Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • N’chifukwa Chiyani Muyenera Kuphunzira Baibulo?
    Nsanja ya Olonda—2015 | April 1
    • Bambo akuwerenga Baibulo mu laibulale

      NKHANI YA PACHIKUTO | KODI MUNGAKONDE KUPHUNZIRA BAIBULO?

      N’chifukwa Chiyani Muyenera Kuphunzira Baibulo?

      • Kodi Mulungu anatilengeranji?

      • N’chifukwa chiyani timavutika komanso kufa?

      • Kodi m’tsogolomu mudzachitika zotani?

      • Kodi Mulungu amadera nkhawa za ine?

      Kodi inunso nthawi zina mumakhala ndi mafunso amenewa? Ngati ndi choncho, dziwani kuti si inu nokha. Anthu ambiri amafuna atadziwa mayankho a mafunso amenewa ndi enanso ambiri. Koma kodi n’zotheka kupeza mayankho a mafunsowa?

      Anthu ambiri angayankhe kuti inde n’zotheka, chifukwa anthuwa anapeza mayankho a m’Baibulo a mafunsowa. Ngati nanunso mukufuna kudziwa mayankho a mafunso amenewa, tikukulimbikitsani kuti muyambe kuphunzira Baibulo ndi a Mboni za Yehova kwaulere.a

      Komabe ambiri amaona kuti sangapeze nthawi yophunzira Baibulo. Enanso amaona kuti kuphunzira Baibulo n’kovuta kwambiri. Pomwe ena amaopa kupangana ndi wa Mboni kuti aziwaphunzitsa Baibulo chifukwa amaona kuti zimenezi ziziwapanikiza. Koma ena salola kuti zimenezi ziwalepheretse kuphunzira Baibulo. Taonani zitsanzo zotsatirazi:

      • Mayi ena a ku England, dzina lawo a Gill, anati: “Ndili ku yunivesite ndinkaphunzira zokhudza Mulungu. Komanso ndinapempherapo m’chipembedzo chachisiki, chachibuda komanso m’matchalitchi osiyanasiyana. Koma sindinapeze mayankho a mafunso anga. Ndiyeno tsiku lina, wa Mboni za Yehova wina anabwera kunyumba kwathu. Wamboniyo anayankha mafunso anga onse pogwiritsa ntchito Baibulo. Chifukwa cha zimenezi ndinavomera kuti azindiphunzitsa Baibulo.”

      • Bambo ena a ku Benin, dzina lawo a Koffi, anati: “Ndinali ndi mafunso ambirimbiri, koma zimene abusa a kutchalitchi kwathu ankandiyankha, sizinkandigwira mtima. Koma wa Mboni wina anayankha mafunso anga onse pogwiritsa ntchito Baibulo. Atandifunsa ngati ndingakonde kuphunzira Baibulo kuti ndidziwe zambiri, ndinavomera.”

      • A José, a ku Brazil, anati: “Ndinkafuna nditadziwa zimene zimachitika munthu akamwalira. Ndinkakhulupirira kuti akufa angathe kuchitira anthu amoyo zinthu zoipa, komabe ndinkafuna nditadziwa zimene Baibulo limanena pa nkhaniyi. Choncho, ndinayamba kuphunzira Baibulo ndi mnzanga wina yemwe anali wa Mboni.”

      • Mayi ena a ku Mexico, dzina lawo a Dennize, anati: “Ndinkawerenga Baibulo koma sindinkalimvetsa. Kenako a Mboni za Yehova anabwera kwathu ndipo anandifotokozera momveka bwino maulosi angapo a m’Baibulo. Ndinkafuna kudziwa zambiri, choncho ndinavomera kuti azindiphunzitsa Baibulo.”

      • A Anju, a ku Nepal, anati: “Ndinkafuna kudziwa ngati Mulungu amandiganizira kapena ayi. Choncho, ndinaganiza zopemphera kwa Mulungu yemwe amatchulidwa m’Baibulo. Tsiku lotsatira, kunyumba kwathu kunabwera a Mboni ndipo atandipempha kuti ndiziphunzira nawo Baibulo, ndinavomera.”

      Zimene anthuwa ananenazi zikutikumbutsa mawu a Yesu akuti: “Odala ndi anthu amene amazindikira zosowa zawo zauzimu.” (Mateyu 5:3) Mwachibadwa, anthufe timafuna kudziwa Mulungu ndipo Mulungu watipatsa Mawu ake, Baibulo. Choncho tiyenera kuphunzira Baibulo kuti timudziwe bwino Mulungu.

      Koma kodi phunziro la Baibulo limachitika bwanji? Nanga kuphunzira Baibulo kungakuthandizeni bwanji? Mafunso amenewa ayankhidwa m’nkhani yotsatira.

      a Baibulo limati dzina la Mulungu ndi Yehova.

      MFUNDO ZOKHUDZA BAIBULO

      Baibulo Lotsegula
      • DZINA LOTI BAIBULO: Dzinali linachokera ku mawu achigiriki akuti bi·bliʹa, ndipo amatanthauza “mabuku ang’onoang’ono”

      • BAIBULO LONSE: Lili ndi mabuku 66. Mabuku 39 analembedwa m’Chiheberi (mbali zina za mabukuwa zinalembedwa m’Chiaramu), ndipo 27 otsalawo analembedwa m’Chigiriki

      • MMENE LINALEMBEDWERA: Linalembedwa ndi amuna 40 ndipo panatenga zaka 1,600 likulembedwa. Linayamba kulembedwa kutatsala zaka 1,513 kuti Yesu abadwe padzikoli, ndipo linamalizidwa patatha zaka 98 kuchokera pamene Yesu anabadwa.

      • ZINENERO: Panopa Baibulo lonse kapena mbali yake, lamasuliridwa m’zinenero zoposa 2,500

      • MABAIBULO AMENE AFALITSIDWA: Alipo okwana pafupifupi 4 biliyoni. Zimenezi zikusonyeza kuti Baibulo ndi buku lomwe lafalitsidwa kwambiri kuposa buku lina lililonse

  • Mwayi Woti Aliyense Aphunzire Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2015 | April 1
    • Akuphunzira Baibulo

      NKHANI YA PACHIKUTO | KODI MUNGAKONDE KUPHUNZIRA BAIBULO?

      Mwayi Woti Aliyense Aphunzire Baibulo

      A Mboni za Yehovafe timadziwika ndi ntchito yathu yolalikira. Koma kodi mukudziwa kuti timaphunziranso Baibulo ndi anthu padziko lonse?

      Bambo akuphunzira Baibulo kuntchito kwake

      M’chaka cha 2014, a Mboni za Yehova pafupifupi 8,000,000 omwe akupezeka m’mayiko 240 ankaphunzira Baibulo ndi anthu pafupifupi 9,500,000 mwezi uliwonse.a Chiwerengero chimenechi ndi chachikulu kuposa chiwerengero cha anthu a m’mayiko 140.

      Kuti tithe kugwira ntchitoyi, timasindikiza Mabaibulo, mabuku, magazini ndi zinthu zina zothandiza kuphunzira Baibulo zokwana 500 miliyoni m’zinenero pafupifupi 700. Zimenezi zimathandiza kuti anthu athe kuphunzira Baibulo m’chinenero chomwe amachidziwa bwino.

      “Kuphunzira Baibulo kunkandisangalatsa kwabasi, ngakhale kuti ndili kusukulu sindinkakonda kuphunzira. Komansotu zomwe ndinkaphunzira m’Baibulo zinkandilimbikitsa kwambiri.”—Katlego wa ku South Africa.

      “Nditayamba kuphunzira Baibulo ndinapeza mayankho a mafunso onse omwe ndinali nawo ndi enanso ambiri.”—A Bertha a ku Mexico.

      “Phunziro la Baibulo linkachitikira kunyumba kwathu pa nthawi yomwe ndinasankha. Zimenezi zinachititsa kuti ndiziona kuti palibe chomwe chingandilepheretse kuphunzira Baibulo.”—A Eziquiel a ku Brazil.

      “Nthawi zambiri ndinkaphunzira kwa maminitsi 15 kapena 30. Koma pena ndinkaphunzira nthawi yochulukirapo kuposa pamenepa. Zinkangodalira nthawi yomwe ndili nayo.”—A Viniana a ku Australia.

      “Phunziroli linali laulere komanso losangalatsa kwabasi.”—A Aimé a ku Benin.

      “Wa Mboni amene ankandiphunzitsa Baibulo anali woleza mtima komanso wokoma mtima kwambiri. Zimenezi zinapangitsa kuti tiyambe kugwirizana kwambiri, moti anali mnzanga wapamtima.”—A Karen a ku Northern Ireland.

      “Anthu ambiri amaphunzira Baibulo koma sakhala a Mboni za Yehova. Choncho si bwino kulephera kuphunzira Baibulo chifukwa choopa kuti mukhala wa Mboni.”—A Denton a ku England.

      MAYANKHO A MAFUNSO AMENE ANTHU AMAKONDA KUFUNSA, OKHUDZA PHUNZIRO LA BAIBULO

      Kodi phunziro la Baibulo limachitika bwanji?

      Timasankha mutu ndipo kenako timakambirana mavesi osiyanasiyana a m’Baibulo ogwirizana ndi mutuwo. Mwachitsanzo, pophunzira Baibulo, tingathe kupeza mayankho a mafunso monga akuti: Kodi Mulungu ndi ndani, nanga ndi wotani? Kodi Mulungu ali ndi dzina? Nanga amakhala kuti? Kodi n’zotheka kukhala naye pa ubwenzi? Koma mwina mungadabwe kuti, kodi timadziwa bwanji mavesi a m’Baibulo omwe akunena za nkhaniyo?

      Pophunzira Baibulo ndi anthu, timagwiritsa ntchito buku la masamba 224 lakuti, Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?b Bukuli limatithandiza kudziwa mavesi amene akugwirizana ndi nkhani imene tikukambirana. Buku limeneli linapangidwa n’cholinga choti lithandize anthu kumvetsa mfundo zosavuta zimene Baibulo limaphunzitsa. M’bukuli muli mutu womwe umanena kuti akufa adzaukitsidwa. Mulinso mutu wonena za Mulungu, wonena za Yesu Khristu, za pemphero, chifukwa chake anthufe timavutika ndi ina yambiri.

      Kodi phunziroli limachitikira kuti ndipo limachitika nthawi yanji?

      Phunziroli limachitika pa nthawi ndi malo amene mungakonde.

      Nanga limatenga nthawi yaitali bwanji?

      Anthu ambiri amaphunzira Baibulo kwa ola limodzi mlungu uliwonse. Komabe, kutalika kwa nthawi ya phunziroli kumasiyanasiyana potengera zimene munthu angakonde. Ifeyo timatha kusintha kuti tigwirizane ndi zimene inuyo mukufuna. Ena amaphunzira kwa maminitsi 10 kapena 15 basi pa mlungu.

      Kodi munthu amalipira ndalama zingati kuti aziphunzira Baibulo?

      Phunziroli ndi laulere, ndipo mabuku amene timagwiritsa ntchito pophunzira sitilipiritsa. Zimenezi n’zogwirizana ndi zimene Yesu anauza ophunzira ake kuti: “Munalandira kwaulere, patsani kwaulere.”—Mateyu 10:8.

      Pamatenga nthawi yaitali bwanji kuti munthu adzamalize kuphunzira?

      Mukhoza kuphunzira Baibulo kwa nthawi imene inuyo mukufuna. Buku lakuti, Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? lili ndi mitu 19. Mukhoza kusankha mitu imene mukufuna kuphunzira kapena mukhoza kusankha kuphunzira mitu yonseyo. Zili kwa inunso kusankha kuti muziphunzira nthawi yaitali bwanji pa tsiku.

      Ndikavomera kuti ndiziphunzira Baibulo, kodi ndiye kuti ndiyenera kukhala wa Mboni za Yehova?

      Ayi. Timadziwa kuti munthu aliyense ali ndi ufulu wosankha chipembedzo chimene akufuna. Komabe timadziwanso kuti munthu akaphunzira Baibulo angathe kusankha bwino pa nkhani ya chipembedzo.

      Kodi ndingatani ngati ndikufuna kudziwa zambiri?

      Pitani pa webusaiti yathu ya jw.org/ny. Webusaitiyi ingakuthandizeni kudziwa zambiri zokhudza a Mboni za Yehova.

      Kodi ndingatani ngati ndikufuna kuphunzira Baibulo?

      • Anthu amapempha kuti aziphunzira Baibulo polemba kalata, kudzera pa Intaneti kapena pofunsa a Mboni za Yehova a kudera lawo

        Mungalembe pa webusaiti yathu ya jw.org/ny kuti mupemphe munthu woti aziphunzira nanu Baibulo.

      • Mukhozanso kutilembera kalata pogwiritsa ntchito adiresi yoyenera pa maadiresi omwe ali patsamba 2.

      • Mungathenso kufunsa a Mboni za Yehova a kudera lanulo.

      a Pophunzira Baibulo, timaphunzira ndi munthu mmodzi payekha kapena anthu angapo nthawi imodzi.

      b Bukuli ndi lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova ndipo likupezeka m’zinenero 260. Mabuku amene asindikizidwa ndi oposa 230 miliyoni.

      KUPHUNZIRA BAIBULO KUMATHANDIZA MABANJA

      Baibulo lotsegula

      “Mkazi wanga atayamba kuphunzira Baibulo, ndinaona kuti wasintha kwambiri. Banja lathunso linayamba kuyenda bwino. Zimenezi zinandichititsa chidwi, moti nanenso ndinayamba kuphunzira Baibulo. Zimene ndinaphunzira zinachititsa kuti nanenso ndisinthe n’kuyamba kuchita zabwino. Kuphunzira Baibulo kwathandiza kuti ine ndi mkazi wanga tizikondana kwambiri.”—A Eziquiel.

      A Eziquiel

      “Nditayamba kuphunzira Baibulo, ndinasiya kugwiritsa ntchito mankhwala osokoneza bongo, kumwa mowa mwauchidakwa komanso kukwiya msanga. Panopa m’nyumba mwathu mumaoneka mwaukhondo kwambiri. Komanso panopa ana ndi mwamuna wanga akachita zabwino, ndimawayamikira ndipo inenso ndimayesetsa kuchita zinthu zowasangalatsa. Ndikuona kuti tsopano ndine munthu wosangalala kusiyana ndi kale.”—A Karen.

      A Karen

      “Nditayamba kuphunzira Baibulo, anthu ena ankandinyoza. Koma mwamuna wanga anandilimbikitsa kuti ndipitirize. Ankandiuza kuti: ‘Zonena za anthu ine ndilibe nazo ntchito. Zimene mukuphunzirazi zikukuthandizani kukhala munthu wabwino. Musasiye kuphunzira.’ Ndikuona kuti kuphunzira Baibulo kwathandiza kuti banja lathu likhale losangalala.”—A Viniana.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena