Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 2/12 tsamba 32
  • “Bukuli Ndi Labwino Kwambiri”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Bukuli Ndi Labwino Kwambiri”
  • Galamukani!—2012
Galamukani!—2012
g 2/12 tsamba 32

“Bukuli Ndi Labwino Kwambiri”

● Kodi mungakonde kuwerenga zimene Yesu Khristu ankaphunzitsa komanso mafanizo osaiwalika amene ankawagwiritsira ntchito? Buku lakuti Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako likhoza kukuthandizani.

Munthu wina amene anawerenga bukuli anati: “Bukuli ndi labwino kwambiri chifukwa linalembedwa mosavuta kumva komanso limafotokoza mwatsatanetsatane moyo wa Ambuye ali padziko lapansi.”

Malinga ndi zimene tikudziwa zokhudza Baibulo, nkhani zimene zinalembedwa m’bukuli zinalembedwa motsatira nthawi imene zinachitika. Nkhani za m’bukuli zinatengedwa m’mabuku anayi ouziridwa, amene analembedwa ndi anthu omwe anakhala ndi moyo pa nthawi ya Yesu. Anthuwa anali Mateyu, Maliko, Luka ndi Yohane. Mateyu ndi Yohane anali atumwi komanso ankayenda ndi Yesu. Maliko anali mnzake kwambiri wa Petulo, yemwe anali mtumwi wa Yesu. Ndipo Luka, yemwe anali dokotala, ankayenda ndi mtumwi Paulo.

Ngati mungafune buku lokhala ndi zithunzi zokongola limeneli, lembani zofunika m’munsimu ndipo tumizani ku adiresi yoyenera pa maadiresi amene ali patsamba 5 m’magazini ino.

□ Ndikupempha kuti munditumizire bukuli.

□ Nditumizireni munthu kuti ayambe kuphunzira nane Baibulo kwaulere.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena