Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Kukhala Oona Mtima N’kwachikale?
    Nsanja ya Olonda (Yogawira)—2016 | Na. 1
    • Bwana akuloza chala wantchito wake

      NKHANI YA PACHIKUTO | N’CHIFUKWA CHIYANI TIYENERA KUCHITA ZINTHU MOONA MTIMA?

      Kodi Kukhala Oona Mtima N’kwachikale?

      A Hitoshi ankagwira ntchito mu ofesi yowerengera ndalama m’bungwe lina loona zolemba anthu ntchito ku Japan. Tsiku lina akuona mmene ndalama zagwirira ntchito m’bungwe lawolo, abwana awo anawauza kuti alembe lipoti labodza. Koma a Hitoshi anauza abwanawo kuti sangachite zimenezo chifukwa n’zosagwirizana ndi zimene amakhulupirira. Abwanawo anawaopseza kuti awachotsa ntchito ndipo m’kupita kwa nthawi anawachotsadi.

      Kenako a Hitoshi anayamba kufufuza ntchito ina, koma anakhumudwa kwambiri chifukwa cha zomwe zinkawachitikira. Mwachitsanzo, pa nthawi ina akufunsidwa mafunso pakampani ina imene inkafuna kuwalemba ntchito, a Hitoshi ananena kuti sachita zinthu zachinyengo. Munthu yemwe ankawafunsayo anadabwa kwambiri moti anati, “Aliponso anthu otero masiku ano?” Komabe achibale ndi anzawo a a Hitoshi ankawalimbikitsa kuti asasiye kuchita zinthu mokhulupirika. Kenako a Hitoshi anayamba kukayikira ngati kuchita zimenezi kunalidi kothandiza moti anafika ponena kuti, “Kodi ndimachita bwino kuulula kuti sindichita zachinyengo chifukwa cha zimene ndimakhulupirira?”

      Zimene zinachitikira a Hitoshi zikungosonyeza kuti anthu ambiri m’dzikoli amaona kuti kuchita zachinyengo kulibe vuto lililonse. Ndipotu ena amaona kuti bizinezi yawo ingayende bwino kwambiri atamachita zachinyengo. Mayi wina wa ku South Africa anati: “Anthu ambiri amene ndimagwira nawo ntchito amachita zachinyengo moti ndimafunika kuyesetsa kuti ndisamachite nawo zimenezi.”

      Masiku ano zinthu zachinyengo zili paliponse. Mwachitsanzo, pa kafukufuku yemwe anachita katswiri wina wa maphunziro a zamaganizo pa yunivesite ya Massachusetts Amherst, dzina lake Robert S. Feldman, anapeza kuti anthu 60 pa 100 alionse amati akamacheza ndi munthu wina amakhala atanena chinachake chabodza ikamatha 10 minitsi iliyonse. A Feldman anati: “Zimene tinapezazi zinatidabwitsa kwambiri chifukwa sitinkaganiza kuti bodza ndi lofala chonchi.” N’zodabwitsa kwambiri kuti anthu amanama ngakhale kuti iwowo safuna kunamizidwa.

      Koma kodi n’chifukwa chiyani anthu ambiri masiku ano amakonda kunama, kuba komanso kuchita zinthu zina zachinyengo? Kodi kuchita zachinyengo kumabweretsa mavuto otani? Nanga kodi tingatani kuti tisamachite nawo zimenezi?

  • Kodi Chinyengo N’choopsa Bwanji?
    Nsanja ya Olonda (Yogawira)—2016 | Na. 1
    • Amayi awiri akukambirana

      NKHANI YA PACHIKUTO | N’CHIFUKWA CHIYANI TIYENERA KUCHITA ZINTHU MOONA MTIMA?

      Kodi Chinyengo N’choopsa Bwanji?

      Mayi wina wa ku South Africa, dzina lake Samantha, anati: “Mavuto ena angathe ngati utangochitako kachinyengo pang’ono.”

      Kodi mukugwirizana ndi zimene mayiyu ananena? N’zoona kuti munthu aliyense amakumana ndi mavuto amene angamuchititse kuganiza zochita chinyengo. Komano zimene timachita tikakumana ndi mavuto oterowo zimasonyeza zomwe zili mumtima mwathu. Mwachitsanzo, munthu akhoza kulolera kuchita chinyengo n’cholinga choti asagwidwe komanso asachite manyazi. Koma zoona zake zikadziwika, munthuyo amakumana ndi mavuto aakulu. Tiyeni tione mavuto amene amabwera chifukwa cha chinyengo.

      ANTHU AMASIYA KUKUKHULUPIRIRA

      Anthu akamakhulupirirana m’pamene amagwirizana kwambiri. Koma sikuti zimenezi zimangochitika lero ndi lero. Anthu amayamba kukhulupirirana akamacheza nthawi zonse n’kumauzana zakukhosi komanso kuchita zinthu moganizirana. Komabe wina akachita zachinyengo ngakhale kamodzi kokha, mnzakeyo amasiya kumukhulupirira. Ndipotu zimakhala zovuta kuti ayambirenso kukhulupirirana.

      Kodi munayamba mwanamizidwapo ndi munthu amene munkaona kuti ndi mnzanu wapamtima? Ngati ndi choncho, n’zosakayikitsa kuti munakhumudwa kwambiri. Kunena zoona chinyengo chimasokoneza mgwirizano ndiponso chibale.

      CHINYENGO CHILI NGATI MATENDA OPATSIRANA

      Pulofesa wa pa yunivesite ya California, dzina lake Robert Innes, anachita kafukufuku wina ndipo anapeza kuti “chinyengo chili ngati matenda opatsirana.” Choncho zimakhala zosavuta kuti munthu ayambe kuchita chinyengo ngati amakonda kuchita zinthu ndi munthu wachinyengo.

      Kodi mungatani kuti musamachite nawo zinthu zachinyengo? Werengani mfundo za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni.

      Zimene Anthu Achinyengo Amachita

      Amanena Bodza

      Bambo wina akuvula mphete ya ukwati

      KODI MUNTHU WABODZA AMATANI? Munthu wabodza amauza munthu wina zinthu zomwe si zoona. Nthawi zina amatha kusintha nkhani, kubisa mfundo zina, kapena kuikokomeza kwambiri.

      ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Pakuti munthu wochita zachiphamaso Yehova amanyansidwa naye, koma amakonda anthu owongoka mtima.” (Miyambo 3:32) “Popeza tsopano mwataya chinyengo, aliyense wa inu alankhule zoona kwa mnzake.”—Aefeso 4:25.

      Amanena Miseche

      Abambo awiri akunong’onezana pamene bambo wina akulowa

      KODI MUNTHU WAMISECHE AMATANI? Amanena zinthu zabodza komanso zoipa zokhudza munthu wina n’cholinga chomuipitsira mbiri.

      ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Kazitape amangokhalira kuyambitsa mikangano, ndipo wonenera anzake zoipa amalekanitsa mabwenzi apamtima.” (Miyambo 16:28) “Popanda nkhuni moto umazima, ndipo popanda munthu wonenera anzake zoipa mikangano imazilala.”—Miyambo 26:20.

      Amaba Mwachinyengo

      Munthu akuloza wotchi yomwe wabisa m’jekete

      KODI MUNTHU WAKUBA MWACHINYENGO AMATANI? Munthu wakuba mwachinyengo amanyengerera kapena kupusitsa munthu wina n’cholinga choti amubere.

      ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Usachitire chinyengo waganyu wovutika ndiponso wosauka n’kumubera.” (Deuteronomo 24:14, 15) “Wobera munthu wosauka mwachinyengo amanyoza amene anamupanga, koma wokomera mtima munthu wosauka amalemekeza amene anamupanga.”—Miyambo 14:31.

      Amaba

      Munthu akuba kachikwama ka ndalama m’chikwama cha munthu wina

      KODI MUNTHU WAKUBA AMATANI? Munthu wakuba amatenga katundu, ndalama kapena zinthu zina zomwe si zake popanda chilolezo.

      ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Wakubayo asabenso, koma agwire ntchito molimbikira. Agwire ndi manja ake ntchito yabwino, kuti akhale ndi kanthu kena kopatsa munthu wosowa.” (Aefeso 4:28) “Musasocheretsedwe. . . . Akuba, aumbombo, zidakwa, olalata, kapena olanda, onsewo sadzalowa mu ufumu wa Mulungu.”—1 Akorinto 6:9, 10.

  • Kodi Ubwino Wopewa Chinyengo Ndi Wotani?
    Nsanja ya Olonda (Yogawira)—2016 | Na. 1
    • Munthu akupereka kachikwama ka ndalama kwa mwiniwake

      NKHANI YA PACHIKUTO | N’CHIFUKWA CHIYANI TIYENERA KUCHITA ZINTHU MOONA MTIMA?

      Kodi Ubwino Wopewa Chinyengo Ndi Wotani?

      “Tikukhulupirira kuti tili ndi chikumbumtima choona, popeza tikufuna kuchita zinthu zonse moona mtima.”—Aheberi 13:18.

      M’Baibulo mawu achigiriki amene nthawi zina amamasuliridwa kuti “kuona mtima,” amatanthauza “chinthu chabwino kwambiri.” Mawuwa angatanthauzenso munthu amene amaonedwa kuti ndi wokongola chifukwa choti ali ndi khalidwe labwino.

      Akhristu amayesetsa kutsatira mawu a Paulo akuti: “Tikufuna kuchita zinthu zonse moona mtima.” Komatu kuchita zimenezi si nkhani yamasewera.

      KUPEWA CHINYENGO SI KOPHWEKA

      Anthu ambiri amakonda kudziyang’anira pagalasi tsiku lililonse. Akaona kuti penapake sipali bwino, amadzikonzakonza kuti aoneke bwino. Komabe kukhala ndi khalidwe labwino n’kofunika kwambiri kuposa kuoneka bwino kapena kutchena. Munthu akhoza kukhala wooneka bwino koma ngati alibe khalidwe, kukongolako kumakhala kopanda ntchito.

      Mawu a Mulungu amanena kuti nthawi zambiri anthufe timakhala ndi maganizo ofuna kuchita zinthu zoipa. Lemba la Genesis 8:21 limati: “Maganizo a anthu amakhala oipa kuyambira pa ubwana wawo.” Choncho kuti tisamachite zinthu zachinyengo, timafunika kulimbana ndi kamtima kameneka. Zimenezi ndi zimenenso mtumwi Paulo ankachita ndipo anafotokoza kuti: “Mumtima mwanga ndimasangalala kwambiri ndi chilamulo cha Mulungu, koma ndimaona chilamulo china m’ziwalo zanga chikumenyana ndi chilamulo cha m’maganizo mwanga n’kundipanga kukhala kapolo wa chilamulo cha uchimo chimene chili m’ziwalo zanga.”—Aroma 7:22, 23.

      Mwachitsanzo, mtima wathu ukamafuna kuchita zoipa, m’pamene maganizo ofuna kuchita zinthu mwachinyengo amakula. Zikatero tisamachite zimene mtima ukufuna koma tizilimbana ndi maganizo oipawo. Ngati munthu atamachita zimenezi akhoza kupewa kuchita zachinyengo ngakhale kuti n’zimene anthu ena amachita.

      N’ZOTHEKA KUPEWA CHINYENGO

      Kuti tipewe kuchita zachinyengo timafunika kukhala ndi malangizo abwino oti tizitsatira. N’zomvetsa chisoni kuti anthu ambiri amatha nthawi yaitali akuganizira za mmene akuonekera m’malo moganizira za khalidwe lawo. Ndiye anthu amenewa akamafuna kuchita zinazake, saona vuto kuchita zachinyengo. Buku lina linati: “Nthawi zambiri anthufe timanama n’cholinga choti ena azingotiona ngati abwino.” (The (Honest) Truth About Dishonesty) Kodi pali malangizo alionse amene angatithandize kuti tisamachite zachinyengo? Inde alipo, ndipo amapezeka m’Baibulo.

      Anthu mamiliyoni ambiri padzikoli amaona kuti Baibulo limawathandiza kuti asamachite zachinyengo. Baibulo lili ndi malangizo abwino kwambiri amene angatithandize kukhala ndi khalidwe labwino. (Salimo 19:7) Lilinso ndi malangizo omwe angatithandize m’banja, pantchito komanso popembedza Mulungu. Malangizowa satha ntchito ngakhale kuti analembedwa kalekale ndipo amathandiza anthu a mitundu yonse. Choncho kuphunzira Baibulo komanso kugwiritsa ntchito zomwe taphunzirazo kungatithandize kuti tiziyesetsa kupewa kuchita zinthu mwachinyengo.

      Komabe pali zinthu zinanso zomwe timafunika kuchita. Popeza tikukhala m’dziko limene anthu ambiri amachita zinthu zoipa, nthawi zina zimakhala zovuta kuchita zinthu zabwino. Choncho tiyenera kumapemphera kwa Yehova kuti azitithandiza. (Afilipi 4:6, 7, 13) Zimenezi zingatithandize kuti tizichita zinthu molimba mtima n’kumapewa kuchita zachinyengo.

      UBWINO WOPEWA CHINYENGO

      A Hitoshi omwe tawatchula kumayambiriro aja, amadziwika kuti ndi munthu wokhulupirika chifukwa choti sachita zinthu zachinyengo. Panopo anapeza ntchito ina ndipo abwana awo amawakonda kwambiri. A Hitoshi ananena kuti: “Ndimasangalala chifukwa ndinapeza ntchito yabwino ndipo sindidziimba mlandu.”

      Pali anthu enanso amene amasangalala chifukwa choti sachita zachinyengo. Tiyeni tione phindu limene apeza chifukwa chotsatira mfundo ya m’Baibulo yakuti, “tikufuna kuchita zinthu zonse moona mtima.”

      • Sudziimba Mlandu

        Cheryl

        Mayi wina wa ku Ireland dzina lake Cheryl anati: “Ndili ndi zaka 13 ndinasiya sukulu n’kuyamba kuba ndi anzanga enaake moti ndalama zanga zambiri zinkakhala zakuba. Nditakwatiwa, ine ndi mwamuna wanga tinayamba kuphunzira Baibulo ndi a Mboni za Yehova. Titaphunzira kuti Yehovaa amadana ndi kuchita zinthu zachinyengo, tinaganiza zosiya kuba. Ndiyeno mu 1990 tinabatizidwa n’kukhala a Mboni za Yehova.”—Miyambo 6:16-19.

        A Cheryl anapitiriza kuti: “M’nyumba mwanga munkangodzaza ndi katundu wakuba yekhayekha, koma panopo ndimasangalala chifukwa ndilibe katundu aliyense wakuba. Ndimaona kuti Yehova ndi Mulungu wachifundo kwambiri chifukwa anandilola kuti ndizimutumikira ngakhale kuti poyamba ndinkachita zinthu zoipa. Panopa ndimagona tulo tabwino chifukwa chodziwa kuti Yehova akusangalala ndi zimene ndikuchita.”

        Sonny

        Bambo wina wa ku Hong Kong, dzina lake Sonny anati: “Abwana anga atadziwa kuti ndinakana kulandira ziphuphu anandiuza kuti, ‘Mulungu wanu ndi amene amakuthandizani kukhala wokhulupirika chonchi. Pakampani pano timafuna anthu ngati inuyo.’ Kupewa kuchita zachinyengo kumandithandiza kuti ndisamadziimbe mlandu. Ndimathandizanso anthu a m’banja langa komanso anthu ena kuti asamachite zachinyengo.”

      • Umakhala Ndi Mtendere Wamumtima

        Tom

        A Tom a ku United States anati: “Ndine wachiwiri kwa bwana wamkulu kubanki ina yaikulu. Anthu ambiri omwe amagwira ntchitoyi amaona kuti munthu sangalemere ngati sachita zachinyengo. Ena mpaka amafika ponena kuti, ‘Si vuto lalikulu kuchita zachinyengo kuti upeze chuma ndipo zimathandiza kuti chuma chadziko chiziyenda bwino.’ Koma ineyo ndimakhala ndi mtendere wa mumtima chifukwa ndimayesetsa kupewa zachinyengo. Ndinatsimikiza mtima kuti sindingachite zachinyengo ngakhale zinthu zitavuta bwanji. Mabwana anganso amadziwa zimenezi ndipo ngakhale iwowo sayerekeza n’komwe kundipempha kuti ndichite zachinyengo.”

      • Anthu Amakulemekeza

        Kaori

        A Kaori a ku Japan anati: “Nthawi ina bwana wanga anandiuza kuti ndipereke lipoti labodza katundu wina atasowa, koma ine ndinamukanira. Anthu amene anaba katunduyo atadziwika, bwana wamkulu pakampani yathuyo anandithokoza kwambiri chifukwa chonena zoona. N’zoona kuti kupewa zachinyengo si kophweka. Koma anthu akadziwa kuti suchita zachinyengo, amakukhulupirira komanso kukulemekeza kwambiri.”

      M’nkhaniyi taona kuti anthu amene sachita zachinyengo sadziimba mlandu, amakhala ndi mtendere wa mumtima ndiponso anthu ena amawalemekeza. Ndiyetu tiyeni tiziyesetsa kupewa kuchita zinthu zachinyengo.

      a Baibulo limati dzina la Mulungu ndi Yehova.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena