-
HeloKukambitsirana za m’Malemba
-
-
Koma magwero enieni a chiphunzitso chochitira chipongwe Mulungu chimenechi ngwozama kwambiri. Malingaliro auchiwanda ogwirizanitsidwa ndi helo wozunza amasinjirira Mulungu ndipo magwero ake ndiye wosinjirira wamkulu wa Mulungu (Mdyerekezi, dzina limene limatanthauza “Wosinjirira”), iye amene Yesu Kristu anamutcha “Atate wabodza.”—Yoh. 8:44.
-
-
ImfaKukambitsirana za m’Malemba
-
-
Imfa
Tanthauzo: Kulekeka kwa kugwira ntchito konse kwa moyo. Pamene kupuma, kugunda kwamtima, ndi kugwira ntchito kwa ubongo zileka, mphamvu ya moyo pang’ono ndi pang’ono imaleka kugwira ntchito m’maselo athupi. Imfa ndiyo kusiyana ndi moyo.
Kodi munthu analengedwa ndi Mulungu kuti afe?
Mosemphana ndi zimenezi, Yehova anachenjeza Adamu kusakhala wosamvera, kumene kukanatsogolera ku imfa. (Gen. 2:17) Pambuyo pake, Mulungu anachenjeza Aisrayeli motsutsana ndi kudzisungira kumene kukanatsogolera ngakhale ku imfa yamwamsanga kwa iwo. (Ezek. 18:31) M’nthaŵi yokwanira anatumiza Mwana wake kukafera anthu kotero kuti awo amene akakhulupirira m’kakonzedwe kameneka akakhale nawo moyo wosatha.—Yoh. 3:16, 36.
Salmo 90:10 limanena kuti nthaŵi yozoloŵereka ya moyo wamunthu ndiyo zaka 70 kapena 80. Zimenezo zinali zowona pamene Mose analemba, koma sizinali choncho kuyambira pachiyambi. (Yerekezerani ndi Genesis 5:3-32.) Ahebri 9:27 amati: “Popeza kwaikikatu kwa anthu kufa kamodzi.” Izinso, zinali zowona pamene zinalembedwa. Koma sizinali choncho Mulungu asanapereke chiŵeruzo pa Adamu wochimwayo.
Kodi nchifukwa ninji timakalamba ndi kufa?
Yehova analenga anthu aŵiri oyamba ali angwiro, okhala ndi chiyembekezo cha kukhala ndi moyo kosatha. Anapatsidwa ufulu wakudzisankhira. Kodi akamvera Mlengi wawo mwachikondi ndi chiyamikiro kaamba ka zonse zimene anali atawachitira? Iwo anali oti nkukhoza kotheratu kuchita choncho. Mulungu anauza Adamu kuti: “Koma mtengo wakudziŵitsa zabwino ndi zoipa usadye umenewo; chifukwa tsiku lomwe udzadye umenewo udzafa ndithu.” Mogwiritsira ntchito njoka monga cholankhulira, Satana ananyenga Hava kuswa lamulo la Yehova. Adamu sanadzudzule mkazi wake koma anagwirizana naye m’kudya chipatso choletsedwacho. Monga momwedi anali ataneneratu, Yehova anapereka chilango cha imfa pa Adamu, koma asanaphe aŵiri ochimwa amenewo, Yehova mwachifundo anawalola kubala ana.—Gen. 2:17; 3:1-19; 5:3-5; yerekezerani ndi Deuteronomo 32:4 ndi Chivumbulutso 12:9.
Aroma 5:12, 17, 19 amati: “Uchimo unaloŵa m’dziko lapansi mwa munthu mmodzi [Adamu] ndi imfa mwa uchimo; chotero imfa inafikira anthu onse, chifukwa kuti onse anachimwa. . . . Ndi kulakwa kwa mmodzi, imfa inachita ufumu . . . Monga ndi kusamvera kwa munthu mmodzi ambiri anayesedwa ochimwa.”
1 Akor. 15:22: “Mwa Adamu onse amafa.”
Wonaninso mutu waukulu wakuti “Choikidwiratu.”
Kodi nchifukwa ninji makanda amafa?
Sal. 51:5: “Wonani, ndinabadwa m’mphulupulu: ndipo mayi wanga anandilandira mu zoipa.” (Wonaninso Yobu 14:4; Genesis 8:21.)
Aroma 3:23; 6:23: “Onse anachimwa, napereŵera pa ulemerero wa Mulungu . . . Mphotho yake ya uchimo ndi imfa.”
Mulungu “samatenga” ana kwa makolo awo, monga momwe ena auzidwira. Ngakhale kuli kwakuti dziko lapansi limatulutsa chakudya chokwanira, magulu adyera andale zadziko ndi amalonda kaŵirikaŵiri amalepheretsa kugaŵiridwa kwake kwa awo ochifuna koposa, zikumachititsa imfa chifukwa cha nthenda ya kudya mosakwanira. Ana ena amafera m’ngozi, monga momwe amachitira akulu. Koma tonsefe tiri ndi choloŵa cha uchimo; tonsefe tiri opanda ungwiro. Tinabadwira m’dongosolo limene aliyense, ponse paŵiri wabwino ndi woipa—potsirizira pake amafa. (Mlal. 9:5) Koma Yehova ‘akulakalaka’ kugwirizanitsa ana ndi makolo awo kupyolera mwa chiukiriro, ndipo mwachikondi iye wapanga makonzedwe akutero.—Yoh. 5:28, 29; Yobu 14:14, 15; yerekezerani ndi Yeremiya 31:15, 16; Marko 5:40-42.
Kodi akufa ali kuti?
Gen. 3:19: “M’thukuta la nkhope yako udzadya chakudya, kufikira kuti udzabwerera kunthaka: chifukwa kuti mmenemo unatengedwa: chifukwa kuti ndiwe fumbi, ndi kufumbiko udzabwerera.”
Mlal. 9:10: “Chirichonse dzanja lako lichipeza kuchichita,
-