-
Yesu Anakhala MesiyaZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 74
Yesu Anakhala Mesiya
Yohane ankalalikira kuti: ‘Wina wamkulu kuposa ine akubwera.’ Yesu ali ndi zaka 30 anapita kumtsinje wa Yorodano kumene Yohane ankabatiza anthu. Pa nthawiyi Yesu ankachokera ku Galileya. Iye ankafuna kuti Yohane amubatize koma Yohaneyo anati: ‘Ayi, ine si woyenera kubatiza inu. Inuyo ndi amene mukuyenera kundibatiza ine.’ Yesu anamuuza kuti: ‘Yehova akufuna kuti undibatize.’ Choncho anapita mumtsinje wa Yorodano ndipo Yohane anabatiza Yesu pomuviika thupi lonse m’madzi.
Yesu atavuuka m’madzimo anayamba kupemphera. Ndiyeno kumwamba kunatseguka ndipo mzimu wa Mulungu wooneka ngati nkhunda unatsika n’kudzamutera. Kenako Yehova analankhula ali kumwamba kuti: “Iwe ndi Mwana wanga wokondedwa, umandisangalatsa kwambiri.”
Mzimu wa Mulungu utafika pa Yesu, Yesuyo anakhala Khristu kapena kuti Mesiya. Tsopano anali wokonzeka kuyamba kugwira ntchito imene Mulungu anamutuma.
Yesu atangobatizidwa anapita m’chipululu ndipo anakhalamo masiku 40. Atachoka m’chipululumo anapita kukaona Yohane. Yohane ataona Yesu akubwera poteropo anati: ‘Uyu ndi Mwanawankhosa wa Mulungu amene akuchotsa uchimo wa dziko.’ Apa Yohane ankafuna kuti anthu adziwe kuti Yesu ndi Mesiya. Koma kodi ukudziwa zimene zinachitika pamene Yesu anali kuchipululu? Tiona m’mutu wotsatira.
“Ndiyeno panamveka mawu ochokera kumwamba akuti: ‘Iwe ndi Mwana wanga wokondedwa, umandisangalatsa kwambiri.’”—Maliko 1:11
-
-
Mdyerekezi Anayesa YesuZimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
-
-
MUTU 75
Mdyerekezi Anayesa Yesu
Yesu atabatizidwa mzimu woyera unamutsogolera kupita kuchipululu. Sanadye chilichonse kwa masiku 40 choncho anali ndi njala kwambiri. Ndiyeno Mdyerekezi anabwera kudzamuyesa ndipo anamuuza kuti: ‘Ngati ndinudi Mwana wa Mulungu, uzani miyalayi kuti isanduke mitanda ya mkate.’ Koma Yesu anamuyankha potchula zimene Malemba amanena. Anati: ‘Malemba amanena kuti munthu safunika chakudya chokha kuti akhale ndi moyo. Amafunikanso kumvera mawu alionse ochokera m’kamwa mwa Yehova.’
Kenako Mdyerekezi anauza Yesu kuti: ‘Ngati ndinudi Mwana wa Mulungu, mudumphe kuchokera pamwamba pa kachisi. Pajatu Malemba amanena kuti Mulungu adzatumiza angelo ake kuti adzakunyamuleni kuti musavulale.’ Koma Yesu anayankhanso pogwiritsa ntchito Malemba. Iye anati: ‘Malemba amanena kuti usamuyese Yehova.’
Kenako Mdyerekezi anaonetsa Yesu maufumu onse a padziko lapansi ndi chuma chawo. Ndiyeno anamuuza kuti: ‘Ndikupatsani maufumu onsewa ndi chuma chonsechi ngati mutagwada pansi kamodzi kokha n’kundilambira.’ Koma Yesu anayankha kuti: ‘Choka Satana! Malemba amati, uyenera kulambira Yehova yekha basi.’
Yesu atanena zimenezi, Mdyerekezi anamusiya ndipo angelo anabwera kudzamupatsa chakudya. Izi zitatha, Yesu anayamba kulalikira uthenga wabwino wa Ufumu. Imeneyi ndi ntchito imene Mulungu anamutuma kuti adzachite. Anthu ankakonda zimene Yesu ankaphunzitsa ndipo ankamutsatira kulikonse kumene wapita.
“[Mdyerekezi] akamanena bodza, amangosonyeza mmene alili, chifukwa iye ndi wabodza komanso tate wake wa bodza.”—Yohane 8:44
-