Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g20 No. 1 tsamba 4
  • Zomwe Zimachititsa Kuti Anthu Azikhala ndi Nkhawa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Zimachititsa Kuti Anthu Azikhala ndi Nkhawa
  • Galamukani!—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Zimene Zimachititsa Moyo Kukhala Wopanikizika ndi Zotsatirapo Zake
    Galamukani!—2005
  • Kupanikizika Maganizo Kwabwino ndi Koipa
    Galamukani!—1998
  • Zimene Tingachite Kuti Tisamapanikizike Kwambiri
    Galamukani!—2010
  • Kodi Ndingatani Ngati Ndimapanikizika Kwambiri Kusukulu?
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Loyamba
Onani Zambiri
Galamukani!—2020
g20 No. 1 tsamba 4

MUNGATANI KUTI MUCHEPETSE NKHAWA?

Zomwe Zimachititsa Kuti Anthu Azikhala ndi Nkhawa

Akatswiri a pachipatala china chotchuka, chotchedwa Mayo, anati: “Nthawi zambiri anthu akuluakulu ndi amene akuvutika kwambiri ndi nkhawa. Zimenezi zili chonchi chifukwa moyo wa masiku ano umasinthasintha komanso ndi wosadalirika.” Zina mwa zinthu zimene zimachititsa kuti anthu azikhala ndi nkhawa ndi monga:

  • kutha kwa banja

  • kumwalira kwa munthu amene timamukonda

  • matenda aakulu

  • ngozi yaikulu

  • kuphwanya malamulo

  • kukhala wotanganidwa nthawi zonse

  • ngozi zachilengedwe kapena zochititsidwa ndi anthu

  • kupanikizika ndi zochitika za kuntchito kapena kusukulu

  • kusowa kwa ntchito komanso mavuto a zachuma

KUCHOTSEDWA NTCHITO

Bungwe lina la ku America loona za kaganizidwe ka anthu linati: “Kuchotsedwa ntchito ndi chinthu chopweteka kwambiri. Anthu ambiri amene anachotsedwa ntchito amadwaladwala, mabanja awo amavutavuta, amakhala ndi nkhawa, amadwala matenda a maganizo ndipo ena amafika podzipha kumene. Kuchotsedwa ntchito kumasokonezeratu moyo wa munthu.”

ANA NAWONSO AMAVUTIKA NDI NKHAWA

Masiku ano ana ena akumavutika ndi nkhawa chifukwa chovutitsidwa ndi anzawo akusukulu komanso chifukwa amanyalanyazidwa ndi makolo awo. Ana ena amachitiridwa nkhanza monga kumenyedwa, kuopsezedwa komanso kugwiriridwa. Ena amada nkhawa chifukwa cha mayeso ndipo ena amasokonezeka maganizo makolo awo akasiyana. Ana omwe amakumana ndi mavuto amenewa amalota maloto oopsa, sakhoza bwino kusukulu, amadwala matenda a maganizo, safuna kucheza ndi anzawo komanso amavutika kukhala odziletsa. Ana akayamba kukhala ndi nkhawa amafunika kuthandizidwa mwamsanga.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena