CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | EZARA 1-5
Yehova Amakwaniritsa Malonjezo Ake
Losindikizidwa
Yehova analonjeza kuti adzabwezeretsa kulambira koona mu Yerusalemu. Koma anthu atamasulidwa ku ukapolo wa ku Babulo, panali mavuto ambiri. Panalinso lamulo loletsa ntchito yomanga malo olambirira moti ambiri ankaganiza kuti ntchitoyo sadzaimaliza.
c. 537 B.C.E.
Koresi analamula kuti kachisi amangidwenso
-
Mwezi wa 7
Guwa linakonzedwa ndipo nsembe zinaperekedwa
-
536 B.C.E.
Maziko anamangidwa
-
522 B.C.E.
Mfumu Aritasasita inaimitsa ntchito yomanga
-
520 B.C.E.
Zekariya ndi Hagai analimbikitsa anthu kuti ayambirenso kumanga
-
515 B.C.E.
Ntchito yomanga kachisi inamalizidwa