Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Sayansi Imatithandiza Bwanji?
    Nsanja ya Olonda—2015 | June 1
    • Zimene sayansi yakwanitsa kuchita monga kupanga galimoto, GPS, masetilaiti, ndege ndi kupanga sikani ubongo

      NKHANI YA PACHIKUTO | KODI SAYANSI INGALOWE M’MALO MWA BAIBULO?

      Kodi Sayansi Imatithandiza Bwanji?

      Buku lina lotanthauzira mawu limanena kuti sayansi ndi “kufufuza zachilengedwe komanso zinthu zina pofuna kudziwa mmene zimachitikira. Pofufuzapo amayeza zinthu, kuyeserera komanso kuona zotsatira zake.” Komatu kuchita zimenezi ndi ntchito yaikulu ndi yotopetsa zedi, chifukwa nthawi zambiri pamatenga nthawi yaitali akugwira ntchitoyi. Ndipotu nthawi zina sapeza n’komwe yankho la zimene akufufuzazo. Komabe nthawi zambiri amapeza zimene akufuna kudziwazo ndipo zimakhala zothandiza kwa anthufe. Taonani zitsanzo izi.

      Kampani ina ya ku Europe inaphatikiza mapulasitiki ndi zinthu zina n’kupanga zosefera madzi. Zosefera madzizi zimathandiza kuti anthu azimwa madzi aukhondo, makamaka pakachitika mavuto ogwa mwadzidzidzi. Mwachitsanzo, zinathandiza kwambiri pa nthawi ya chivomerezi chomwe chinachitika ku Haiti mu 2010.

      Asayansi apanga chipangizo china chothandiza kudziwa mapu a dziko lonse chotchedwa GPS. Chipangizochi chimagwiritsa ntchito setilaiti ndipo chimathandiza munthu kudziwa kumene akupita. Poyamba asilikali ndi amene ankagwiritsa ntchito GPS. Koma masiku ano imagwiritsidwanso ntchito ndi oyendetsa galimoto, oyendetsa ndege, oyenda panyanja, alenje komanso okwera mapiri. Izi zikusonyeza kuti asayansi anagwira ntchito yotamandika popanga chipangizochi chifukwa n’chothandiza kwambiri.

      Ambirife timagwiritsa ntchito foni, kompyuta kapena Intaneti. Ena akafuna kupita kwinakwake amakwera ndege. Palinso anthu ambiri omwe anachira kapena kukhala ndi moyo wathanzi chifukwa cha mankhwala enaake. Zonsezi zikusonyeza kuti zimene asayansi apanga, zimatithandiza m’njira zosiyanasiyana.

      KODI SAYANSI YAFIKA PATI MASIKU ANO?

      Asayansi akufufuza chilengedwechi kuti adziwe zambiri. Ena akuyesetsa kufufuza zambiri zokhudza maatomu. Pomwe ena akufufuza zomwe zinachitika zaka mabiliyoni apitawo n’cholinga choti adziwe kuti zinthu zamoyo zinachokera kuti. Asayansi enanso afika kutali kwambiri m’mlengalenga ndipo amaona kuti Mulungu yemwe amatchulidwa m’Baibulo akanakhala kuti alipodi, bwenzi atamupeza.

      Wolemba mabuku wina dzina lake Amir D. Aczel ananena kuti “asayansi komanso afilosofi ena atafufuza kwambiri, anayamba kukayikira zoti Mulungu alipo.” Mwachitsanzo, wasayansi wina wotchuka padziko lonse ananena kuti: “Popeza sitinapeze umboni uliwonse wosonyeza kuti kuli Mulungu yemwe analenga zinthu, m’pomveka kuganiza kuti Mulunguyo kulibe.” Ena amaganiza kuti si zoona kuti kuli Mulungu wotchulidwa m’Baibulo ndipo nkhani zonena za zimene Mulungu ankachita, n’zongofuna kupusitsa anthu. Amaonanso kuti amene amakhulupirira zimenezi amangokhulupirira zamatsenga.a

      Komabe, kodi panopa asayansi akudziwa zonse zokhudza chilengedwechi moti zonse zomwe anganene zingakhale zolondola? Ayi. N’zoona kuti sayansi yapita patsogolo kwambiri, komabe asayansi ambiri amadziwa kuti padakali zinthu zambiri zomwe sakuzidziwa komanso zoti sangathe kuzidziwa. Wasayansi wina, dzina lake Steven Weinberg, anati: “Ngakhale titayesetsa bwanji, sitidzadziwa zonse.” Pulofesa wina, dzina lake Martin Rees, ananenanso kuti: “Pali zinthu zambiri zimene anthufe sitingathe kuzimvetsa.” Apa mfundo ndi yakuti, ngakhale kuti sayansi yapita patsogolo, asayansi sangatithandize kudziwa zonse. Taonani zitsanzo zotsatirazi.

      • DNA

        Asayansi samvetsa zimene zimachitika mkati mwa selo. Sakudziwa bwinobwino kuti maselo amagwiritsa ntchito bwanji mphamvu zimene amapeza kuchokera ku dzuwa, zakudya ndi zinthu zina. Sakudziwanso kuti maselowa amapanga bwanji mapuloteni komanso kuti amachulukana bwanji.

      • Mnyamata akunjanjitsa mpira

        Mphamvu yokoka ya dziko lapansi imathandiza kwambiri. Komatu asayansi sadziwa bwinobwino mmene mphamvuyi imagwirira ntchito. Mwachitsanzo, sadziwa kuti mphamvuyi imatikokera bwanji pansi tikadumpha m’mwamba. Sadziwanso mmene mphamvuyi imathandizira kuti mwezi uzizungulira dziko lapansili.

      • Chithunzi cha chilengedwe chonse

        Asayansi ena amaganiza kuti 95 peresenti ya zinthu zakuthambo ndi zinthu zosaoneka ndipo ngakhale atagwiritsa ntchito zipangizo zawo sangathe kuzitulukira. Asayansiwa sadziwanso mmene zinthu zimenezi zimagwirira ntchito.

      Wasayansi winanso wotchuka anati: “Zinthu zimene timadziwa ndi zochepa kwambiri poyerekeza ndi zimene sitidziwa. Choncho wasayansi sayenera kumangokhutira ndi zomwe amadziwa. Ineyo ndimaona kuti ukamafufuza zambiri za sayansi, m’pamene umaonanso kuti pali zambiri zomwe sudziwa.”

      Ndiyeno ngati mumaona kuti sayansi yangotsala pang’ono kulowa m’malo mwa Baibulo kapena kupangitsa anthu kuti asamakhulupirire Mulungu, mungachite bwino kuganizira mfundo iyi: Ngati akatswiri asayansi omwe ali ndi zipangizo zamphamvu kwambiri sakudziwabe zonse zokhudza chilengedwechi, kodi ndi bwino kufulumira kuganiza kuti Mulungu kulibe chifukwa choti asayansi sanapeze umboni woti alipo? Mpake kuti buku lina limanena kuti, “ngakhale kuti sayansi yapita patsogolo kwambiri, zimene tikudziwa panopa sizikusiyana kwenikweni ndi zimene akatswiri ofufuza zakuthambo akale, monga a ku Babulo, ankadziwa zaka 4,000 zapitazo. Zikuoneka kuti padakali zambiri zimene sitikuzidziwa.”—Encyclopedia Britannica.

      A Mboni za Yehova amadziwa kuti aliyense ali ndi ufulu wosankha zimene akufuna kukhulupirira pa nkhaniyi. Amachita zimenezi chifukwa amatsatira mfundo ya m’Baibulo yakuti: “Anthu onse adziwe kuti ndinu ololera.” (Afilipi 4:5) Komabe, tikukupemphani kuti muone kugwirizana kwa zimene asayansi apeza ndi zimene Baibulo limanena pa nkhani zasayansi.

      a Anthu ena sakhulupirira Baibulo chifukwa cha zimene matchalitchi ena amaphunzitsa. Matchalitchiwa amaphunzitsa kuti dziko lapansili ndiye pakati pa chilengedwe chonse komanso kuti Mulungu analenga dzikoli m’masiku 6 enieni a maola 24.—Onani bokosi lakuti, “Baibulo Silitsutsana Ndi Mfundo Zolondola Zasayansi.”

      Baibulo Silitsutsana Ndi Mfundo Zolondola Zasayansi

      N’zoona kuti Baibulo si buku lophunzitsa sayansi. Komabe, zimene anthu olemba Baibulo analemba zokhudza sayansi sizitsutsana ndi mfundo zolondola zasayansi. Taonani zitsanzo zotsatirazi.

      • Chithunzi cha chilengedwe chonse

        Kutalika kwa nthawi yomwe dziko lapansili komanso chilengedwe chonse chakhalako

        Asayansi amati dziko lapansili lakhalako zaka pafupifupi 4 biliyoni ndiponso chilengedwe chonse chakhalapo zaka 13 kapena 14 biliyoni. Baibulo silinena kutalika kwa nthawi yomwe chilengedwe chonse chakhalako. Komanso silinena kuti dziko lapansili langokhalapo zaka masauzande ochepa. Vesi loyambirira la m’Baibulo linangonena kuti: “Pa chiyambi, Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.” (Genesis 1:1) Popeza Baibulo langoti “pa chiyambi,” zimene asayansi amapeza zokhudza kutalika kwa nthawi imene dzikoli komanso chilengedwe chonse chakhalapo, sitingati n’zotsutsana ndi zimene Baibulo limanena pavesili.

      • Mapiri, zomera ndi madzi

        Mulungu sanalenge dziko lapansili m’masiku 6 enieni

        Chaputala 1 cha Genesis chimagwiritsa ntchito mawu akuti “tsiku” pofotokoza nthawi imene Mulungu anayamba kukonza dziko lapansi kuti pakhale zamoyo. Limanenanso kuti pomaliza, Mulungu analenga anthu. Baibulo silinena kuti masiku 6 amene Mulungu analenga zinthu, anali aatali bwanji. Choncho asayansi akhoza kufufuza n’kudziwa kuti nthawi imene Mulungu analenga dzikoli inali yaitali bwanji. Timadziwa kuti masiku 6 amene Mulungu analenga zinthuwa, si a maola 24 enieni.

      • Dziko lapansi

        Dziko lapansili lili m’malere

        Baibulo limanena kuti dziko lapansili lili “m’malere.” (Yobu 26:7) Baibulo silinena kuti dzikoli lili pamsana pa njovu zomwe zaima pamsana pa kamba wamkulu wa m’madzi, ngati mmene anthu ena akale ankaganizira. Komabe silinenanso chimene chimapangitsa kuti dzikoli likhale m’malere. Wasayansi wina dzina lake Nicolaus Copernicus, ndi wina dzina lake Johannes Kepler anapeza kuti pali mphamvu inayake imene imathandiza kuti mapulaneti azikhala m’malere n’kumayenda mozungulira dzuwa. Kenako wasayansi winanso, dzina lake Isaac Newton, anatulukira kuti mphamvu yokoka imathandiza kuti zinthu zonse m’mlengalenga ziziyenda mwadongosolo.

      • Mabakiteriya

        Malangizo okhudza ukhondo komanso kupewa matenda

        M’buku la Levitiko muli malangizo omwe ankathandiza Aisiraeli kupewa matenda opatsirana. Mulinso malamulo ena onena kuti munthu wodwala matenda opatsirana azikhala kwayekha. Komanso lamulo lomwe lili pa Deuteronomo 23:12, 13 linkathandiza Aisiraeli kuti azikhala aukhondo. Linkanena kuti munthu akafuna kudzithandiza, azipita kunja kwa msasa ndipo akamaliza ‘azikwirira zoipazo.’ Komatu si kale kwambiri pamene asayansi komanso madokotala anatulukira kuti malamulo amenewa ndi othandiza ndipo nawonso amalimbikitsa anthu kuti azitsatira malangizowa.

      Mfundo za m’Baibulo zimene zili m’nkhaniyizi, zinalembedwa kale kwambiri. Ndiye kodi anthu amene analemba Baibulo, anakwanitsa bwanji kulemba zolondola zokhudza sayansi, pomwe anthu ophunzira a m’nthawi yawo sankadziwa mfundo zimenezi? N’chifukwa choti anathandizidwa ndi Mulungu yemwe ndi wanzeru kuposa anthu. Mulungu amatiuza m’Baibulo kuti: “Monga momwe kumwamba kulili pamwamba kuposa dziko lapansi, momwemonso njira zanga n’zapamwamba kuposa njira zanu, ndiponso maganizo anga ndi apamwamba kuposa maganizo anu.”—Yesaya 55:9.

  • Sayansi Singatithandize Kudziwa Zonse
    Nsanja ya Olonda—2015 | June 1
    • Wasayansi ali mu labotale

      NKHANI YA PACHIKUTO | KODI SAYANSI INGALOWE M’MALO MWA BAIBULO?

      Sayansi Singatithandize Kudziwa Zonse

      Zaka zapitazi, anthu alemba mabuku ambiri ofotokoza zimene anthu omwe sakhulupirira kuti kuli Mulungu ananena. Anthu ambiri amachita chidwi ndi zimene mabukuwa amanena moti amayamba kukhala ndi maganizo osiyanasiyana pa nkhani yoti kuli Mulungu kapena ayi. Wasayansi wina dzina lake David Eagleman analemba kuti: “Anthu ena akawerenga mabukuwa . . . amaganiza kuti asayansi amadziwa zonse moti amakhulupirira kuti zimene asayansiwa anganene pa nkhani yoti kulibe Mulungu, zikhoza kukhala zoona. Koma asayansi enieni amadziwa kuti pali zinthu zambiri zomwe sanazidziwebe ndipo zimenezi zimaonekera bwino akatulukira chinthu chatsopano.”

      Katswiri wa zakuthambo akugwiritsa ntchito chipangizo choonera kutali

      Kuyambira kale kwambiri, akatswiri a sayansi akhala akufufuza kuti adziwe zambiri zokhudza chilengedwechi ndipo adabwa kwambiri ndi zimene apeza. Komabe nthawi zina zimene apeza sizikhala zolondola. Mwachitsanzo wasayansi wina, dzina lake Isaac Newton yemwe anatulukira zinthu zambiri, ankaphunzitsa kuti mphamvu yokoka imachititsa kuti mapulaneti, nyenyezi komanso magulu a nyenyezi zizikhala mwadongosolo m’mlengalenga. Anayambitsanso njira ina yosovera masamu yomwe masiku ano amagwiritsa ntchito popanga makompyuta. Asayansi amagwiritsanso ntchito masamuwa kuti adziwe mmene angayendere kupita kumapulaneti ena komanso popanga zinthu monga mabomba, magetsi ndi zina zomwe zimapangidwa pogwiritsa ntchito mphamvu ya nyukiliya. Komabe, zinthu zina zomwe Newton ankakhulupirira zinali zabodza. Mwachitsanzo ankakhulupirira kuti akhoza kugwiritsa ntchito njira zamatsenga kuti asinthe zitsulo kukhala golide.

      Zaka 1,500 Newton asanapeze zimenezi, munthu wina wa ku Greece, yemwenso anali katswiri wolemba mapu, dzina lake Ptolemy, ankafufuza zinthu za m’mlengalenga ndi maso ake. Ankachita zimenezi usiku kuti aone mapulaneti omwe ali m’mlengalenga. Ptolemy ankakhulupirira kuti dzikoli ndiye pakati pa chilengedwe chonse. Komabe wasayansi wina dzina lake Carl Sagan analemba kuti: “Anthu anakhala akukhulupirira zimene Ptolemy ankanenazi kwa zaka zoposa 1,500 koma sankadziwa kuti n’zabodza. Zimenezi zikusonyeza kuti wasayansi, ngakhale wanzeru kwambiri akhoza kupeza zinthu zomwe si zolondola.”

      Wasayansi akuwerenga Baibulo

      Masiku anonso, asayansi amalephera kudziwa bwinobwino zinthu zina zokhudza chilengedwechi ndipo amapangitsa anthu kuganiza zolakwika. N’zoona kuti masiku ano sayansi yapita patsogolo kwambiri ndipo zimene asayansi apeza zikuthandiza anthu. Komatu ndi bwino kudziwa kuti asayansi sangatithandize kudziwa zonse. Wasayansi wina dzina lake Paul Davies, anati: “Takhala tikufufuza kuti tidziwe mmene zinthu zina m’chilengedwechi zimachitikira. Koma kunena zoona zinthu zambiri n’zozunguza mutu ndipo sitingathe kufotokoza bwinobwino mmene zinthuzi zimagwirira ntchito.” Apatu mfundo ndi yakuti, anthufe sitingakwanitse kudziwa zonse zokhudza chilengedwechi. Choncho anthu ena akamati sayansi ingatithandize kudziwa zonse, si bwino kufulumira kukhulupirira zimenezo.

      Baibulo ndi lothandiza kwambiri kuposa sayansi

      Pali zinthu zambiri zimene anthufe sitingazimvetse komanso kuzidziwa. Ponena za chilengedwechi, Baibulo limati: “Zimenezi ndi kambali kakang’ono chabe ka zochita [za Mulungu], ndipo timangomva kunong’ona kwapansipansi kwa mawu ake.” (Yobu 26:14) Izi zikusonyeza kuti zimene Paulo analemba zaka 2,000 zapitazo n’zoona. Iye anati: “Ndithudi, madalitso amene Mulungu amapereka ndi ochuluka kwambiri. Nzeru zake n’zozama, ndiponso iye ndi wodziwa zinthu kwambiri. Ziweruzo zake ndi zosasanthulika, ndipo ndani angatulukire njira zake?”—Aroma 11:33.

      Malangizo Amene Asayansi Sangapereke

      N’zoona kuti asayansi amatithandiza kudziwa zambiri. Koma Baibulo lili ndi mfundo komanso malangizo omwe angatithandize kuti tizikhala osangalala komanso kuti tizikhala bwino ndi anthu. Taonani zitsanzo zotsatirazi.

      • Dzanja

        Kupewa Kuphwanya Malamulo

        Kuona kuti moyo ndi wofunika

        “Usaphe munthu.”—Ekisodo 20:13.

        “Aliyense amene amadana ndi m’bale wake ndi wopha munthu.”—1 Yohane 3:15.

        Kukhala mwamtendere ndi anthu

        “Patukani pa zinthu zoipa ndipo chitani zabwino. Funafunani mtendere ndi kuusunga.”—Salimo 34:14.

        “Chilungamo ndicho chipatso cha mbewu zimene anthu odzetsa mtendere amafesa mu mtendere.”—Yakobo 3:18.

        Kupewa zachiwawa

        “Yehova amasanthula anthu olungama ndi oipa omwe, ndipo Mulungu amadana kwambiri ndi aliyense wokonda chiwawa.”—Salimo 11:5.

        “Usasirire munthu wachiwawa, kapena kusankha njira zake. Pakuti munthu wochita zachiphamaso Yehova amanyansidwa naye.”—Miyambo 3:31, 32.

      • Banja

        Malangizo Othandiza Mabanja

        Ana azimvera makolo awo

        “Ananu, muzimvera makolo anu mwa Ambuye, pakuti kuchita zimenezi n’chilungamo. ‘Uzilemekeza bambo ako ndi mayi ako,’ ndilo lamulo loyamba lokhala ndi lonjezo: ‘Kuti zinthu zikuyendere bwino, ndiponso kuti ukhale ndi moyo wautali padziko lapansi.’”—Aefeso 6:1-3.

        Makolo aziphunzitsa bwino ana awo

        “Inunso abambo, musamapsetse mtima ana anu, koma muwalere m’malangizo a Yehova ndi kuwaphunzitsa kaganizidwe kake.”—Aefeso 6:4.

        “Inu abambo, musamakwiyitse ana anu, kuti angakhale okhumudwa.”—Akolose 3:21.

        Muzikondana ndi kulemekezana m’banja

        “Aliyense wa inu akonde mkazi wake ngati mmene amadzikondera yekha, komanso mkazi azilemekeza kwambiri mwamuna wake.”—Aefeso 5:33.

      • Mtengo

        Kusamala Zachilengedwe

        Kale anthu ena a ku Isiraeli ankawononga zinthu zosiyanasiyana. Ponena za anthu amenewa Baibulo linati: “Dzikolo laipitsidwa ndi anthu okhalamo . . . anthu okhala m’dzikolo apezeka ndi mlandu.” (Yesaya 24:5, 6) Mulungu adzaimba mlandu anthu onse amene amawononga zinthu zachilengedwe. Baibulo limati Mulungu ‘adzawononga amene akuwononga dziko lapansi.” (Chivumbulutso 11:18) Anthuwa sadzathawa ndipo adzalandira chilango cha zochita zawozo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena