Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kupirira Kuli ndi Mphoto Yake
    Utumiki wa Ufumu—2004 | August
    • Kupirira Kuli ndi Mphoto Yake

      1 “Mudzakhala nawo moyo wanu m’chipiriro.” (Luka 21:19) Mawu ameneŵa amene ndi mbali ya ulosi umene Yesu ananena wokhudza “mathedwe a nthaŵi ya pansi pano,” amasonyeza bwino lomwe kuti pamene tikukhala okhulupirika, tiyeneranso kukhala okonzekera kukumana ndi ziyeso. Koma mwa mphamvu ya Yehova, aliyense wa ife akhoza ‘kulimbika chilimbikire kufikira chimaliziro’ ndi ‘kupulumuka.’—Mat. 24:3, 13; Afil. 4:13.

      2 Zinthu zingakhale zovuta tsiku lililonse chifukwa cha chizunzo, matenda, mavuto a zachuma, ndi kuvutika maganizo. Komabe, tisaiwale kuti Satana akuyesetsa kuwononga chikhulupiriro chathu mwa Yehova. Tsiku lililonse limene takhulupirika kwa Atate wathu, timakhala titathandizira kupereka yankho kwa Wotonza ameneyo. N’zolimbikitsa kwambiri kudziŵa kuti “misozi” imene timagwetsa pokumana ndi mavuto siiŵalika! Yehova amaiona kukhala yamtengo wapatali, ndipo kukhulupirika kwathu kumasangalatsa mtima wake!—Sal. 56:8; Miy. 27:11.

      3 Ziyeso Zimatiyenga: Mavuto angavumbule mbali inayake imene sili bwino pa chikhulupiriro chathu kapena pa umunthu wathu, monga kunyada kapena kusaleza mtima. M’malo moyesa kuzemba kapena kuthetsa ziyeso potsata njira zomwe si za m’malemba, tifunika kumvera langizo la Mawu a Mulungu lakuti “chipiriro chikhale nayo ntchito yake yangwiro.” Chifukwa chiyani? Chifukwa chakuti kupirira ziyeso mokhulupirika kumatithandiza ‘kukhala angwiro ndi opanda chilema.’ (Yak. 1:2-4) Kupirira kungatithandize kukhala ndi makhalidwe ena ofunika, monga kulolera, kuganizira ena ndiponso chifundo.—Aroma 12:15.

      4 Chikhulupiriro Choyesedwa: Tikapirira ziyeso, timakhala ndi chikhulupiriro choyesedwa chimene chili chamtengo wapatali pamaso pa Mulungu. (1 Pet. 1:6, 7) Chikhulupiriro chotero chimatithandiza kuti tidzakhale olimba pamene tidzakumana ndi ziyeso zina m’tsogolo. Kuwonjezera pamenepo, timatha kuona kuti Mulungu akutiyanja, ndipo zimenezi zimalimbitsa chiyembekezo chathu. Chiyembekezo chathu chikalimba, chimakhala chodalirika kwambiri.—Aroma 5:3-5.

      5 Mphoto yaikulu ya kupirira yalembedwa pa Yakobo 1:12, pamene pamati: “Wodala munthu wakupirira poyesedwa; pakuti pamene wavomerezeka, adzalandira korona wa moyo.” Ndiyetu, tiyeni tikhalebe olimba pa kudzipereka kwathu kwa Yehova, podziŵa kuti adzapereka mphoto yaikulu kwa “akum’konda Iye.”

  • Kuchititsa Maphunziro a Baibulo Opita Patsogolo Gawo 2:
    Utumiki wa Ufumu—2004 | August
    • Kuchititsa Maphunziro a Baibulo Opita Patsogolo​—Gawo 2:

      Kukonzekera Kuchititsa Phunziro

      1 Kuphunzitsa kogwira mtima pochititsa phunziro la Baibulo kumafuna zambiri m’malo mongokambirana nkhaniyo ndi kuŵerenga malemba amene sanagwidwe mawu. Pophunzitsa, tiyenera kum’fika pamtima wophunzira wathu. Zimenezi zimafuna kuti tizikonzekera mokwanira bwino ndiponso tiziganiza za wophunzira wathuyo pamene tikukonzekera.—Miy. 15:28.

      2 Mmene Mungakonzekerere: Choyamba, pempherani kwa Yehova za wophunzira wanu ndi zosoŵa zake. M’pempheni Yehova kuti akuthandizeni kum’fika pamtima wophunzira wanu. (Akol. 1:9, 10) Kuti mumvetsetse bwino kwambiri mfundo yaikulu ya nkhani imene mukaphunzire, ganizani kaye za mutu wa nkhaniyo, timitu take , ndi zithunzi zake. Dzifunseni kuti, ‘Kodi cholinga chake cha nkhaniyi n’chiyani?’ Zimenezi zidzakuthandizani kuti pokachititsa phunzirolo, mukatsindike mfundo zake zazikulu.

      3 Mosamalitsa, ŵerengani nkhaniyo ndime ndi ndime. Pezani mayankho a mafunso amene aperekedwa, ndi kudula mzera kunsi kwa mawu okhawo amene ali ofunikira kwambiri. Ŵerengani malemba osagwidwa mawu ndi kuona mmene akugwirizanirana ndi mfundo yaikulu m’ndimeyo, ndipo sankhani amene mukaŵerenge pochititsa phunzirolo. Zimathandizanso kulemba timawu tochepa m’mphepete mwa tsamba la buku lanulo tofotokozera malembawo. Wophunzira wanu azitha kuona kuti zimene akuphunzira zilidi zochokera m’Mawu a Mulungu.—1 Ates. 2:13.

      4 Gwirizanitsani Nkhaniyo ndi Zosoŵa Zake: Kenako, ganizirani za mmene nkhani imeneyo ikukhudzira wophunzira wanuyo. Yesani kupeza mafunso amene wophunzira wanu akhoza kukafunsa ndi mfundo zina zimene zingam’vute kuti azimvetsetse kapena kuti azivomereze. Dzifunseni kuti: ‘Kodi n’chiyani chimene afunika kumvetsetsa kapena kuwongolera kuti apite patsogolo mwauzimu? Kodi ndingam’fike bwanji pamtima? Ndiyeno konzani kaphunzitsidwe kanu kuti kagwirizane ndi zimene mwapezazo. Nthaŵi zina, mungaone kuti m’pofunika kukonza fanizo, kumveketsa bwinobwino mfundo inayake, kapena kukafunsa mafunso angapo kuti mukam’thandize wophunzirayo kumvetsa zimene mfundo inayake kapena lemba likutanthauza. (Neh. 8:8) Koma peŵani kuphatikizapo mfundo zina zimene sizikugwirizana kwenikweni ndi nkhaniyo. Pomaliza phunzirolo, bwereranimo mwachidule m’nkhaniyo kuti muthandize wophunzirayo kukumbukira mfundo zazikulu.

      5 Timasangalala kwambiri atsopano akayamba kubereka zipatso zolungama zolemekeza Yehova! ( Afil. 1:11) Kuti muwathandize kufika pamenepo, muzikonzekera mokwanira bwino nthaŵi iliyonse pamene mukukachititsa phunziro la Baibulo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena