Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ssb nyimbo 102
  • Chisangalalo cha Chiukiliro

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chisangalalo cha Chiukiliro
  • Imbirani Yehova Zitamando
  • Nkhani Yofanana
  • Mphamvu ya Chiyembekezo cha Chiukiriro
    Ogwirizana m’Kulambiridwa kwa Mulungu Yekha Wowona
  • Njira Yokhayo Yothetsera Imfa
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Mphamvu ya Chiyembekezo cha Kuuka kwa Akufa
    Lambirani Mulungu Woona Yekha
  • Kodi Mawu Akuti Sheoli ndi Hade Amatanthauza Chiyani?
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
Onani Zambiri
Imbirani Yehova Zitamando
Ssb nyimbo 102

Nyimbo 102

Chisangalalo cha Chiukiliro

(Chivumbulutso 20:13)

1. Lazaro nagona

M’manda amwala.

Alongo namlira!

Sakumudzutsa.

‘Ngati bwenzi Yesu

Akanadzatu,

Akali kudwala

Sakadafatu.’

Kumandako Yesu

Anafuula,

Kwa wakufa uja:

‘Lazaro uka!’

Nkana womangidwa

Lazaro ’namva.

Mabwezi akewo

Anakondwera!

2. Odalira Kristu

Kuwamasula,

Anamva chisoni

Pomwe anafa.

Mabwenzi a Yesu

Anamuika.

Anadzadzidwatu

Ndi chisonidi!

Komabe m’Hademo

Sanasiyidwe.

Anaukitsidwa

Ndi Mulunguyo.

Ophunzira ake

Anakondwera.

Mfungulo za imfa

Ziri ndi Kristu.

3. Tchimo la Adamu

Ladzetsa imfa;

Chiukilirocho

Chidza ndi Kristu.

Okhala mu Hade

Adzamumvatu

Nadzaukitsidwa

Nadzakondwera.

Adzaweruzidwa

Mwachilungamo

Pazochita zawo

Mu Ufumuwo.

Awo olembedwa

M’bukhu la M’lungu

Adzakhala m’dziko

Latsopanolo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena