Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ssb nyimbo 191
  • Pangani Chowonadi Kukhala Chanu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pangani Chowonadi Kukhala Chanu
  • Imbirani Yehova Zitamando
  • Nkhani Yofanana
  • Muzikonda Kwambiri Choonadi Panokha
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • Inuyo Panokha Muzikonda Kwambiri Choonadi
    Imbirani Yehova
  • “Ndidzayenda M’choonadi Chanu”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
  • ‘Pitirizani Kuyenda M’choonadi’
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2022
Onani Zambiri
Imbirani Yehova Zitamando
Ssb nyimbo 191

Nyimbo 191

Pangani Chowonadi Kukhala Chanu

(2 Akorinto 4:2)

1. Njira ya chowonadi ndiyo yabwino.

Palibe yoposa iyi.

Yesu anatiphunzitsatu kupatsa,

Kuti chimwemwe chikule.

M’khale owona.

M’sonye chikhulupiro.

Mwamakhalidwe anu inu

Mudziŵitsa cho’nadi nchanu.

2. Mwa kuika Ya poyamba ndi kumtama,

Mudzasiyana ndi dziko.

Kwa osakhulupilira nkodabwitsa

Kusankhadi chilungamo.

M’khale owona.

Siyanani ndi dziko.

Poyandikira kwa Yehova,

Mudziŵitsa cho’nadi nchanu.

3. Mdyerekezi adzayesa kutinyenga,

Koma mungathe kumtsutsa.

Chidaliro chidzakutetezerani

Ndi kupeŵa mivi yake.

M’khale owona.

Satana timamdziŵa.

Potenga zovala za M’lungu,

Mudziŵitsa cho’nadi nchanu.

4. Thupi nlofo’ka ndipo mtima ngwoipa.

Tilimbana ndi uchimo.

Tsimikizani kuti Mungagonjetse,

M’lungu ndi Mthandizi wanu.

M’khale owona.

Mukanetu zoipa.

M’kaletsa ziŵalo zathupi,

Mudziŵitsa cho’nadi nchanu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena