Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • th phunziro 1 tsamba 4
  • Mawu Oyamba Abwino

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mawu Oyamba Abwino
  • Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
  • Nkhani Yofanana
  • Mawu Oyamba Ogwira Mtima
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Mawu Oyamba Okopa Chidwi
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Kusonyeza Kuti Nkhaniyo Ndi Yothandiza
    Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
th phunziro 1 tsamba 4

PHUNZIRO 1

Mawu Oyamba Abwino

Lemba

Machitidwe 17:22

MFUNDO YAIKULU: M’mawu anu oyamba, muyenera kunena zinthu zochititsa chidwi, kutchula zokhudza nkhani yanu komanso kusonyeza chifukwa chake nkhaniyo ili yothandiza kwambiri kwa omvera.

MMENE MUNGACHITIRE:

  • Kukopa chidwi. Sankhani funso, mawu enaake, zochitika zenizeni kapena nkhani imene omvera anu angachite nayo chidwi.

    Mfundo yothandiza

    Muziganizira zinthu zimene zingachititse chidwi anthu n’kukonza mawu oyamba kuti agwirizane ndi zimenezo.

  • Fotokozani nkhani yanu. M’mawu anu oyamba muyenera kuthandiza anthu kudziwa nkhani imene mukambirane komanso cholinga chake.

  • Sonyezani chifukwa chake nkhaniyo ndi yofunika. Konzekerani nkhani yanu m’njira yoti igwirizane ndi zimene zingathandize anthu amene mukukambirana nawo. Anthuwo ayenera kuona mosavuta kuti nkhaniyo iwathandizadi.

    Mfundo yothandiza

    Mukamakonzekera nkhani ya onse muzidzifunsa kuti, ‘Kodi panopa anthu mumpingo wathu akukumana ndi mavuto otani?’ Ndiye mawu anu oyamba asonyeze kuti nkhaniyo iwathandiza pa mavuto amenewo.

MU UTUMIKI

Kuti mudziwe zimene munthu angachite nazo chidwi, muziyang’ana zimene munthuyo akuchita kapena mmene pakhomo pake pakuonekera. Ndiye poyamba kukambirana naye muziyamba ndi funso kapena mawu okhudza zinthu zimenezo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena