Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ufumu Wofanana ndi Mtengo Waukulu
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
    • Mtengo umene Nebukadinezara analota ukugwetsedwa

      MUTU 62

      Ufumu Wofanana ndi Mtengo Waukulu

      Tsiku lina Nebukadinezara analota maloto oopsa. Ndiyeno anaitana anthu anzeru a mu ufumu wake kuti amuuze tanthauzo lake. Koma palibe amene anakwanitsa kumasulira malotowo. Kenako Nebukadinezara anauza Danieli maloto akewo.

      Anamufotokozera kuti: ‘Ndinalota mtengo womwe unakula kwambiri n’kufika kumwamba. Umaoneka padziko lonse ndipo unali ndi masamba okongola komanso zipatso zambiri. Nyama zakutchire zimakhala mumthunzi wake komanso mbalame zimamanga zisa munthambi zake. Kenako mngelo anabwera kuchokera kumwamba n’kufuula kuti: “Gwetsani mtengowo ndipo mudule nthambi zake. Koma musiye chitsa ndi mizu yake munthaka ndipo muchikulunge ndi mkombero wachitsulo komanso wakopa. Mtima wake usinthidwe kuchoka kumtima wa munthu nʼkukhala mtima wa nyama ndipo padutse nthawi zokwana 7. Anthu adziwe kuti Mulungu ndi Wolamulira ndiponso kuti amapereka ulamuliro kwa aliyense amene akufuna kumupatsa.”’

      Yehova anathandiza Danieli kuti adziwe zimene malotowa ankatanthauza. Danieli anachita mantha ndi tanthauzo la malotowo. Anauza Nebukadinezara kuti: ‘Mfumu, malotowa akunena za inu. Koma zikanakhala bwino akanakhala kuti akunena za adani anu. Mtengo waukulu umene unadulidwawo ukuimira inuyo. Mudzasiya kukhala mfumu ndipo mudzapita kutchire n’kumakadya msipu ngati nyama yakutchire. Koma popeza mngelo ananena kuti chitsa cha mtengowo chisazulidwe, ndiye kuti mudzabwereranso n’kukhala mfumu.’

      Patatha chaka, tsiku lina Nebukadinezara ankayenda padenga la nyumba yake n’kumaona zinthu zikuluzikulu zimene anachita mu ufumu wake. Iye anati: ‘Koma ndiye zinthu zikundiyendera bwino. Taonani mmene mzinda wa Babulo ukukongolera!’ Koma mawu ake adakali m’kamwa, anamva mawu ochokera kumwamba akuti: ‘Nebukadinezara! Ufumu wachoka m’manja mwako.’

      Nthawi yomweyo Nebukadinezara anachita misala ndipo anakhala ngati nyama yakutchire. Anachoka kunyumba yake yachifumu n’kumakakhala kutchire ndi nyama. Tsitsi lake linatalika ngati nthenga za chiwombankhanga ndipo zikhadabo zake zinatalika ngati za mbalame.

      Patatha zaka 7, Nebukadinezara anachira ndipo Yehova anamuikanso kukhala mfumu ya Babulo. Kenako iye anati: ‘Ndikutamanda Yehova, Mfumu yakumwamba. Panopa ndadziwa kuti iye ndi Wolamulira. Amatsitsa anthu odzikweza ndipo angathe kupereka ufumu kwa aliyense amene akufuna.’

      “Kunyada kumachititsa kuti munthu awonongeke, ndipo mtima wodzikuza umachititsa kuti munthu apunthwe.”​—Miyambo 16:18

      Mafunso: Kodi maloto a Nebukadinezara ankatanthauza chiyani? Kodi Nebukadinezara ananena kuti waphunzira chiyani zokhudza Yehova?

      Danieli 4:1-37

  • Dzanja Linalemba Pakhoma
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
    • Dzanja Linalemba Pakhoma

      MUTU 63

      Dzanja Linalemba Pakhoma

      Patapita nthawi, Belisazara anakhala mfumu ya Babulo. Tsiku lina madzulo anakonza phwando ndipo anaitana nduna zake zokwana 1,000. Kenako anauza atumiki ake kuti akatenge makapu agolide amene Nebukadinezara anatenga m’kachisi wa Yehova. Iye ndi nduna zakezo anayamba kumwera vinyo m’makapuwo n’kumatamanda milungu yawo. Koma mwadzidzidzi, anangoona dzanja la munthu likulemba mawu odabwitsa pakhoma la m’chipinda chimene ankachitira phwandolo.

      Belisazara anachita mantha kwambiri. Anaitana anthu a matsenga n’kuwauza kuti: ‘Aliyense amene angandiuze tanthauzo la mawuwa, ndimuika kukhala wolamulira wachitatu mu ufumu wa Babulo.’ Koma palibe anatha kumuuza tanthauzo la mawuwo. Kenako mfumukazi inabwera n’kudzamuuza kuti: ‘Pali munthu wina dzina lake Danieli amene ankauza Nebukadinezara tanthauzo la zinthu zosiyanasiyana. Akhozatu kukuuzani tanthauzo la mawuwa.’

      Danieli atafika, Belisazara anamuuza kuti: ‘Ngati ungathe kuwerenga mawuwa n’kundiuza kumasulira kwake, ndikupatsa mkanda wagolide komanso ndikuika kuti ukhale wolamulira wachitatu mu ufumuwu.’ Koma Danieli anayankha kuti: ‘Sindikufuna mphatso zanuzo. Komabe ndikuwerengerani mawuwa ndiponso ndikuuzani kumasulira kwake. Bambo anu, a Nebukadinezara, anali odzikweza ndipo Yehova anawachepetsa. Inuyo mukudziwa zimene zinawachitikira, koma mukunyoza Yehova ndipo mukumwera vinyo m’makapu agolide a m’kachisi wake. Choncho Yehova walemba mawu awa: Mene, Mene, Tekeli ndi Parasini. Mawuwa akutanthauza kuti Amedi ndi Aperisiya adzagonjetsa Babulo ndipo inu simukhalanso mfumu.’

      Asilikali a Mfumu Koresi akuwoloka mtsinje kukalowa pageti la mzinda wa Babulo

      Pa nthawiyo zinkaoneka ngati palibe angagonjetse mzinda wa Babulo. Mzindawu unkaoneka kuti unali wotetezeka ndi mpanda wolimba komanso mtsinje waukulu. Koma usiku womwewo, Amedi ndi Aperisiya anaukira mzindawu. Mfumu ya Aperisiya, dzina lake Koresi, inapatutsa madzi a mumtsinje ndipo asilikali ake anawoloka n’kukafika pageti la mzindawu. Atafika, anapeza kuti pagetipo m’posatseka. Choncho analowa n’kulanda mzindawo komanso kupha mfumu. Ndiyeno Koresi anayamba kulamulira Babulo.

      Pasanathe chaka, Koresi ananena kuti: ‘Yehova wandiuza kuti ndimangenso kachisi wake wa ku Yerusalemu. Anthu ake amene akufuna kukathandiza nawo ntchitoyi, angathe kupita.’ Choncho mogwirizana ndi zimene Yehova analonjeza, Ayuda ambiri anabwerera ku Yerusalemu. Apa n’kuti patatha zaka 70 kuchokera pamene Yerusalemu anawonongedwa. Koresi anabwezeretsa makapu asiliva komanso zinthu zina zimene Nebukadinezara anatenga m’kachisi wa Yehova. Kodi waona mmene Yehova anagwiritsira ntchito Koresi pothandiza anthu ake?

      “Wagwa! Babulo Wamkulu wagwa, ndipo wakhala malo amene ziwanda zimakhala.”​—Chivumbulutso 18:2

      Mafunso: Kodi mawu amene analembedwa pakhoma ankatanthauza chiyani? Kodi Yehova anauza Koresi kuti achite chiyani?

      Ezara 1:1-11; Danieli 5:1-30; Yesaya 44:27, 28; 45:1, 2; Yeremiya 25:11, 12

Mabuku a Chichewa (1974-2026)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena