-
Dziko Lapansi Lidzakhalanso ParadaisoKodi Baibulo Lili Ndi Uthenga Wotani?
-
-
GAWO 26
Dziko Lapansi Lidzakhalanso Paradaiso
Kudzera mu Ufumu wa Khristu, Yehova adzayeretsa dzina lake, adzasonyeza kuti iye yekha ndi woyenera kulamulira ndiponso adzathetsa mavuto onse
BUKU la Chivumbulutso, lomwe ndi lomaliza m’Baibulo, lili ndi uthenga wothandiza anthu onse kukhala ndi chiyembekezo. Mtumwi Yohane ndi amene analemba bukuli ndipo muli masomphenya ambiri amene akusonyeza mmene chifuniro cha Yehova chidzakwaniritsidwire.
M’masomphenya oyamba, Yesu amene anali ataukitsidwa anapereka malangizo kumipingo ingapo ndiponso anaiyamikira. Masomphenya otsatira amasonyeza mpando wachifumu wa Mulungu kumwamba, kumene angelo akumutamanda.
Pamene chifuniro cha Mulungu chinapitiriza kukwaniritsidwa, Mwanawankhosa amene ndi Yesu Khristu, analandira mipukutu 7 yokhala ndi zidindo. Pamene zidindo zinamatulidwa pamipukutu inayi yoyambirira, anthu anayi okwera pamahatchi ophiphiritsa anaonekera padziko lapansi. Munthu woyamba anali Yesu, atavala chisoti chachifumu ndipo anakwera pahatchi yoyera. Kenako anthu enawo anaonekera atakwera pamahatchi a mitundu yosiyanasiyana ndipo akuimira nkhondo, njala ndiponso miliri. Zinthu zonsezi zikuchitika m’masiku otsiriza a dziko loipali. Chidindo cha 7 chitamatulidwa, malipenga 7 ophiphiritsa anaimbidwa ndipo zimenezi zinalengeza kuperekedwa kwa chiweruzo cha Mulungu. Kenako kunachitika miliri 7 yophiphiritsa imene inasonyeza mkwiyo wa Mulungu.
Ufumu wa Mulungu, womwe m’masomphenyawa uli ngati mwana wakhanda wamwamuna, unakhazikitsidwa kumwamba. Kenako nkhondo inayambika ndipo Satana ndi angelo ake oipa anaponyedwa padziko lapansi ndipo panamveka mawu amphamvu akuti: “Tsoka dziko lapansi.” Mdyerekezi ali ndi mkwiyo waukulu chifukwa akudziwa kuti wangotsala ndi kanthawi kochepa.—Chivumbulutso 12:12.
Yohane anaona Yesu ali kumwamba ndipo ankaoneka ngati mwana wa nkhosa. Kumwambako anali limodzi ndi anthu okwana 144,000 osankhidwa pakati pa anthu. Anthu amenewa “adzalamulira monga mafumu limodzi” ndi Yesu. Choncho buku la Chivumbulutso limasonyeza kuti mbali yachiwiri ya mbewu yolonjezedwa inapangidwa ndi anthu okwana 144,000.—Chivumbulutso 14:1; 20:6.
Masomphenyawa akusonyeza kuti olamulira osiyanasiyana a dziko lapansi adzasonkhana “kunkhondo ya tsiku lalikulu la Mulungu Wamphamvuyonse,” yotchedwa Aramagedo. Iwo adzamenya nkhondo polimbana ndi Yesu amene anakwera hatchi yoyera uja. Pa nkhondoyi, iye adzatsogolera magulu ankhondo akumwamba. Atsogoleri onse a dzikoli adzawonongedwa, Satana adzamangidwa ndipo Yesu ndi anthu 144,000 aja adzayamba kulamulira dziko lapansi kwa “zaka 1,000.” Zaka zimenezi zikadzatha, Satana adzawonongedwa.—Chivumbulutso 16:14; 20:4.
Kodi Ulamuliro wa Zaka 1,000 wa Khristu ndi olamulira anzake udzachita zotani kwa anthu okhulupirika? Yohane analemba kuti: “[Yehova] adzapukuta misozi yonse m’maso mwawo, ndipo imfa sidzakhalaponso. Sipadzakhalanso kulira, kapena kubuula, ngakhale kupweteka. Zakalezo zapita.” (Chivumbulutso 21:4) Dziko lonse lapansi lidzakhala paradaiso.
Choncho, buku la Chivumbulutso limamaliza bwino uthenga wa m’Baibulo. Kudzera mwa Ufumu wa Mesiya, dzina la Yehova lidzayeretsedwa ndipo zidzaonekeratu kuti iye yekha ndi woyenera kulamulira mpaka muyaya.
—Nkhaniyi yachokera m’buku la Chivumbulutso.
-
-
Onani Uthenga wa M’Baibulo—MwachiduleKodi Baibulo Lili Ndi Uthenga Wotani?
-
-
Onani Uthenga wa M’Baibulo
Yehova analenga Adamu ndi Hava kuti akhale ndi moyo wosatha m’Paradaiso. Satana anaipitsa dzina la Mulungu ndipo anasonyeza kuti Mulungu siwoyenera kulamulira. Adamu ndi Hava anagwirizana ndi Satana pogalukira Mulungu ndipo zimenezi zinachititsa kuti iwowo ndiponso ana amene anabereka akhale ochimwa ndiponso ayambe kufa
Yehova anaweruza ochimwawo ndipo analonjeza kuti kudzabwera Mpulumutsi, kapena kuti Mbewu, amene adzaphwanya Satana ndi kuchotsa mavuto onse amene anabwera chifukwa cha kugalukira ndi kuchimwa kumene kunachitikako
Yehova analonjeza Abulahamu ndi Davide kuti adzakhala makolo a Mbewu kapena kuti Mesiya, amene adzalamulire monga Mfumu kwamuyaya
Yehova anauza aneneri kuti alosere zoti Mesiya adzathetsa uchimo ndi imfa. Monga Mfumu, Mesiyayo limodzi ndi olamulira anzake, adzalamulira mu Ufumu wa Mulungu umene udzathetse nkhondo, matenda ngakhalenso imfa
Yehova anatumiza Mwana wake padziko lapansi ndipo anam’dziwikitsa kuti ndi Mesiya. Yesu analalikira za Ufumu wa Mulungu ndipo anapereka moyo wake monga nsembe. Kenako Yehova anamuukitsa monga mzimu
Yehova anaika Mwana wake kukhala Mfumu kumwamba ndipo chimenechi chinali chiyambi cha masiku otsiriza a dziko loipali. Yesu amatsogolera otsatira ake akamalalikira za Ufumu wa Mulungu padziko lonse lapansi
Yehova adzalamula Mwana wake kuti Ufumu wake uyambenso kulamulira padziko lapansi. Ufumuwu udzaphwanya maboma onse oipa, udzabweretsa Paradaiso, komanso mu ufumuwu, anthu onse okhulupirika adzakhala angwiro. Pa nthawiyi, zidzadziwika kuti Yehova ndiye woyenera kulamulira ndipo dzina lake lidzayeretsedwa mpaka muyaya
-