Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 7/99 tsamba 1
  • Pemphererani Thandizo la Yehova

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pemphererani Thandizo la Yehova
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Nkhani Yofanana
  • “Zopempha Zanu Zidziwike kwa Mulungu”
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Kodi Mapemphero Anu Amasonyeza Chiyani za Inuyo?
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Muziyamikira Mwayi Wanu wa Pemphero
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2022
  • Zimene Tingachite Kuti Mapemphero Athu Azikhala Abwino Kwambiri
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
km 7/99 tsamba 1

Pemphererani Thandizo la Yehova

1 Yesu anagogomezera ophunzira ake kufunika kwa madalitso a Yehova pa utumiki wawo. (Mat. 9:37, 38) Mapemphero athu ochokera pansi pa mtima a chitamando ndi chiyamiko pamodzi ndi kupempha moonadi ndi mapembedzero, amasonyeza kudalira kwathu konse Yehova kaamba ka thandizo lake. (Afil. 4:6, 7) Malemba amatilimbikitsa kupitirizabe kupemphera “pemphero lonse ndi pembedzero,” ndipo izi zingagwire ntchito pa mapemphero athu okhudza utumiki.—Aef. 6:18.

2 Timatamanda Yehova m’pemphero chifukwa cha mikhalidwe yake yapadera ndi zochita zake. Timamutamandanso monga Wotipatsa uthenga wabwino umene timalalika. N’gwoyenera kumutamanda chifukwa iye yekha ndi amene amapangitsa utumiki wathu kukhala wachipambano.—Sal. 127:1.

3 Mapemphero athu a chiyamiko amasonyeza kuyamikira kwathu chidziŵitso chimene Yehova watipatsa ponena za chifuno ndi cholinga chake. Kodi si mwayi kugaŵana choonadi cha Ufumu ndi ena? Timathokoza Yehova kaamba ka zonse zimene timachita mu utumiki.—Sal. 107:8; Aef. 5:20.

4 Moyenerera, timapempha thandizo kwa Yehova kuti tipeze anthu amene angavomere pempho lathu la phunziro la Baibulo ndi kuti tikhudze mitima yawo ndi choonadi. Mwa kupereka mapemphero amenewa, timatsimikiza kuti Mulungu yekha ndiye angapangitse ntchito yathu ya utumiki kukhala yobala zipatso.—1 Akor. 3:5-7.

5 Mlongo wina ankadzimva kuti mayi wina panjira yake ya magazini sanali kuŵerenga Nsanja za Olonda ndi Galamukani! Posafuna kuti magazini ofunikawa azingowonongeka, anapempha Yehova kuti ngati mayi ameneyu sanali kuwaŵerenga, asamawalandire. Mlongoyu atapitako nthaŵi ina, mwamuna wa mayiyu anati: “Zikomo kwambiri pomatibweretsera magazini amenewa nthaŵi zonse. Ndimawaŵerenga ndipo ndimawakonda kwambiri.”

6 Modzichepetsa komanso ndi mtima wonse, tingam’pemphe Yehova kuti atithandize mmene tingachitire ndi anthu amphwayi ndi onyoza komanso mmene tingagonjetsere kuopa anthu kuti tipitirizebe kuchitira umboni kwa ena molimba mtima. (Mac. 4:31) Ngati tipitirizabe kupemphera “pemphero lonse ndi pembedzero” pamene tikuchitabe utumiki wathu wopatulika mokhulupirika, tingakhale ndi chidaliro chakuti Yehova atithandiza.—1 Yoh. 3:22.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena