Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ssb nyimbo 49
  • Mulungu Wamkulu, Yehova!

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mulungu Wamkulu, Yehova!
  • Imbirani Yehova Zitamando
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova, Nyonga Yathu ndi Mphamvu Yathu
    Imbirani Yehova Zitamando
  • Zimene Zili M‘buku la Masalimo
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • M’patseni Yehova Ulemerero
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • O Yendani ndi Mulungu!
    Imbirani Yehova Zitamando
Onani Zambiri
Imbirani Yehova Zitamando
Ssb nyimbo 49

Nyimbo 49

Mulungu Wamkulu, Yehova!

(Salmo 95:3)

1. M’lungu Wamkulu, Wamwambamwamba,

Tikukuimbirani, Tiyenda m’njira zanu.

Ndinu Atate, Mfumu, Kalonga.

Tiri ndi mangawa nanu kosatha.

O Mulungu, ndinu wabwino ndithu.

Mutithandize kutumikira.

Tilemekezetu dzina lanulo,

ndi kutumikirabe mokhutira.

Inu ndinutu wopatsa moyo.

Munatipatsa zonse.

2. M’lungu Wamkulu, Wamphamvuyonse,

Tikondwa m’ntchito yanu, Pochita ntchito yathu.

Mulitu Nsanja, Mphamvu yathudi.

Tikudalirani ndi mtima wonse.

O Mulungu, ndinu wachikondidi.

M’katithandiza sitidzalakwa.

Tiumirire ku zifuno zanu

Ndi kutumikira inu, nokhanu.

Mulitu linga, Chikopa chathu.

Timakudalirani.

3. M’lungu Wamkulu, Mbusa, Mlangizi,

Mumatiyang’anira, Mumatidera nkhaŵa.

Mpulumutsidi, Ndi woombola.

Tingadze kwa inu mumapemphero.

O Mulungu, ndinu wokoma mtima.

Titonthozedwa moyenerera.

Timalemekeza dzina lanulo

Mudzakhala monga momwe mufuna.

Mbuye Yehova, Palibe wina,

kusiyapo nokhanu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena