Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kuloŵa Mmalo Kwautumwi
    Kukambitsirana za m’Malemba
    • Kodi pakhalapo mzera wosadukiza wa oloŵa mmalo kuyambira pa Petro kufikira kwa apapa amakono?

      M’Jesuit John McKenzie, pamene anali profesala wanthanthi zaumulungu pa Notre Dame, analemba kuti: “Palibe umboni wa m’mbiri yolembedwa umene ulipo wa mtandadza wathunthu wa kuloŵana mmalo kwa olamulira a tchalitchi.”—The Roman Catholic Church (New York, 1969), p. 4.

      New Catholic Encyclopedia ikuvomereza kuti: “ . . . kusoŵeka kwa zolembedwa kukuchititsa zambiri zokaikitsa ponena za mzera woyambirira wa oyang’anira . . . ”—(1967), Vol. I, p. 696.

      Kudzinenera kuti ngwoikidwa ndi Mulungu sikumatanthauza kanthu ngati owapanga saali omvera kwa Mulungu ndi Kristu

      Mat. 7:21-23, JB: “Saali awo onena kwa ine kuti, ‘Ambuye, Ambuye,’ amene adzaloŵa ufumu wakumwamba, koma munthu wochita chifuniro cha Atate wanga wakumwamba. Pamene tsikulo lifika ambiri adzati kwa ine, ‘Ambuye, Ambuye, kodi sitinalosere m’dzina lanu, kutulutsa ziwanda m’dzina lanu, kuchita zozizwitsa m’dzina lanu?’ Pamenepo ndidzawauza pamaso pawo: Sindinakudziweni konse inu; chokani kwa ine, anthu oipa inu!”

      Wonaninso Yeremiya 7:9-15.

      Kodi odzinenera kukhala oloŵa mmalo a atumwi amamatira ku ziphunzitso ndi ntchito za Yesu Kristu ndi atumwi ake?

      A Catholic Dictionary imati: “Tchalitchi cha Roma chiri Chautumwi, chifukwa chakuti chiphunzitso chake chiri chikhulupiriro chimene poyamba chinavumbulutsidwa kwa Atumwi, chikhulupiriro chimene chatetezera ndi kulongosola, popanda kuwonjezerako kapena kuchotsako.” (London, 1957, W. E. Addis ndi T. Arnold, p. 176) Kodi zenizeni zikuvomereza?

      Umunthu wa Mulungu

      “Utatu ali mawu ogwiritsiridwa ntchito kusonyeza chiphunzitso chachikulu cha chipembedzo Chachikristu.”—The Catholic Encyclopedia (1912), Vol. XV, p. 47.

      “Liwu lakuti Utatu, kapenanso chiphunzitso chotsimikizirika chotero, sizimawonekera m’Chipangano Chatsopano . . . Chiphunzitsocho chinayambika mwapang’onopang’ono m’kupita kwazaka mazana angapo kupyola m’mikangano yambiri.”—The New Encyclopædia Britannica (1976), Micropædia, Vol. X, p. 126.

      “Pali kuvomereza kochitidwa ndi otanthauzira ndi aphunzitsi anthanthi Zabaibulo zaumulungu, kuphatikizapo chiŵerengero chokula mosalekeza cha Aroma Katolika, kuti munthu sayenera kulankhula za chiphunzitso cha Utatu m’Chipangano Chatsopano popanda chiletso chachikulu. Palinso kuzindikiridwa kofanana kwambiri kwa olemba mbiri ponena za chiphunzitso ndi dongosolo la anthanthi kuti pamene munthu alankhula za chiphunzitso cha Utatu wosatsimikiziridwa, munthuyo wasamuka kuchoka ku nyengo ya chiyambi Chachikristu nafika, tinene kuti, ku nusu yotsirizira ya zaka za zana la 4.”—New Catholic Encyclopedia (1967), Vol. XIV, p. 295.

      Kusakwatira kwa atsogoleri achipembedzo

      Papa Paulo VI, mu kalata yake yolembera abishopo yotchedwa Sacerdotalis Caelibatus (Kusakwatira kwa Ansembe, 1967), anatchula kusakwatira monga chofunika cha atsogoleri achipembedzo, koma iye anavomereza kuti “Chipangano Chatsopano chimene chiri ndi chiphunzitso cha Kristu ndi Atumwi . . . sichimafunsira mwachindunji kusakwatira kwa aminisitala opatulika . . . Yesu Iye mwiniyo sanakupange kukhala chiyeneretso m’kusankha Kwake Khumi ndi Aŵiriwo, sanateronso Atumwi m’kusankha awo amene anatsogoza m’zitaganya Zachikristu zoyamba.”—The Papal Encyclicals 1958-1981 (Falls Church, Va.; 1981), p. 204.

      1 Akor. 9:5, NAB: “Kodi tiribe kuyenera kwa kukwatira mkazi wokhulupirira mofanana ndi otsala a atumwiwo ndi abale a Ambuye ndi Kefa?” (“Kefa” liri dzina Lachiaramu loperekedwa kwa Petro; wonani Yohane 1:42. Wonaninso Marko 1:29-31, pamene patchulidwa za mpongozi wa Simoni, kapena Petro.)

      1 Tim. 3:2, Dy: “Chifukwa chake, kuli koyenera, kuti bishopo akhale . . . mwamuna wa mkazi mmodzi [“wokwatira kamodzi kokha,” NAB].”

      Nyengo Yachikristu isanafike, Chibuddha chinafuna ansembe ake ndi mamonke kukhala osakwatira. (History of Sacerdotal Celibacy in the Christian Church, London, 1932, chotuluka chachinayi, chosindikizidwanso, Henry C. Lea, p. 6) Ngakhale poyambirirapo, malamulo apamwamba kwambiri aunsembe wa Chibabulo anali kufunikiritsa mchitidwe wa kusakwatira, mogwirizana ndi The Two Babylons lolembedwa ndi A. Hislop.—(New York, 1943), p. 219.

      1 Tim. 4:1-3, JB: “Mzimu wanena motsimikizira kuti mkati mwa nthaŵi zotsiriza mudzakhala ena amene adzachoka pa chikhulupiriro ndi kusankha kumvetsera mizimu yonyenga ndi ziphunzitso zimene zimachokera kwa ziwanda; . . . ndipo adzanena kuti ukwati ngoletsedwa.”

      Kulekana ndi dziko

      Papa Paulo VI, polankhula ku Mitundu Yogwirizana mu 1965 anati: “Anthu a padziko lapansi akutembenukira ku Mitundu Yogwirizana monga chiyembekezo chotsirizira cha chigwirizano ndi mtendere; ndi chidaliro tikupereka panopa, kudzipereka kwawo ndi kwa Ife, kwaulemu ndi chiyembekezo.”—The Pope’s Visit (New York, 1965), Time-Life Special Report, p. 26.

      Yoh: 15:19, JB: “[Yesu Kristu anati:] Ngati mukanakhala a dziko, dziko likadakukondani monga ake; koma chifukwa chakuti simuli a dziko, chifukwa chakuti kukusankhani kwanga kunakupatulani kudziko, chotero dziko likudani.”

      Yak. 4:4 JB: “Kodi simudziŵa kuti kupanga dziko kukhala bwenzi lanu kuli kupanga Mulungu kukhala mdani wanu.”

      Kutembenukira ku zida zankhondo

      Wolemba mbiri Wachikatolika E. I. Watkin akulemba kuti: “Mulimonse mmene kuvomereza kuyenera kukhalira kopweteketsa mtima, ife sitingathe kulandula kapena kunyalanyaza chenicheni cha m’mbiri ichi moyanja malangizo onyenga kapena kukhulupirika konyenga chakuti Abishopo nthaŵi zonse achirikiza nkhondo zonse zomenyedwa ndi boma ladziko lawo. Ndithudi sindikudziŵa ngakhale nyengo imodzi mu imene bungwe la abishopo lamtunduwo linatsutsa nkhondo iriyonse kukhala yosalungama . . . Chirichonse chimene chiri chiphunzitso cha lamulo chochitika chakuti ‘dziko langa nlolungama nthaŵi zonse’ chakhala mwambi wakale wotsatiridwa m’nthaŵi yankhondo ndi Abishopo a Katolika.”—Morals and Missiles (London, 1959), lolembedwa ndi Charles S. Thompson, pp. 57, 58.

      Mat. 26:52, JB: “Pamenepo Yesu anati, ‘Bwezera lupanga lako, pakuti onse osolola lupanga adzafa ndi lupanga.’”

      1 Yoh. 3:10-12, JB: “Mwanjira iyi timasiyanitsa ana a Mulungu ndi ana a mdyerekezi: yense . . . wosakonda mbale wake saali mwana Mulungu. . . . Tiyenera kukondana wina ndi mnzake; osafanana ndi Kaini, amene anali wa Woipayo nadula pakhosi mbale wake.”

      Mounikiridwa ndi zapamwambapazi, kodi awo odzinenera kukhala oloŵa mmalo atumwi aphunzitsadi ndi kuchita zimene Kristu ndi Atumwi ake anachita?

  • Kumwamba
    Kukambitsirana za m’Malemba
    • Kumwamba

      Tanthauzo: Malo okhala Yehova Mulungu ndi zolengedwa zauzimu zokhulupirika; chigawo chosawoneka ndi maso aumunthu. Baibulo limagwiritsiranso ntchito liwu lakuti “kumwamba” m’malingaliro ena osiyanasiyana; mwachitsanzo: Kuimira Mulungu mwiniyo, gulu lake la zolengedwa zauzimu zokhulupirika, malo a chiyanjo cha Mulungu, chilengedwe chakuthupi chosaphatikizapo dziko lapansi, m’mlengalenga mozungulira planetili Dziko Lapansi, maboma aumunthu otsogozedwa ndi Satana, ndi boma latsopano lolungama lakumwamba m’limene Yesu Kristu limodzi ndi oloŵa nyumba anzake apatsidwa mphamvu ndi Yehova kulamulira.

      Kodi tonsefe tinayamba takhala m’chigawo chamizimu tisanabadwe monga anthu?

      Yoh. 8:23: “[Yesu Kristu anati] Inu ndinu ochokera pansi; ine ndine wochokera kumwamba; inu ndinu a m’dziko lino lapansi; sindiri ine wa dziko lino lapansi.” (Yesu anachokera ku malo a mizimu. Koma monga momwe Yesu adanenera, anthu anewo sanatero.)

      Aroma 9:10-12: “Rebeka anakhala ndi pakati pa amapasa . . . asanabadwe, kapena asanachite kanthu kabwino kapena koipa, kuti kutsimikiza mtima kwa Mulungu monga mwa kusankha kukhale, sichifukwa cha ntchito ayi, koma chifukwa cha wakuitananiyo, chotero kunanenedwa kwa uyo, Wamkulu adzakhala kapolo wa wamng’ono.” (Ndithudi, ngati amapasa Yakobo ndi Esau anali atakhala ndi moyo kalelo m’malo a mizimu iwo akanakhaladi ndi cholembedwa chozikidwa pamkhalidwe wawo kumeneko, kodi sichoncho? Koma analibe cholembedwa chotero kufikira pambuyo pa kubadwa kwawo monga anthu.)

      Kodi anthu onse abwino amapita kumwamba?

      Mac. 2:34: “Davide [amene Baibulo limamtchula kukhala

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena