Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yehova Anamulezera Mtima Yona
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
    • Yona akumira m’nyanja ndipo chinsomba chachikulu chikusambira chapafupi

      MUTU 54

      Yehova Analezera Mtima Yona

      Anthu a mumzinda wa Nineve ankachita zinthu zoipa. Choncho Yehova anauza mneneri wake Yona kuti apite kukawachenjeza kuti asiye zoipazo. Koma Yona anathawa ndipo anakwera sitima yapamadzi yopita ku Tarisi.

      Ali pa ulendowu, panyanja panayamba chimphepo champhamvu moti oyendetsa sitima anachita mantha kwambiri. Iwo anapemphera kwa milungu yawo n’kumafunsa kuti: ‘Kodi izi zikuchitika chifukwa chiyani?’ Kenako Yona anawauza kuti: ‘Anthuni, wolakwa ndine. Yehova anandiuza kuti ndichite zinazake ndiye ndikuthawa. Mundiponye m’nyanjamu ndipo mphepoyi isiya.’ Oyendetsa sitimawo sankafuna kumuponya m’madzi koma Yona analimbikira kuti amuponye. Kenako anamuponyadi ndipo mphepo ija inasiyira pomwepo.

      Yona ankangoganiza kuti afa basi. Pamene ankamira, anayamba kupemphera kwa Yehova. Zitatero, Yehova anatumiza chinsomba chimene chinameza Yona. Komabe iye sanafe. Ali m’mimba mwa chinsombacho anapempheranso kuti: ‘Yehova, ndikukulonjezani kuti ndizimvera chilichonse chimene mungandiuze.’ Yona anakhala m’mimba mwa chinsombacho kwa masiku atatu ndipo kenako chinakamulavulira kumtunda.

      Yona atapulumuka, Yehova anamuuzanso kuti apite ku Nineve kuja. Pa nthawiyi Yona sanakane. Atafika kumeneko anauza anthu oipawo kuti: ‘Kwangotsala masiku 40 okha ndipo mzinda wa Nineve uwonongedwa.’ Kenako panachitika zinthu zimene aliyense samayembekezera. Anthu a ku Nineve atamva uthengawo anasinthiratu. Mfumu yawo inalamula kuti: ‘Tiyeni tipemphere kwa Mulungu ndipo tisiye zoipa. Mwina satiwononga.’ Yehova ataona kuti anthuwo alapa, sanawononge mzindawo.

      Yona akufika mumzinda wa Nineve

      Izi si zimene Yona ankayembekezera choncho anakwiya kwambiri. Ndiye tangoganiza, Yehova analezera mtima Yona komanso kumuchitira chifundo, koma iyeyo sanachitire chifundo anthu a ku Nineve. M’malomwake Yona anangotuluka mumzindawo n’kukakhala pansi pa chomera cha mtundu wa mphonda. Kenako chomeracho chinauma ndipo Yona anakwiyanso. Ndiyeno Yehova anamufunsa kuti: ‘Kodi ukumvera chisoni chomerachi koma osamvera chisoni anthu a ku Nineve? Inetu ndawachitira chifundo ndipo sindinawawononge.’ Kodi Yehova ankatanthauza chiyani pamenepa? Ankatanthauza kuti anthu a ku Nineve anali ofunika kuposa chomera chilichonse.

      “Yehova . . . akukulezerani mtima chifukwa sakufuna kuti munthu aliyense adzawonongedwe, koma akufuna kuti anthu onse alape.”​—2 Petulo 3:9

      Mafunso: Kodi Yehova anathandiza Yona kukhala ndi khalidwe liti? Kodi tingaphunzire chiyani pa zimene zinachitikira Yona?

      Yona chaputala 1 mpaka chaputala 4

  • Mngelo wa Yehova Anateteza Hezekiya
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
    • Mngelo akupha asilikali pamsasa wa Asuri

      MUTU 55

      Mngelo wa Yehova Anateteza Hezekiya

      Senakeribu yemwe anali mfumu ya Asuri anagonjetsa ufumu wa Isiraeli wa mafuko 10. Ndiyeno ankafunanso kugonjetsa ufumu wa Yuda wa mafuko awiri. Iye anayamba kugonjetsa mizinda ya Yuda. Mzinda umene ankaufunitsitsa unali wa Yerusalemu. Koma Senakeribu sankadziwa kuti Yehova ankateteza mzindawu.

      Hezekiya, yemwe anali mfumu ya Yuda, anapereka ndalama zambiri kwa Senakeribu kuti asalande mzinda wa Yerusalemu. Senakeribu analandira ndalamazo, komabe anatumiza gulu la asilikali ake kuti akagonjetse Yerusalemu. Anthu a mumzindawo atamva kuti asilikaliwo atsala pang’ono kufika, anachita mantha kwambiri. Koma Hezekiya anawauza kuti: ‘Musachite mantha. N’zoona kuti Asuri ndi amphamvu, komabe Yehova atithandiza.’

      Senakeribu anatumiza Rabisake kuti apite ku Yerusalemu kukalankhula ndi Ayuda. Rabisake anaima panja pa mzindawu n’kukuwa kuti: ‘Inutu Hezekiya asakupusitseni. Yehova sangakuthandizeni. Palibe mulungu amene angatilepheretse kukugonjetsani!’

      Hezekiya anapempha Yehova kuti amuthandize kudziwa zoyenera kuchita. Yehova anayankha kuti: ‘Musaope zimene Rabisake akunenazo. Senakeribu sangagonjetse Yerusalemu.’ Kenako Hezekiya analandira makalata ochokera kwa Senakeribu. M’makalatawo munali mawu akuti: ‘Tangonenani kuti mwagonja. Yehovatu sakupulumutsani.’ Zitatero Hezekiya anapemphera kuti: ‘Chonde Yehova tipulumutseni kuti aliyense adziwe kuti inu nokha ndinu Mulungu woona.’ Yehova anamuuza kuti: ‘Mfumu ya Asuri sifika ku Yerusalemu. Ineyo nditeteza mzinda wangawu.’

      Senakeribu ankaona kuti agonjetsa Yerusalemu basi. Koma usiku wina, Yehova anatumiza mngelo kumalo amene asilikali a Asuri ankagona. Mngeloyo anapha asilikali 185,000. Asilikali onse amphamvu a Senakeribu anathera pomwepo. Zitatero Senakeribu anadziwa kuti wagonja ndipo anangouyamba ulendo wobwerera kwawo. Apa ndiye kuti Yehova anakwaniritsa lonjezo lake loti adzateteza Hezekiya komanso mzinda wa Yerusalemu. Kodi iweyo ukanakhala ku Yerusalemu, ukanadalira Yehova?

      “Mngelo wa Yehova amamanga msasa kuzungulira anthu onse amene amaopa Mulungu, ndipo amawapulumutsa.”​—Salimo 34:7

      Mafunso: Kodi Yehova anateteza bwanji Yerusalemu? Kodi iweyo umakhulupirira zoti Yehova angakuteteze?

      2 Mafumu 17:1-6; 18:13-37; 19:1-37; 2 Mbiri 32:1-23

Mabuku a Chichewa (1974-2026)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena