Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • sp tsamba 28-29
  • Moyo Udzakhala Wosangalatsa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Moyo Udzakhala Wosangalatsa
  • Kodi Mizimu ya Akufa Ilipodi?
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Anthu Amene Anamwalira Adzakhalanso ndi Moyo
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
    Nsanja ya Olonda—2004
  • Mutu wa Njoka Udzaphwanyidwa
    Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
  • Yesu Ali ndi Mphamvu Kuposa Ziwanda
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
  • Chiphunzitso Chaumulungu Chilimbana ndi Ziphunzitso za Ziŵanda
    Nsanja ya Olonda—1994
Onani Zambiri
Kodi Mizimu ya Akufa Ilipodi?
sp tsamba 28-29

Moyo Udzakhala Wosangalatsa

Yesu akuponyera Satana kuphompho

Posachedwapa Satana ndi ziwanda zake sazidzasocheretsanso anthu

Nthawi yoti Satana ndi ziwanda zake asocheretse anthu itha posachedwapa. Yehova anawathamangitsa kale kumwamba. (Chivumbulutso 12:9) Mtumwi Yohane anaona masomphenya osonyeza kuti posachedwapa Yehova athana ndi Satana ndi ziwanda. Iye analemba kuti: “Ndipo ndinaona mngelo akutsika kuchokera kumwamba ali ndi kiyi wa paphompho [dzenje lakuya kwambiri] ndi unyolo waukulu m’dzanja lake. Kenako anagwira chinjoka, njoka yakale ija, amene ndi Mdyerekezi ndiponso Satana, ndi kumumanga zaka 1,000. Ndipo anamuponyera m’phompho ndi kutseka pakhomo pa phompholo n’kuikapo chidindo kuti asasocheretsenso mitundu ya anthu kufikira zitatha zaka 1,000.” (Chiv. 20:1-3) Kenako Mdyerekezi pamodzi ndi ziwanda zake adzawonongedwa ndipo sadzakhalaponso.​—Chivumbulutso 20:10.

Anthu onse oipa adzawonongedwanso.​—Salimo 37:9, 10; Luka 13:5.

Anthu Amene Anamwalira Adzakhalanso ndi Moyo

Anthu ali m’Paradaiso ndipo akulandira anthu amene aukitsidwa

Anthu amene anamwalira adzaukitsidwa n’kumakhala padzikoli

Satana ndi ziwanda akadzawonongedwa, Yehova adzadalitsa kwambiri anthu. Yesu anayerekezera imfa ndi tulo. Izi zikutanthauza kuti munthu akafa sadziwa chilichonse ndipo amangokhala ngati wagona popanda kulota chilichonse. (Yohane 11:11-14) Yesu ananena zimenezi chifukwa ankadziwa kuti posachedwapa anthu amene anafa adzaukitsidwa. Paja iye anati: “Idzafika nthawi pamene onse ali m’manda achikumbutso . . . adzatuluka.”​—Yohane 5:28, 29; Yerekezerani ndi Machitidwe 24:15.

Anthu oukitsidwawo adzakhala padziko lomweli. M’malo molandira uthenga wa maliro, tizidzalandira mauthenga osangalatsa oti akutiakuti aja aukitsidwa. Zidzakhala zosangalatsa kwambiri kulandira anthu amene adzaukitsidwe.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena