Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • sn nyimbo 22
  • “Yehova Ndi M’busa Wanga”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Yehova Ndi M’busa Wanga”
  • Imbirani Yehova
  • Nkhani Yofanana
  • “Yehova ndi Mbusa Wanga”
    Imbirani Yehova Zitamando
  • “Yehova Ndi M’busa Wanga”
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • Yehova Ndi Mbusa Wathu
    Nsanja ya Olonda—2005
  • “Ndine Pano! Munditumize Ine”
    Imbirani Yehova Zitamando
Onani Zambiri
Imbirani Yehova
sn nyimbo 22

Nyimbo 22

“Yehova Ndi M’busa Wanga”

Losindikizidwa

(Salmo 23)

1. Yehova ndi M’busa wanga;

Kodi ndingaopenji?

Amasamala nkhosa zake,

Sadzaziiwaladi.

Andipititsa kumadzi

Kukanditsitsimula.

Anditsogolera poyenda

M’njira zachilungamo.

Anditsogolera poyenda

M’njira zachilungamo.

2. Poyenda mumdima ndekha,

Sindidzaopa kanthu.

M’busa wanga alitu nane

Kumandilimbikitsa.

Adzozatu mutu wanga,

Wadzaza chikho changa.

Chifundo chake chinditsate,

Ndikhale m’nyumba yake.

Chifundo chake chinditsate,

Ndikhale m’nyumba yake.

3. N’ngwachikonditu M’busayo!

Ndim’tamanda mokondwa.

Ndidzalalikira kwa ena

Za chikondi chakecho.

Ndidzamvera Mawu ake

Poyenda m’njira zake.

Mwayi wanga wom’tumikira

Ndiugwiritsa ntchito.

Mwayi wanga wom’tumikira

Ndiugwiritsa ntchito.

(Onaninso Sal. 28:9; 80:1.)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena