Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ssb nyimbo 183
  • Malo a Achichepere m’Makonzedwe a Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Malo a Achichepere m’Makonzedwe a Mulungu
  • Imbirani Yehova Zitamando
  • Nkhani Yofanana
  • Khalani ndi Moyo Wopambana
    Imbirani Yehova
  • Kufufuza Anthu Okonda Mtendere
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • Kufufuza Anthu Okonda Mtendere
    Imbirani Yehova—Nyimbo Zatsopano
  • Moyo Ndi Wodabwitsa
    Imbirani Yehova
Onani Zambiri
Imbirani Yehova Zitamando
Ssb nyimbo 183

Nyimbo 183

Malo a Achichepere m’Makonzedwe a Mulungu

(Salmo 148:12, 13)

1. Onse ali n’malo m’makonzedwe a Ya.

Aitana ana ndi akulunso.

Kuyankha kwa anawo nkokondweretsa,

Polengeza za Ufumu padziko.

Umboni wawo uli wogwira mtima,

Ali audongo ndi aulemu!

Iwo ali ofunika kwa Yehova;

Kwa akulunso adzetsa chimwemwe.

2. Achichepere onsewo odziŵa Ya,

Ndichisangalalo chotani nanga!

Pomalingalira zamtsogolo mwawo

—Moyo wosathawo m’Paradaiso!

Panopo tikukhala m’zitsenderezo

Zado ngosolo limene likutha.

Timenyere nkhondo kuti tililake;

Tikhulupirike ku Ufumuwo.

3. Angapeze mabwenzi mwa anthu a Ya.

Afunirenji ubwenzi ndi dziko?

Atanganitsidwe ndi zinthu zomanga,

Adalire pamawu a Mulungu.

Mumavuto afufuze owakonda,

Kuwauza zothetsa nzeru zawo.

Koma bwenzi lawo lalikulu ndi Ya;

Adzamupeza ali wachifundo.

4. Tiri ziŵalo za mpingo Wachikristu,

Kumene Yesu agaŵira zonse.

Mokhulupirika tiime nayedi;

Tilabadire uphungu wakewo.

Tisapanikizidwetu ndi dzikoli;

Mawu a Ya ayeretse mitima.

Tonsefe tikhale okhulupirika;

Kumtamanda ndiko moyo wosatha.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena