-
Kodi Mudzaima Motani ku Mpando wa Chiweruzo?Nsanja ya Olonda—1995 | October 15
-
-
pa zonse, kwa Eklesia.” (Aefeso 1:20-23) Chifukwa chakuti Yesu nthaŵiyo anali ndi ulamuliro waufumu pa Akristu, Paulo anakhoza kulemba kuti Yehova “anatilanditsa ife ku ulamuliro wa mdima, natisunthitsa kutiloŵetsa mu ufumu wa Mwana wa chikondi chake.”—Akolose 1:13; 3:1.
15, 16. (a) Kodi nchifukwa ninji tikuti Yesu sanakhale Mfumu ya Ufumu wa Mulungu mu 33 C.E.? (b) Kodi Yesu anayamba liti kulamulira mu Ufumu wa Mulungu?
15 Komabe, nthaŵiyo Yesu sanakhale Mfumu ndi Woweruza pa amitundu. Anakhala pafupi ndi Mulungu, akumayembekezera nthaŵi ya kukhala Mfumu ya Ufumu wa Mulungu. Paulo analemba ponena za iye kuti: “Za mngelo uti anati nthaŵi iliyonse, Khala pa dzanja lamanja langa, kufikira ndikaika adani ako mpando wa ku mapazi ako?”—Ahebri 1:13.
16 Mboni za Yehova zafalitsa umboni wochuluka wakuti nyengo ya kuyembekeza kwa Yesu inatha mu 1914, pamene iye anakhala wolamulira wa Ufumu wa Mulungu m’miyamba yosaoneka. Chivumbulutso 11:15, 18 chimati: “Ufumu wa dziko lapansi wayamba kukhala wa Ambuye wathu, ndi wa Kristu wake: ndipo adzachita ufumu kufikira nthaŵi za nthaŵi.” “Ndipo amitundu anakwiya, ndipo unadza mkwiyo wanu.” Inde, amitundu anakwiyirana pa Nkhondo Yadziko I. (Luka 21:24) Nkhondo, zivomezi, miliri, njala, ndi zina zotero, zimene taona chiyambire 1914 zimatsimikiza kuti Yesu tsopano akulamulira mu Ufumu wa Mulungu, ndi kuti mapeto a dzikoli ali pafupi.—Mateyu 24:3-14.
17. Kodi ndi mfundo zofunika ziti zimene tapeza kufikira pano?
17 Nawa malongosoledwe achidule: Mulungu anganenedwe kuti wakhala pa mpando wachifumu monga Mfumu, koma m’lingaliro lina iye angakhale pa mpando wake wachifumu kuweruza. Mu 33 C.E., Yesu anakhala kudzanja lamanja la Mulungu, ndipo tsopano ndi Mfumu ya Ufumuwo. Koma kodi Yesu, amene akulamulira monga Mfumu tsopano, alinso Woweruza? Ndipo nchifukwa ninji zimenezi zili zofunika kwa ife, makamaka nthaŵi inoyi?
18. Kodi pali umboni wotani wakuti Yesu adzakhalanso Woweruza?
18 Yehova, amene ali ndi mphamvu ya kuika oweruza, anasankha Yesu monga Woweruza wokwaniritsa miyezo Yake. Yesu anasonyeza zimenezi polankhula zakuti anthu adzakhala amoyo mwauzimu: “Atate saweruza munthu aliyense, koma anapereka kuweruza konse kwa Mwana.” (Yohane 5:22) Komabe, mbali ya Yesu ya kuweruza imaposa pamenepo, pakuti alinso woweruza wa amoyo ndi akufa. (Machitidwe 10:42; 2 Timoteo 4:1) Nthaŵi ina Paulo anati: “[Mulungu] anapangira tsiku limene adzaweruza dziko lokhalamo anthu m’chilungamo, ndi munthu [Yesu] amene anamuikiratu, napatsa anthu chitsimikizo, pamene anamuukitsa iye.”—Machitidwe 17:31; Salmo 72:2-7.
19. Kodi nchifukwa ninji kuli kolondola kunena kuti Yesu amakhala pa mpando monga Woweruza?
19 Kodi tili ndi chifukwa chomveka chonenera kuti Yesu amakhala pa chimpando cha ulemerero wake pantchito yeniyeni ya Woweruza? Inde. Yesu anauza atumwi kuti: “Inu amene munanditsata ine, m’kubadwanso, pamene Mwana wa munthu adzakhala pa chimpando cha ulemerero wake, inunso, mudzakhala pa mipando khumi ndi iŵiri, kuweruza mafuko khumi ndi aŵiri a Israyeli.” (Mateyu 19:28) Ngakhale kuti Yesu tsopano ndi Mfumu ya Ufumuwo, ntchito yake ina yotchulidwa pa Mateyu 19:28 idzaphatikizapo kukhala pa mpando wachifumu kuweruza mkati mwa Zaka Chikwi. Panthaŵiyo adzaweruza anthu onse, olungama ndi osalungama. (Machitidwe 24:15) Kuli kothandiza kukumbukira zimenezi pamene tisumika maganizo athu pa limodzi la mafanizo a Yesu limene limakhudza nthaŵi yathu ndi miyoyo yathu.
Kodi Fanizolo Limati Chiyani?
20, 21. Kodi atumwi a Yesu anafunsa za chiyani chimene chimakhudza nthaŵi yathu, chikumabutsa funso lotani?
20 Imfa ya Yesu itayandikira, atumwi ake anamfunsa kuti: “Zija zidzaoneka liti? Ndipo chizindikiro cha [kukhalapo, NW] kwanu nchiyani, ndi cha mathedwe a nthaŵi ya pansi pano?” (Mateyu 24:3) Yesu analosera zochitika zazikulu zimene zidzakhalako pa dziko lapansi ‘mathedwe asanadze.’ Mapetowo atakhala pafupi, mitundu ‘idzapenya Mwana wa munthu alinkudza pa mitambo ya kumwamba, ndi mphamvu ndi ulemerero waukulu.’—Mateyu 24:14, 29, 30.
21 Koma kodi anthu a mitunduwo zinthu zidzawakhalira bwanji pamene Mwana wa munthu adza ndi ulemerero wake? Tiyeni tipeze yankho lake m’fanizo la nkhosa ndi mbuzi, limene limayamba ndi mawu aŵa: “Koma pamene Mwana wa munthu adzadza mu ulemerero wake, ndi angelo onse pamodzi naye, pomwepo iye adzakhala pa chimpando cha kuŵala kwake: ndipo adzasonkhanidwa pamaso pake anthu a mitundu yonse.”—Mateyu 25:31, 32.
22, 23. Kodi ndi mfundo ziti zimene zikusonyeza kuti fanizo la nkhosa ndi mbuzi silinayambe kukwaniritsidwa mu 1914?
22 Kodi fanizo limeneli limanena za nthaŵi pamene Yesu anakhala pa mpando m’mphamvu yachifumu mu 1914, malinga ndi zimene tadziŵa nthaŵi yaitali? Eya, Mateyu 25:34 amanenadi kuti iye ndi Mfumu, choncho fanizolo moyenerera liyamba kugwira ntchito Yesu atakhala Mfumu mu 1914. Koma kodi ndi kuweruza kotani kumene anachita mwamsanga pambuyo pake? Sikunali kuweruza “mitundu yonse.” M’malo mwake, anasumika maganizo ake pa aja omwe amati ndiwo “nyumba ya Mulungu.” (1 Petro 4:17) Mogwirizana ndi Malaki 3:1-3, Yesu, monga mthenga wa Yehova, anayang’anira mwa chiweruzo Akristu odzozedwa otsala pa dziko lapansi. Inalinso nthaŵi ya kupereka chiweruzo pa Dziko Lachikristu, limene monama linati ndilo “nyumba ya Mulungu.”c (Chivumbulutso 17:1, 2; 18:4-8) Komabe palibe chimene chikusonyeza kuti panthaŵiyo, kapena chiyambire nthaŵiyo, Yesu anakhala pa mpando kuweruza anthu a mitundu yonse komaliza monga nkhosa kapena mbuzi.
23 Tikapenda zochita za Yesu m’fanizolo, tikumuona iye akuweruza mitundu yonse komaliza. Fanizolo silikusonyeza kuti kuweruzako kudzapitiriza kwa nyengo ya zaka zambiri, ngati kuti anthu onse amene afa zaka zakumbuyoku aweruzidwira ku imfa yosatha kapena ku moyo wosatha. Zikuoneka kuti unyinji wa awo amene amwalira zaka zaposachedwapa apita kumanda a anthu onse. (Chivumbulutso 6:8; 20:13) Koma, fanizolo likusonyeza nthaŵi pamene Yesu akuweruza anthu a “mitundu yonse” amene ali amoyo panthaŵiyo ndipo akuyang’anizana ndi chilango cha chiweruzo chake.
24. Kodi fanizo la nkhosa ndi mbuzi lidzakwaniritsidwa liti?
24 M’mawu ena, fanizolo likusonya mtsogolo pamene Mwana wa munthu adzadza mu ulemerero wake. Adzakhala pa mpando kuweruza anthu amoyo panthaŵiyo. Chiweruzo chake chidzazikidwa pa umunthu wawo umene asonyeza. Nthaŵiyo “wolungama ndi woipa” adzakhala atazindikiridwa bwino. (Malaki 3:18) Kupereka chiweruzocho ndi chilango chake kudzachitika panthaŵi yaifupi. Yesu adzapereka ziweruzo zolungama zozikidwa pa mkhalidwe umene munthu yense adzakhala atasonyeza.—Onaninso 2 Akorinto 5:10.
25. Kodi Mateyu 25:31 akusonyezanji mwa kunena kuti Mwana wa munthu wakhala pa chimpando choŵala?
25 Chotero, zimenezi zikutanthauza kuti ‘kukhala kwa Yesu pa chimpando cha kuŵala kwake’ kwa chiweruzo, kotchulidwa pa Mateyu 25:31, kumanena za nthaŵi ya mtsogolo pamene Mfumu yamphamvu imeneyi idzakhala pa mpando kupereka chiweruzo ndi chilango pa mitundu. Inde, nkhani ya chiweruzo imene ikunena za Yesu pa Mateyu 25:31-33, 46 njofanana ndi nkhani ya pa Danieli chaputala 7, pamene Mfumu yolamulira, Nkhalamba ya Kale Lomwe, inakhala pa mpando kuchita ntchito yake ya Woweruza.
26. Kodi ndi kafotokozedwe kotani katsopano kamene kakhalapo?
26 Kulimva mwa njira imeneyi fanizo la nkhosa ndi mbuzi kumasonyeza kuti chiweruzo pa nkhosa ndi mbuzi chidzaperekedwa mtsogolo. Chidzachitika “masauko” [“chisautso,” NW] otchulidwa pa Mateyu 24:29, 30 atayamba ndipo Mwana wa munthu ‘adza ndi ulemerero.’ (Yerekezerani ndi Marko 13:24-26.) Ndiyeno, pokhala dongosolo lonse loipa lidzakhala litafika pamapeto ake, Yesu adzakhala pabwalo la milandu ndi kupereka chiweruzo ndi chilango.—Yohane 5:30; 2 Atesalonika 1:7-10.
27. Kodi tiyenera kufuna kudziŵa chiyani ponena za fanizo la Yesu lomaliza?
27 Zimenezi zikuwongolera kamvedwe kathu ka nthaŵi ya kukwaniritsidwa kwa fanizo la Yesu, kamene kakusonyeza pamene nkhosa ndi mbuzi zidzaweruzidwa. Koma kodi zimatikhudza motani ife amene tikulalikira mwachangu uthenga wabwino wa Ufumu? (Mateyu 24:14) Kodi zikuchititsa ntchito yathu kukhala yosafunika kwenikweni, kapena kodi zikutipatsa thayo lolemera kwambiri? Tiyeni tione m’nkhani yotsatira mmene zikutikhudzira.
-
-
Kodi Nkhosazo ndi Mbuzizo Zili ndi Mtsogolo Motani?Nsanja ya Olonda—1995 | October 15
-
-
Kodi Nkhosazo ndi Mbuzizo Zili ndi Mtsogolo Motani?
“Iye adzalekanitsa iwo wina ndi mnzake, monga mbusa alekanitsa nkhosa ndi mbuzi.”—MATEYU 25:32.
1, 2. Kodi nchifukwa ninji tiyenera kuchita chidwi ndi fanizo la nkhosa ndi mbuzi?
YESU KRISTU analidi Mphunzitsi wamkulu woposa onse pa dziko lapansi. (Yohane 7:46) Imodzi ya njira zake zophunzitsira inali kugwiritsira ntchito miyambi, kapena mafanizo. (Mateyu 13:34, 35) Ameneŵa anali osavuta koma amphamvu posonyeza choonadi chakuya chauzimu ndi chaulosi.
2 M’fanizo la nkhosa ndi mbuzi, Yesu anasonyeza nthaŵi pamene iye adzakhala ndi malo apadera: “Koma pamene Mwana wa munthu adzadza mu ulemerero wake, ndi . . . ” (Mateyu 25:31) Fanizo limeneli tiyenera kuchita nalo chidwi chifukwa ndilo limene Yesu akumaliza nalo yankho lake pa funsolo: “Chizindikiro cha [kukhalapo, NW] kwanu nchiyani, ndi cha mathedwe a nthaŵi ya pansi pano?” (Mateyu 24:3) Koma kodi zimenezi zikutanthauzanji kwa ife?
3. Poyambirira m’nkhani yake, kodi Yesu anati nchiyani chidzachitika chitangoyamba chisautso chachikulu?
3 Yesu ananeneratu za zochitika zodabwitsa zimene zidzachitika “pomwepo” chitaulika chisautso chachikulu, zochitika zomwe tikuziyembekezera. Anati pomwepo padzaoneka
-