-
Mzinda wa Yerusalemu UnawonongedwaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 58
Mzinda wa Yerusalemu Unawonongedwa
Nthawi zambiri, Ayuda ankasiya Yehova n’kumalambira milungu yabodza. Yehova anayesetsa kuwathandiza kwa zaka zambiri. Ankawatumizira aneneri ambiri kuti awachenjeze koma iwo sankawamvera. M’malomwake ankangowaseka. Kodi Yehova anathetsa bwanji vuto lolambira mafanoli?
Nebukadinezara, yemwe anali mfumu ya Babulo, ankagonjetsa mayiko ambiri. Pa ulendo woyamba umene anagonjetsa Yerusalemu, anagwira Mfumu Yehoyakini, akalonga, asilikali komanso anthu ena aluso ndipo anapita nawo ku Babulo. Anatenganso chuma chonse chimene chinali m’kachisi wa Yehova. Kenako, Nebukadinezara anasankha Zedekiya kuti akhale mfumu ya Yuda.
Poyamba, Zedekiya ankamvera Nebukadinezara. Koma kenako anthu a m’mayiko apafupi komanso aneneri abodza anamuuza kuti aukire ulamuliro wa Babulo. Koma Yeremiya anamuuza kuti: ‘Mukasiya kumvera Ababulo, anthu anu ambiri aphedwa ndipo m’dziko lino mukhala njala ndi matenda.’
Zedekiya atangolamulira zaka 8, anasiya kumvera Ababulo. Iye anapempha asilikali a ku Iguputo kuti amuthandize. Ndiyeno Nebukadinezara anatumiza asilikali ake kuti akawononge mzinda wa Yerusalemu. Asilikaliwo atazungulira mzindawo, Yeremiya anauza Zedekiya kuti: ‘Yehova wanena kuti mukangouza Ababulo kuti mwagonja, mzindawu komanso anthu anu apulumuka. Koma mukachita makani, Ababulo awotcha mzindawu ndipo inuyo apita nanu ku ukapolo.’ Zedekiya anayankha kuti: ‘Sindingayerekeze n’komwe kuwauza Ababulo kuti ndagonja!’
Patangopita zaka zitatu ndi hafu, asilikali a Babulo analowa mumzindawo n’kuuwotcha. Iwo anawotcha kachisi, kupha anthu ambiri n’kutenga ena kupita nawo ku ukapolo ku Babulo.
Zedekiya anayamba kuthawa koma asilikali a ku Babulo anamuthamangitsa. Anamugwira pafupi ndi Yeriko n’kupita naye kwa Nebukadinezara. Mfumuyi inapha ana a Zedekiya iye akuona. Kenako anamuchotsa maso n’kumutsekera m’ndende ndipo anafera momwemo. Koma Yehova anauza Ayuda kuti: ‘Pakatha zaka 70 ndidzakubwezeretsani ku Yerusalemu.’
Kodi ukuganiza kuti achinyamata amene anapita ku Babulo zinawathera bwanji? Kodi iwo anakhalabe okhulupirika kwa Yehova?
“Yehova Mulungu, inu Wamphamvuyonse, ziweruzo zanu ndi zoona komanso zolungama.”—Chivumbulutso 16:7
-
-
Anyamata 4 Amene Anamvera YehovaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 59
Anyamata 4 Amene Anamvera Yehova
Nebukadinezara atatenga akalonga a ku Yuda n’kupita nawo ku Babulo, anasankha nduna ina dzina lake Asipenazi kuti iziyang’anira akalongawo. Nebukadinezara anauza Asipenazi kuti asankhe anyamata athanzi komanso anzeru. Anamuuza kuti anyamatawo asamaliridwe komanso aphunzitsidwe kwa zaka zitatu n’cholinga choti adzakhale akuluakulu a boma ku Babuloko. Anyamata amenewa anayeneranso kuwaphunzitsa kuwerenga, kulemba komanso kulankhula chilankhulo cha Akasidi. Ankafunikanso kumawapatsa chakudya chimene mfumu ndi anthu ogwira ntchito kunyumba kwake ankadya. Pagulu la anyamatawa panali Danieli, Hananiya, Misayeli ndi Azariya. Koma Asipenazi anawapatsa mayina achibabulo akuti, Belitesazara, Shadireki, Misheki ndi Abedinego. Kodi zimene ankawaphunzitsazo zinachititsa kuti anyamatawa asiye kutumikira Yehova? Ayi.
Iwo anatsimikiza kuti apitirizabe kumvera Yehova. Ankadziwa kuti sakuyenera kudya chakudya cha mfumu chifukwa Chilamulo cha Yehova chinkaletsa zina mwa zakudya zimenezo. Choncho anauza Asipenazi kuti: ‘Chonde musamatipatse chakudya cha mfumu.’ Koma Asipenazi anawayankha kuti: ‘Mukapanda kumadya zakudya za mfumu muwonda ndipo mfumu indipha.’
Ndiyeno Danieli anapeza nzeru. Anauza Asipenazi kuti: ‘Muzitipatsa masamba ndi madzi kwa masiku 10. Kenako mudzayerekeze mmene tizidzaonekera ndi mmene anyamata ena azidzaonekera.’ Asipenazi anavomera.
Patatha masiku 10, Danieli ndi anzake atatuwo ankaoneka athanzi kuposa anyamata ena onse. Yehova anasangalala chifukwa choti anyamatawa anamumvera ndipo anapatsa Danieli nzeru moti ankatha kudziwa tanthauzo la masomphenya ndi maloto.
Zaka zitatu zija zitatha Asipenazi anapita ndi anyamata onse kwa Nebukadinezara. Mfumuyo italankhula nawo, anaona kuti Danieli, Hananiya, Sadirake ndi Azariya anali anzeru komanso ochangamuka kuposa anyamata enawo. Choncho anawasankha kuti azigwira ntchito kunyumba kwake. Mfumuyi inkafunsira nzeru kwa anyamatawa chifukwa Yehova anawathandiza kukhala ndi nzeru kuposa anzeru onse a m’dzikolo.
Ngakhale kuti anyamata 4 amenewa ankakhala kudziko la eni, sanaiwale kuti anali anthu a Mulungu. Kodi iwenso utakhala kumalo koti kulibe makolo ako, ungapitirizebe kumvera Yehova?
“Usalole kuti munthu aliyense akuderere poona kuti ndiwe wamngʼono. Mʼmalomwake, ukhale chitsanzo kwa okhulupirika pa zimene umalankhula, makhalidwe ako, chikondi, chikhulupiriro ndi khalidwe loyera.”—1 Timoteyo 4:12
-