Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb19 October tsamba 5
  • Munthu Akhoza Kusintha Akaona Ulemu Komanso Khalidwe Lanu Labwino

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Munthu Akhoza Kusintha Akaona Ulemu Komanso Khalidwe Lanu Labwino
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
  • Nkhani Yofanana
  • Muzilemekeza Mwamuna Kapena Mkazi Wanu
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Muzidalira Kwambiri Mulungu
    Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala
  • Muzikhala Okhulupirika
    Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala
  • Zimene Mungachite Kuti Muzigwirizana ndi Achibale
    Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
mwb19 October tsamba 5

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Munthu Akhoza Kusintha Akaona Ulemu Komanso Khalidwe Lanu Labwino

Nthawi zambiri, akazi okwatiwa akamasonyeza makhalidwe abwino amathandiza amuna awo kuti ayambe kutumikira Yehova. Koma kuti alongowa achite zimenezi amafunika kupirira kwa zaka zambiri. (1 Pet. 2:21-23; 3:1, 2) Ngati mwamuna wanu amakuponderezani, muyenera kupitirizabe kugonjetsa choipa pochita chabwino. (Aroma 12:21) N’kutheka kuti mwamuna wanu sangamvetsere mukamamuuza za Yehova. Komabe akaona khalidwe lanu labwino, akhoza kukopeka n’kuyamba kuphunzira.

Muziyesetsa kumvetsa zimene zikuchititsa mnzanuyo kuchita zinthu mwa njira inayake. (Afil. 2:3, 4) Muzichita zinthu mokoma mtima komanso muziyesetsa kukwaniritsa udindo wanu. Muzimumvetsera akamafotokoza maganizo ake. (Yak. 1:19) Muzikhala oleza mtima ndipo muzimutsimikizira kuti mumamukonda kwambiri. Ngakhale zitaoneka kuti mnzanuyo sayamikira zimene mumamuchitira, muzikumbukira kuti Yehova amasangalala akamaona kukhulupirika kwanu.​—1 Pet. 2:19, 20.

ONERANI VIDIYO YAKUTI YEHOVA AMATILIMBIKITSA KUTI TITHE KULIMBANA NDI MAVUTO ATHU, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi zinthu zinali bwanji a Grace Li atangolowa m’banja?

  • N’chiyani chinachititsa kuti ayambe kuphunzira Baibulo?

  • Kodi Mlongo Li anakumana ndi mavuto otani atangobatizidwa?

  • Kodi Mlongo Li ankapempha chiyani kwa Yehova zokhudza mwamuna wake?

  • Kodi Mlongo Li anadalitsidwa bwanji chifukwa cholemekeza kwambiri mwamuna wake komanso kusonyeza khalidwe labwino?

Zithunzi zochokera m’vidiyo yakuti  Yehova Amatilimbikitsa Kuti Tithe Kulimbana ndi Mavuto Athu, zosonyeza moyo wa a Grace Li. 1. A Grace akulira. 2. Mlongo akuphunzira Baibulo ndi a Grace Li. 3. A Grace ndi ana awo akutuluka mu lesitilanti yawo popita ku misonkhano. 4. A Grace ndi anthu 9 a m’banja mwawo ali ku Nyumba ya Ufumu.

Ulemu komanso khalidwe lanu labwino zikhoza kusintha mtima wa mwamuna wanu!

Kuchita zinthu mwaulemu komanso kusonyeza khalidwe labwino kungathandizenso ngati mwamuna wanu, amene ndi wobatizidwa, sakutsogolera banja lanu pa zinthu zauzimu. Onerani vidiyo yakuti, Khalidwe Lanu Lingalimbikitse Mwamuna Wanu.

Mlongo akuyang’ana mwamuna wake yemwe anasiya kusonkhana
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena