Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 8
  • Zimphona pa Dziko

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zimphona pa Dziko
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Angelo Ena Anaukira Mulungu
    Kodi Mizimu ya Akufa Ilipodi?
  • Mmene Angelo Amatikhudzira
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Angelo Ndiwo “Mizimu Yotumikira Anthu”
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Angelo a Mulungu Amatithandiza
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 8

NKHANI 8

Zimphona pa Dziko

NGATI wina wake analinkudza kwa inu ndipo anali wamtali mapazi 9, mofanana ndi kufika pa siling’i ya nyumba yanu, kodi mukanaganizanji? Munthu’yo akakhala chimphona! Pa nthawi ina panali’di zimphona pa dziko. Baibulo limasonyeza kuti atate ao anali angelo ochokera kumwamba. Kodi zikanatero motani?

Kumbukirani, mngelo woipa’yo Satana anali wotanganidwa kupanga bvuto. Anali kuyesa’di kuipitsa ngakhale angelo a Mulungu. M’kupita kwa nthawi, angelo ena anayamba kumumvetsera. Iwo analeka ntchito imene Mulungu anawapatsa kumwamba. Ndipo anadza pa dziko nadzipangira matupi aumunthu. Kodi mukudziwa chifukwa chake?

Baibulo limati chifukwa chakuti ana a Mulungu’wa anaona akazi okongola pa dziko nafuna kukhala nawo. Chotero anadza ku dziko nakwatira akazi’wa. Baibulo limati zimene’zi n’zolakwa, chifukwa chakuti Mulungu anapanga angelo kuti adzikhala kumwamba.

Angelo’wo ndi akazi ao atabala ana, ana’wa anali osiyana. Poyamba iwo sanaonekere kukhala osiyana kwambiri. Koma iwo anakula-kulabe, nakhala ndi mphamvu moonjezereka-onjezereka, kufikira anakhala zimphona.

Zimphona’zi zinali zoipa. Ndipo chifukwa cha kukula kwao kwambiri ndi mphamvu, zinkabvulaza anthu. Iwo anaumiriza ali yense kukhala woipa ngati iwo.

Enoke anali atafa, koma panali munthu wina pa dziko tsopano amene anali wabwino. Dzina la munthu’yu linali Nowa. Nthawi zonse anachita zimene Mulungu anafuna kuti iye achite.

Tsiku lina Mulungu anauza Nowa kuti nthawi inakwana yakuti Iye aononge anthu onse oipa. Koma iye akapulumutsa Nowa, banja lake ndi zinyama. Tiyeni tione m’mene Mulungu anachitira zimene’zi.

Genesis 6:1-8; Yuda 6.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena