Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • th phunziro 7 tsamba 10
  • Kulankhula Zoona Komanso Zofika Pamtima

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kulankhula Zoona Komanso Zofika Pamtima
  • Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
  • Nkhani Yofanana
  • Kunena Zoona Zokhazokha
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Kunena Mawu Oyenera Musanayambe Kuwerenga Lemba
    Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
  • Kusonyeza Kuti Nkhaniyo Ndi Yothandiza
    Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
  • Kugwiritsa Ntchito Mafunso
    Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
Onani Zambiri
Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
th phunziro 7 tsamba 10

PHUNZIRO 7

Kulankhula Zoona Komanso Zofika Pamtima

Lemba

Luka 1:3

MFUNDO YAIKULU: Muzigwiritsa ntchito maumboni odalirika kuti anthu amene mukukambirana nawo adziwe zoona.

MMENE MUNGACHITIRE:

  • Muzigwiritsa ntchito maumboni odalirika. Zolankhula zanu zizikhala zochokera m’Mawu a Mulungu ndipo ngati n’zotheka muzichita kuwerenga m’Baibulo. Ngati mukufuna kupereka umboni wochokera kwa asayansi, nyuzi, kapena zinthu zina muzitsimikizira kuti n’zodalirika komanso zolondola.

  • Muzigwiritsa ntchito bwino maumboniwo. Zimene mukufotokoza pa lemba zizikhala zogwirizana ndi nkhani yonse ya lembalo, Baibulo lonse komanso zimene “kapolo wokhulupirika ndi wanzeru” wafalitsa. (Mat. 24:45) Ngati mukugwiritsa ntchito umboni wina muzionetsetsa kuti ukugwirizana ndi nkhani yonse komanso cholinga cha wolembayo.

    Mfundo yothandiza

    Musamakokomeze mfundo kapena kuwonjezera manambala. Mwachitsanzo mawu oti “anthu ena” musawasinthanitse ndi oti “anthu ambiri.” Mawu oti “nthawi zina” musawasinthanitse ndi oti “nthawi zambiri” komanso mawu oti “n’kutheka kuti” musawasinthanitse ndi oti “zikuoneka kuti.”

  • Fotokozani m’njira yogwira mtima. Mukawerenga lemba kapena kutchula umboni winawake, muzifunsa mafunso abwino kapena kupereka chitsanzo chothandiza anthu kuzindikira zimene mukutanthauza.

MU UTUMIKI

Mukamakonzekera utumiki muziganizira mafunso amene anthu angakufunseni n’kufufuziratu mayankho ake. Ngati simukudziwa yankho la funso limene mwafunsidwa, muzipempha kuti mukafufuze kaye kenako n’kudzabwererako kukayankha.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena