-
Mawu Oyambirira Ogwiritsira Ntchito mu Uminisitala WakumundaKukambitsirana za m’Malemba
-
-
PAMENE ANTHU AMBIRI ANENA KUTI: ‘NDIRI WOTANGANITSIDWA’
● ‘Moni. Tikuchezera munthu aliyense m’chigawo chino ndi uthenga wofunika. Mosakaikira inu muli munthu wotanganitsidwa, chotero ndidzalankhula mwachidule.’
● ‘Moni. Dzina langa ndine——. Chifuno cha kufika kwanga ndicho kukambitsirana nanu madalitso a Ufumu wa Mulungu ndi mmene tingawalandirire. Koma ndingathe kuwona kuti muli wotanganitsidwa (kapena, muli pafupi kuchoka). Kodi ndingakusiireni mfundo yachidule chabe?’
M’GAWO LOFOLEDWA KAŴIRIKAŴIRI
● ‘Ndiri wokondwa kukupezani panyumba. Tikuchita kucheza kwathu kwamlungu ndi mlungu m’chitaganya chino, ndipo tiri ndi kanthu kena koti tigaŵane nanu ponena za zinthu zabwino kwambiri zimene Ufumu wa Mulungu udzachitira anthu.’
● ‘Moni. Nkokondweretsa kukuwonaninso. . . . Kodi aliyense m’banja ali bwino? . . . Ndaima pano kugaŵana nanu mfundo yonena za . . . ’
● ‘Moni. Muli bwanji? . . . Ndakhala ndikufunafuna mpata wina wa kulankhula nanu. (Ndiyeno tchulani nkhani yeniyeni imene mukufuna kulankhula.)’
-
-
Mmene Mungayankhire Oyembekezera Kuimitsa KukambitsiranaKukambitsirana za m’Malemba
-
-
Mmene Mungayankhire Oyembekezera Kuimitsa Kukambitsirana
Ndemanga: Ziyembekezo za moyo wa anthu zimadalira pamkhalidwe wawo kulinga kwa Yehova Mulungu ndi Ufumu wake mwa Kristu Yesu. Uthenga wa Ufumu wa Mulungu ngwochititsa chidwi, ndipo umasonya ku chiyembekezo chokha chodalirika cha anthu. Ndiwo uthenga umene umasanduliza miyoyo. Timafuna kuti aliyense aumve. Timazindikira kuti ochepekera okha adzaulandira molabadira, koma tidziŵa kuti anthu ngofunikiradi kuumva ngati iwo ati apange chosankha chotsimikizirika. Komabe siyense amene ali wofunitsitsa kumvetsera, ndipo ife sitimayesayesa kuwakakamiza. Koma kaŵirikaŵiri mwaluso kuli kotheka kusanduliza oyembekezera kuimitsa kukambitsirana kukhala mwaŵi wa kukambitsirana kowonjezereka. Pano pali zitsanzo za zimene Mboni zachidziŵitso zagwiritsira ntchito m’zoyesayesa zawo za kufunafuna anthu oyenerera. (Mat. 10:11) Ife sitikuvomereza kuti muloŵeze pamtima alionse amayankho ameneŵa koma kuti muloŵetse lingalirolo m’maganizo, liikeni m’mawu a inu mwini ndi kulinena mwanjira imene imasonyeza chikondwerero chanu chowona mtima mwa munthu amene mukulankhula naye. Pamene mukutero, mungathe kukhala ndi chidaliro chakuti awo amene ali ndi mitima yolungama adzamvetsera ndi kuyankha molabadira ku zimene Yehova akuchita kuwakokera ku makonzedwe ake achikondi a moyo.—Yoh. 6:44; Mac. 16:14.
‘SINDIRI WOKONDWERERA’
● ‘Ndikufunseni, Kodi mukutanthauza kuti simuli wokondwerera Baibulo kapena ndicho chipembedzo chonse chimene simuli wokondwera nacho? Ndikufunsa motero chifukwa chakuti takumana ndi ambiri amene panthaŵi zina anali achipembedzo koma amene saali kupitanso kutchalitchi chifukwa chakuti amawona chinyengo m’matchalitchi (kapena, iwo akulingalira kuti chipembedzo ndicho bizinesi lina lopangira ndalama; kapena, iwo samavomereza kuloŵerera kwa chipembedzo m’ndale zadziko; ndi zina zotero). Baibulo nalonso silimavomereza zizoloŵezi zotero ndipo limatipatsa maziko okha oyang’anira mtsogolo ndi chidaliro.’
● ‘Ngati mutanthauza kuti simuli wokondwera ndi chipembedzo china, ndingathe kumvetsetsa zimenezo. Koma mwachiwonekere kwambiri muli wokondwera ndi mtundu wamtsogolo mmene tingathe kuyembekezera chifukwa cha chiwopsezo cha nkhondo yanyukliya (kapena, mmene tingatetezerere ana athu ku kugwiritsira ntchito molakwa anamgoneka; kapena, zimene zingachitidwe ponena za upandu kotero kuti sitidzafunikira kuchita mantha kuyenda m’makwalala; ndi zina zotero). Kodi mungathe kuwona chiyembekezo chirichonse cha njira yeniyeni yothetsera?’
● ‘Kodi chiri chifukwa chakuti muli kale ndi chipembedzo? . . . Tandiuzani, Kodi muganiza kuti tidzawona nthaŵi pamene munthu aliyense adzakhala wa chipembedzo chimodzimodzi? . . . Kodi nchiyani chimene chikuwonekera kukhala chopinga? . . . Kuti icho chikhale chopereka tanthauzo, kodi ndimaziko amtundu wotani amene akafunika?’
● ‘Ndingathe kuzindikira zimenezo. Zaka zoŵerengeka zapitazo ndinalingalira mwanjira yofananayo. Koma ndinaŵerenga kanthu kena m’Baibulo kamene kanandithandiza kuwona zinthu mosiyana. (Sonyezani munthuyo zimene kanthuko kanali.)’
● ‘Kodi mungakondwere ngati nditakusonyezani kuchokera m’Baibulo mmene mukanawonera akufa anu okondedwa kachiŵirinso (kapena, chimene kwenikweni chiri chifuno cha moyo; kapena, mmene lingatithandizire kusunga mabanja athu ali ogwirizana; ndi zina zotero)?’
● ‘Ngati mutanthauza kuti simuli wokondwera kugula kanthu kena, tandilolani kumasula maganizo anu. Ine sindikuchita ntchito yotsatsa malonda. Koma kodi mukakondwerera mwaŵi wakukhala ndi moyo padziko lapansi la paradaiso, lopanda matenda ndi upandu, limodzi ndi anansi amene kwenikweni amakukondani?’
● ‘Kodi limenelo ndilo yankho lanu lanthaŵi zonse pamene Mboni za Yehova zikufikirani? . . . Kodi kwenikweni munayamba mwadabwa chifukwa chake timapitirizabe kufika kapena zimene timanena? . . . Mwachidule, chifukwa chimene ndadzakuwonerani chiri chakuti ndimadziŵa kanthu kena kamene inunso muyenera kudziŵa. Bwanji osamvetsera kamodzi kokha kano?’
‘SINDIRI WOKONDWERA NDI CHIPEMBEDZO’
● ‘Ndingathe kumvetsetsa mmene mukulingalirira. Mosabisa mawu, matchalitchi sakupanga dziko lino kukhala malo otetezereka kwambiri a
-