Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • sn nyimbo 68
  • Pemphero la Munthu Wovutika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pemphero la Munthu Wovutika
  • Imbirani Yehova
  • Nkhani Yofanana
  • Pemphero la Munthu Wovutika
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • Mulungu Imvani Pemphero Langa
    Imbirani Yehova
  • Imvani Pemphero Langa
    Imbirani Yehova Mosangalala
  • Ndithandizeni Ndikhale Wolimba Mtima
    Imbirani Yehova Mosangalala
Onani Zambiri
Imbirani Yehova
sn nyimbo 68

Nyimbo 68

Pemphero la Munthu Wovutika

Losindikizidwa

(Salimo 4:1)

1. Yehova ndapempha:

“Imvani pemphero langa.”

Zilonda zanga zakula

Sizipola msanga.

Kuvutika ndi maganizo

Kwandifoola.

Ndikomereni mtima

Mulungu wotonthoza.

(KOLASI)

Ndidzutseni. Ndichizeni

Nkhawa zanga zichotseni.

Pa mavuto n’thandizeni,

Yehova ndilimbitseni.

2. Ndikafo’ka

Mawu anu amanditonthoza

Kwambiri,

Moti sindingathe kufotokoza.

Ndidziwe kuti,

Chikondi chanu ndi chosatha

Ndiponso n’chachikulu

Kuposa mtima wanga.

(KOLASI)

Ndidzutseni. Ndichizeni

Nkhawa zanga zichotseni.

Pa mavuto n’thandizeni,

Yehova ndilimbitseni.

(Onaninso Sal. 42:6; 119:28; 2 Akor. 4:16; 1 Yoh. 3:20.)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena