani Chivumbulutso 14:6, 7, kenako mukambirane mafunso awa:

      • N’chifukwa chiyani timafunikira kuthandizidwa ndi angelo tikamalalikira?

      • Kodi mukumva bwanji mukaganizira kuti angelo angakutsogolereni kwa anthu amene akufuna kuphunzira Baibulo? N’chifukwa chiyani mukumva choncho?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena