Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi kuchita Chibwenzi Mobisa N’koopsa Motani?
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
    • Mutu 2

      Kodi kuchita Chibwenzi Mobisa N’koopsa Motani?

      Jessica anathedwa nzeru mnyamata wina wa m’kalasi mwake, dzina lake Jeremy, atayamba kusonyeza kuti akum’funa. Ponena za Jeremy, Jessica anati: “Anali mnyamata wooneka bwino kwambiri, ndipo anzanga ankandiuza kuti sindidzapezanso mnyamata wakhalidwe labwino ngati ameneyu. Panali atsikana angapo amene ankamusirira koma iye sankawafuna. Ankangofuna ineyo basi.”

      Pasanapite nthawi yaitali, Jeremy anafunsira Jessica. Jessica anauza Jeremy kuti iye ndi wa Mboni za Yehova, motero sangaloledwe kukhala pachibwenzi ndi mnyamata yemwe si wa Mboni. Jessica anati: “Nditamuuza zimenezi, Jeremy anatulukira nzeru inayake. Iye anati, ‘Tingathe kumangoyendetsa chibwenzi chathucho makolo ako osadziwa.’”

      KODI inuyo mungatani ngati munthu amene amakudololani atakuuzani nzeru yotereyi? Mwina mudabwa kumva kuti Jessica anamvera maganizo a Jeremy aja. Iye anati: “Ndinkaganiza kuti nditakhala naye pachibwenzi ndingathe kumuphunzitsa kuti ayambe kukonda Yehova.” Koma kodi zinaterodi? Chakumapeto kwa nkhaniyi tiona zimene zinachitika, koma choyamba tiyeni tione zimene zimachititsa ena kuchita chibwenzi mobisa.

      N’chifukwa Chiyani Amachita Zimenezi?

      Kodi achinyamata ena amachitiranji chibwenzi mobisa? Mnyamata wina dzina lake David ananena mwachidule kuti: “Iwowa amadziwa kuti makolo awo sangasangalale nazo.” Mtsikana wina dzina lake Jane anatchula chifukwa chinanso. Iye anati: “Ena amachita zibwenzi mobisa pofuna kutsimikizira kuti angathe kuchita zinthu paokha, popanda kuuzidwa zochita. Akamaona kuti sakupatsidwa ufulu wochita zinthu ngati munthu wamkulu, amaona kuti ndi bwino kungochita zimene akufuna popanda kuuza makolo awo.”

      Kodi mungaganizire zifukwa zina zimene zimapangitsa ena kuchita chibwenzi mobisa? Lembani m’munsimu zifukwazo.

      ․․․․․

      Mosakayikira, mukudziwa kuti Baibulo limati muyenera kumvera makolo anu. (Aefeso 6:1) Ndipotu ngati makolo anu akukuletsani kukhala pachibwenzi, ayenera kuti ali ndi zifukwa zomveka. Komabe musadabwe ngati mutakhala ndi maganizo otsatirawa:

      ● Ndimaona kuti ndine wotsalira chifukwa aliyense ali ndi chibwenzi kupatulapo ineyo.

      ● Munthu amene si wachipembedzo changa wandidolola.

      ● Ndimafuna kukhala pachibwenzi ndi Mkhristu mnzanga ngakhale kuti sindinafike pamsinkhu wolowa m’banja.

      N’kutheka kuti mukudziwiratu zimene makolo anu anganene pa maganizo amenewa. Ndipo pansi pamtima mungavomereze kuti makolo anuwo akunena zoona. Komabe, mwina mumamva ngati mmene ankamvera mtsikana wina dzina lake Manami, yemwe anati: “Ndimafuna kwambiri kukhala ndi chibwenzi moti nthawi zina ndimakayikira ngati ndi bwino kukhalabe wopanda chibwenzi. Achinyamata ambiri masiku ano, amaona kuti kukhala wopanda chibwenzi n’kutsalira kwambiri. Ndiponso palibe amene angafune kukhala yekhayekha.” Motero ena amachita chibwenzi mobisira makolo awo. Kodi amachita zimenezi motani?

      “Anatiuza Kuti Tisaulule”

      Mawu akuti “chibwenzi chobisa,” akusonyezeratu kuti pali zinazake zachinyengo. Ena amayendetsa chibwenzi chotere polankhulana pafoni kapena pa Intaneti. Akakhala pagulu, amangoonetsa ngati palibe chilichonse, koma mungadabwe kwambiri mutadziwa zimene amauzana pa Intaneti ndiponso pafoni.

      Njira inanso yobisira chibwenzi choterechi ndi yoti iwowa amaitana gulu la anzawo kuti akachite zinazake pamodzi, koma kenaka amene ali pachibwenziwo amangocheza awiri basi. James anati: “Nthawi ina, tinaitanidwa kuti tikacheze kwinakwake monga gulu, osadziwa kuti imeneyi inali njira yoti mnyamata ndi mtsikana winawake akacheze awiri, ndipo anatiuza kuti tisaulule.”

      Monga mmene James ananenera, nthawi zambiri anthu amathandizidwa ndi anzawo poyendetsa chibwenzi mobisa. Carol anati: “Mwina pamakhala mnzako mmodzi kapena awiri amene amadziwa za chibwenzicho koma sanena chilichonse chifukwa safuna kutchedwa kuti ndi apakamwa.” Nthawi zina, ena amachita kunena bodza lamkunkhuniza. Beth, wazaka 17, anati: “Ambiri amabisa zoti ali pachibwenzi ponamiza makolo awo za kumene akupita.” Misaki, mtsikana wazaka 19, anachita zimenezo. Iye anati: “Ndinkangopeka zoti ndiwauze. Komano pofuna kuti makolo anga asasiye kundikhulupirira, ndinkayesetsa kuti ndisamaname pa china chilichonse kupatulapo za chibwenzicho basi.”

      Kuopsa Kochita Chibwenzi Mobisa

      Ngati mukufuna kukhala ndi chibwenzi chobisa kapena ngati muli nacho kale, m’pofunika kuti muganizire mafunso awiri otsatirawa:

      Kodi khalidwe langali likandifikitsa kuti? Kodi muli ndi cholinga chokwatirana ndi munthuyo posachedwapa? Mnyamata wina wazaka 20 dzina lake Evan, anati: “Kukhala pachibwenzi popanda cholinga chomanga banja n’kofanana ndi kutsatsa malonda chinthu chinachake chimene sukuchigulitsa.” Mukatero, n’chiyani chingachitike? Lemba la Miyambo 13:12 limati: “Chiyembekezo chozengereza chidwalitsa mtima.” Kodi mungafune kuti munthu amene mumam’kondadi adwale mtima? Taonani chenjezo linanso: Kuchita chibwenzi mobisa kumakumanitsani mwayi woti makolo anu kapena achikulire ena okukondani akuthandizeni. Choncho, m’posavuta kuti muchite chiwerewere.—Agalatiya 6:7.

      Kodi Yehova Mulungu akumva bwanji ndi zimene ndikuchitazi? Baibulo limati: “Zinthu zonse zili pambalambanda ndi zoonekera poyera pamaso . . . pa uyo amene tidzayenera kuyankha kwa iye.” (Aheberi 4:13) Motero musadzinamize kuti mukubisa chibwenzi chanu kapena cha mnzanu, chifukwatu Yehova akuzidziwa kale zimenezo. Choncho, ngati mukuchita zachinyengo, dziwani kuti mukusewera paulimbo. Ndipotu, Yehova Mulungu amadana kwambiri ndi bodza. Moti “lilime lonama” lili m’gulu la zinthu zimene Baibulo linachita kuneneratu kuti iye amadana nazo.—Miyambo 6:16-19.

      Ululani

      N’chinthu chanzeru kuuza makolo anu kapena Mkhristu wamkulu wokhwima mwauzimu za chibwenzi chilichonse chimene mukuyendetsa mobisa. Ndipo ngati muli ndi mnzanu amene akuchita chibwenzi mobisa, musam’thandize chinyengo chakecho pomusungira chinsinsi. (1 Timoteyo 5:22) Komanso, kodi mungamve bwanji ngati mnzanuyo atagwa m’vuto chifukwa cha chibwenzicho? Kodi sitinganene kuti inuyo mwachititsa nawo vutolo?

      Tiyerekeze kuti muli ndi mnzanu amene amadwala matenda a shuga ndiyeno akudya zinthu zotsekemera kwambiri mobisa. Inuyo mutadziwa zimenezi, mnzanuyo akukupemphani kuti musaulule. Kodi mungatani? Kodi nkhawa yanu ingakhale pa kupulumutsa moyo wake kapena kumusungira chinsinsi?

      N’chimodzimodzinso ngati mukudziwa kuti mnzanu winawake akuchita chibwenzi mobisa. Musaope kuti mudana naye, muululeni. Ngati ali mnzanu weniwenidi, patsogolo pake adzazindikira kuti munatero chifukwa chomufunira zabwino.—Salmo 141:5.

      Mobisa Kapena Mosaonetsera?

      Sikuti nthawi zonse anthu akakhala pachibwenzi chimene anthu ena sakuchidziwa ndiye kuti akuchita zolakwika. Tayerekezerani kuti mnyamata ndi mtsikana akufuna kudziwana bwino, komano sakufuna kudzionetsera kwa kanthawi ndithu. N’kutheka kuti akutero pa chifukwa chofanana ndi chimene mnyamata wina dzina lake Thomas, ananena. Iye anati: “Iwo safuna kuti anthu aziwavutitsa ndi mafunso monga akuti: ‘Kodi mukwatirana liti?’”

      N’zoona kuti zonena za anthu ena zingathe kukulowetsani m’mavuto. (Nyimbo ya Solomo 2:7) Motero, anyamata ndi atsikana ena amaona kuti ndi bwino kusaonetsera akangoyamba kumene chibwenzi mpaka patapita nthawi ndithu. (Miyambo 10:19) Anna, yemwe ali ndi zaka 20, anati: “Kusaonetsera kumathandiza anthuwo kuti akhale ndi nthawi yokwanira yoona bwinobwino ngati onse atsimikizadi kumanga banja. Ndiyeno akatsimikizira zimenezi, m’pamene angayambe kuonetsera kwa anthu.”

      Komabe, dziwani kuti n’kulakwa kuwabisira anthu amene ayenera kudziwa za chibwenzicho, monga makolo anu komanso makolo a mnzanuyo. Ngati mukuona kuti simungauze munthu wina aliyense, dzifunseni chifukwa chake. Kodi n’kutheka kuti mukudziwa kuti makolo anu ali ndi zifukwa zomveka zokuletsani kutero?

      “Ndinadziwa Zoyenera Kuchita”

      Jessica, amene tam’tchula poyamba uja, anaganiza zothetsa chibwenzi chobisa ndi Jeremy atamva zimene zinachitikira mtsikana wina wachikhristu amenenso anachita chibwenzi mobisa. Jessica anati: “Nditamva mmene iye anathetsera chibwenzicho ndinadziwa zoyenera kuchita.” Kodi zinali zosavuta kuti Jessica athetse chibwenzi chakecho? Ayi. Jessica anati: “Uyutu anali mnyamata yekhayo amene ndinam’kondadi. Ndinkalira tsiku lililonse kwa milungu ingapo.”

      Komabe, Jessica ankadziwa kuti amakonda Yehova. Motero, ngakhale kuti anasokonezeka pang’ono, ankafunitsitsa kuchita zoyenera. Ndipo patapita nthawi, iye anasiya kuganiza za chibwenzicho. Jessica anati: “Tsopano ubwenzi wanga ndi Yehova walimba kwambiri. Ndikuyamikira kwambiri kuti iye amatipatsa malangizo ofunika panthawi yoyenera.”

      M’MUTU WOTSATIRA

      Tiyerekezere kuti mwafika poti n’kukhala ndi chibwenzi ndipo mwapeza munthu yemwe wakudololani. Kodi mungadziwe bwanji ngati munthuyo ndi wokuyenererani?

      LEMBA LOFUNIKA

      “Timafuna kuchita zinthu zonse moona mtima.”—Aheberi 13:18.

      MFUNDO YOTHANDIZA

      M’posafunika kuti muzingouza aliyense kuti muli pachibwenzi. Koma mufunikira kuuza anthu amene ali oyenera kudziwa. Anthu amenewa angakhale makolo anu ndiponso makolo a mnzanuyo.

      KODI MUKUDZIWA . . . ?

      Pamafunika kukhulupirirana kuti anthu akhale pa ubwenzi wokhalitsa. Kuchita chibwenzi mobisa kumachititsa kuti makolo anu asamakukhulupirireni, ndiponso chibwenzi choterocho chimakhala chopanda maziko abwino.

      ZOTI NDICHITE

      Ngati ndikuchita chibwenzi mobisa ndi Mkhristu mnzanga, ndiyenera kuchita izi: ․․․․․

      Ngati mnzanga akuchita chibwenzi mobisa, ndiyenera kuchita izi: ․․․․․

      Zimene ndikufuna kufunsa makolo anga pankhaniyi ndi izi: ․․․․․

      MUKUGANIZA BWANJI?

      ● Taonani mawu omwe ali m’zilembo zakuda kwambiri patsamba 22 m’buku lino. Kodi ndi mawu ati omwe akufotokoza mmene inuyo mumamvera nthawi zina?

      ● Kodi mungathane bwanji ndi maganizo anuwo popanda kuchita chibwenzi mobisa?

      ● Kodi mungatani mutadziwa kuti mnzanu akuchita chibwenzi mobisa, ndipo n’chifukwa chiyani mungasankhe kuchita zimenezo?

      [Mawu Otsindika patsamba 27]

      “Ndinathetsa chibwenzi chomwe ndinkachita mobisa. N’zoona kuti zinali zovuta kwambiri kuchita zimenezi chifukwa tsiku lililonse ndikapita ku sukulu ndinkamuona mnyamatayo. Koma Yehova Mulungu amadziwa zonse ndipo amaona zimene ifeyo sitingathe kuona. Choncho, tiyenera kumudalira.’’—Anatero Jessica”

      [Chithunzi pamasamba 25]

      Kusaulula mnzanu amene akuchita chibwenzi mobisa kuli ngati kusaulula munthu wodwala matenda a shuga amene akudya zotsekemera kwambiri mobisa

  • N’chifukwa Chiyani Sindiyenera Kugonana ndi Aliyense Mpaka N’talowa M’banja?
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
    • Mutu 5

      N’chifukwa Chiyani Sindiyenera Kugonana ndi Aliyense Mpaka N’talowa M’banja?

      “Ndimafuna n’tagonana ndi mwamuna kuti ndidziwe mmene zimakhalira.”—Anatero Kelly.

      “Ndimadzikayikira chifukwa sindinagonanepo ndi mtsikana mpaka pano.”—Anatero Jordon.

      “KODI sunagonepo ndi aliyense mpaka pano?” Funso limeneli lingakuchititseni mantha. M’madera ambiri wachinyamata amene sanagonanepo ndi aliyense amaonedwa ngati wotsalira ndiponso wopepera. N’chifukwa chake achinyamata ambiri amakhala atagonapo ndi munthu wina asanafike zaka 20.

      Kukopeka ndi Chilakolako Chawo Komanso Kulimbikitsidwa ndi Anzawo

      Ngati ndinu Mkhristu, mukudziwa kuti Baibulo limakuuzani kuti ‘mupewe dama.’ (1 Atesalonika 4:3) Komabe, mungaone kuti kudziletsa n’kovuta. Mnyamata wina dzina lake Paul, anati: “Nthawi zina ndimangoyamba kuganiza za kugonana popanda chifukwa chenicheni.” Koma dziwani kuti n’kwachibadwa kumva choncho nthawi zambiri.

      Komabe, zimachititsa manyazi kwambiri kuti anthu azikuseka nthawi zonse kuti sunagonanepo ndi munthu. Mwachitsanzo, kodi mungamve bwanji anzanu atakuuzani kuti sindinu mwamuna kapena mkazi weniweni chifukwa simunagonanepo ndi munthu? Ellen anati: “Anzako amakuchititsa kuganiza kuti kugonana n’kosangalatsa ndiponso koyenera.” Iye anapitiriza kuti: “Anthu amakukayikira ngati sunagonanepo ndi aliyense.”

      Koma pankhani yokhudza kugonana musanalowe m’banja, pali mfundo inayake imene anzanuwo sanganene. Mwachitsanzo, Maria, amene anagonapo ndi chibwenzi chake, anati: “Pambuyo pogonana naye, ndinachita manyazi kwambiri. Ndinakhumudwa kwambiri ndi zomwe tinachitazo.” Zinthu zoterezi zimachitika kawirikawiri ngakhale kuti achinyamata ambiri sazindikira zimenezi. Kunena zoona, kugonana musanalowe m’banja kumasokoneza maganizo kwambiri ndipo zotsatira zake n’zoopsa.

      Komabe, mtsikana wina dzina lake Shanda anafunsa kuti, “N’chifukwa chiyani Mulungu amapatsa achinyamata chilakolako chogonana, koma akudziwiratu kuti safunika kugonana mpaka atalowa m’banja?” Limeneli ndi funso labwino kwambiri. Koma taganizirani izi:

      Kodi chilakolako champhamvu chomwe inuyo mumakhala nacho ndi chogonana basi? Ayi. Yehova Mulungu anakulengani m’njira yoti muzitha kulakalaka ndi kuganizira zinthu zosiyanasiyana.

      Kodi mumachita panthawi yomweyo chinthu chilichonse chimene thupi lanu lafuna? Ayi, chifukwa chakuti Mulungu anakulengani m’njira yoti muzitha kudziletsa.

      Motero, kodi tikuphunzirapo chiyani? Mwina simungathe kuletsa thupi lanu kulakalaka zinthu zina, koma mungathe kudziletsa kuti musachite zinthu zomwe mukulakalakazo. Choncho, kugonana ndi munthu mukangokhala ndi chilakolako chogonana n’kulakwa ndiponso n’kupanda nzeru chifukwa zili ngati kumenya munthu nthawi iliyonse pamene mwakwiya.

      Mfundo ndi yakuti, Mulungu safuna kuti tizigwiritsa ntchito molakwika chilakolako chogonana. Baibulo limati: “Aliyense wa inu akhale woyera mwa kudziwa kusunga thupi lake m’chiyero ndi ulemu.” (1 Atesalonika 4:4) Monga mmene palili “mphindi yakukonda ndi mphindi yakudana,” palinso nthawi yomvera chilakolako chanu cha kugonana ndiponso nthawi yodziletsa. (Mlaliki 3:1-8) Kwenikweni, inuyo muli ndi udindo wonse pa zilakolako za thupi lanu.

      Koma kodi mungatani munthu wina atakusekani, n’kukufunsani modabwa kuti, “Kutereku sunagonepo ndi aliyense mpaka pano?” Zikatero musachite mantha. Munthu amene akungofuna kukunyozani mungamuuze kuti: “Inde, ndipo ndimasangalala kwambiri kuti sindinagonepo ndi munthu aliyense.” Kapena mungamuuze kuti, “Zimenezo sizikukukhudza ndipo sindikambirana ndi aliyense nkhani imeneyi.”a (Miyambo 26:4; Akolose 4:6) Komabe, mwina mungaone kuti m’pofunika kumuuza zambiri munthu amene akukufunsaniyo. Ngati ndi choncho, mungathe kum’fotokozera mfundo za m’Baibulo zimene mumatsatira pankhaniyi.

      Kodi mukuganizira njira zinanso zimene mungayankhire munthu amene wakufunsani monyoza kuti, “Kutereku sunagonepo ndi aliyense mpaka pano?” Ngati ndi choncho, lembani njira zimenezo m’munsimu.

      ․․․․․

      Mphatso Yamtengo Wapatali

      Kodi Mulungu amamva bwanji anthu akagonana asanalowe m’banja? Tayerekezerani kuti mwagula mphatso yoti mupatse mnzanu. Koma musanam’patse mphatsoyo, mnzanuyo akuitsegula, n’cholinga chongofuna kuona kuti ndi yotani. Kodi mungasangalale nazo? Ndiyeno taganizirani mmene Mulungu angamvere ngati mutagonana ndi munthu musanalowe m’banja? Iye amafuna kuti mudikire mpaka mudzalowe m’banja kuti mudzasangalale ndi mphatso ya kugonana.—Genesis 1:28.

      Kodi muyenera kutani mukakhala ndi chilakolako chogonana? Mwachidule, tinganene kuti muyenera kudziletsa ndipo mukhoza kuchitadi zimenezi. Pempherani kwa Yehova kuti akuthandizeni. Iye angakupatseni mzimu wake kuti ukuthandizeni kudziletsa. (Agalatiya 5:22, 23) Musaiwale kuti Yehova “sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.” (Salmo 84:11) Wachinyamata wina dzina lake Gordon anati: “Ndikayamba kuganiza kuti palibe cholakwika kugonana ndisanalowe m’banja ndimaganizira kaye mavuto amene angabwere pamoyo wanga wauzimu. Ndiyeno ndimaona kuti ngakhale tchimo litakhala losangalatsa chotani siliyenera kusokoneza ubwenzi wanga ndi Yehova.”

      Mfundo ndi yakuti palibe chodabwitsa kukhala wosagonana ndi munthu mpaka mutalowa m’banja. Kuchita zachiwerewere n’koopsa ndiponso kumamuchotsera munthu ulemu. Choncho, musalole kuti maganizo a dzikoli akuchititseni kuganiza kuti inuyo muli ndi vuto chifukwa chotsatira mfundo za m’Baibulo. Mukapewa kugonana ndi munthu mpaka mutalowa m’banja, mudzakhala ndi thanzi labwino, simudzavutika ndi maganizo, ndipo koposa zonse, mudzakhala ndi ubwenzi wabwino ndi Mulungu.

      WERENGANI ZAMBIRI PANKHANIYI M’BUKU LOYAMBA, MUTU 24

      [Mawu a M’munsi]

      a N’zochititsa chidwi kuti Yesu sanayankhe chilichonse Herode atam’funsa funso. (Luka 23:8, 9) Nthawi zambiri ndi bwino kusayankha mafunso opanda pake.

      LEMBA LOFUNIKA

      “Ngati wina . . . wasankha mu mtima mwake kukhalabe [wosagonana ndi munthu], achita bwino.”—1 Akorinto 7:37.

      MFUNDO YOTHANDIZA

      Pewani kucheza ndi anthu amakhalidwe oipa ngakhale atamanena kuti muli nawo chipembedzo chimodzi.

      KODI MUKUDZIWA . . . ?

      Kawirikawiri anthu achiwerewere sasintha khalidwe lawo ngakhale atalowa m’banja. Koma anthu amene amatsatira mfundo za Mulungu zamakhalidwe abwino asanalowe m’banja, amakhalanso okhulupirika kwa mwamuna kapena mkazi wawo.

      ZOTI NDICHITE

      Kuti ndisagone ndi munthu aliyense mpaka nditalowa m’banja, ndiyenera kuchita izi: ․․․․․

      Anzanga akamandivutitsa kuti ndigonane ndi munthu, ndizichita izi: ․․․․․

      Zimene ndikufuna kufunsa makolo anga pankhaniyi ndi izi: ․․․․․

      MUKUGANIZA BWANJI?

      ● N’chifukwa chiyani ena amaseka anthu amene sanagonanepo ndi munthu aliyense?

      ● N’chifukwa chiyani kukhalabe osagonana ndi munthu n’kovuta?

      ● Kodi ubwino wosagonana ndi munthu aliyense mpaka mutalowa m’banja ndi wotani?

      ● Kodi mng’ono wanu mungamufotokozere motani ubwino wosagonana ndi munthu mpaka atalowa m’banja?

      [Mawu Otsindika patsamba 51]

      “Kukumbukira nthawi zonse kuti ‘wadama kapena wopanda chiyero sadzalowa konse mu ufumu wa Mulungu,’ kumandilimbikitsa kupewa chiwerewere.”(Aefeso 5:5)—Anatero Lydia

      [Chithunzi patsamba 49]

      Zimene Munalemba

      Kodi Zotsatirapo Zake Zimakhala Zotani Kwenikweni?

      Anzanu komanso zosangalatsa zotchuka sizitchula mavuto amene angabwere chifukwa cha kugonana musanalowe m’banja. Taonani zochitika zitatu zotsatirazi. Kodi mukuganiza kuti achinyamatawa chingawachitikire n’chiyani kwenikweni?

      ● Mnyamata wina kusukulu akudzitama kuti wagonapo ndi atsikana ambirimbiri. Iye akuti n’zosangalatsa ndipo palibe vuto lililonse. Koma kodi n’chiyani kwenikweni chingachitikire mnyamatayu ndiponso atsikanawo? ․․․․․

      ● Filimu ina ikutha ndi achinyamata awiri osakwatirana akugonana ngati njira yosonyezerana chikondi. Ngati anthu atachitadi zimenezi, kodi zotsatirapo zake zingakhale zotani? ․․․․․

      ● Mwakumana ndi mnyamata winawake wokongola kwambiri ndipo akukupemphani kuti mugone naye. Iye akuti palibe aliyense amene angadziwe zimenezi. Ngati mutalola kugona naye n’kubisa zomwe mwachitazo, kodi zotsatirapo zake zingakhale zotani kwenikweni? ․․․․․

      [Chithunzi patsamba 54]

      Kugonana ndi munthu musanalowe m’banja, kuli ngati kutsegula mphatso musanapatsidwe

  • Kodi Ndingapewe Bwanji Kutengera Zochita za Anzanga?
    Mayankho a Zimene Achinyamata Amafunsa, Buku Lachiwiri
    • Mutu 15

      Kodi Ndingapewe Bwanji Kutengera Zochita za Anzanga?

      “Kusukulu kumachitika zinthu zambiri monga kusuta fodya, kumwa mankhwala osokoneza bongo, ndi zachiwerewere. Munthu umadziwa kuti zimene anzako akufuna kuti uchite ndi zoipa, koma nthawi zina umalephera kukana.”—Anatero Eve.

      ALIYENSE amafuna kuti anzake azimukonda. N’chifukwa chake anzanu ena amapezerapo mwayi pa zimenezi kuti muzichita nawo zoipa. Mwachitsanzo, ngati mwakulira m’banja lachikhristu mumadziwa kuti chiwerewere ndiponso kuledzera n’zolakwika. (Agalatiya 5:19-21) Komabe, anzanu angakukakamizeni kuti muzichita zimenezi. Kodi iwowo anayamba bwanji khalidwe loipali? Ambiri amachita zimenezi chifukwa chotengera anzawo. Amafuna kuti anzawo aziwakonda, choncho amangochita zimene anzawowo akufuna. Kodi inunso mumatero kapena mumakana molimba mtima?

      Nthawi inayake, Aroni, mchimwene wake wa Mose anagonjera zofuna za anthu. Aisiraeli atamuunjirira n’kumuumiriza kuti awapangire fano, iye anagonja n’kupanga zimene iwo amafunazo. (Eksodo 32:1-4) N’zodabwitsa kuti munthu amene anauza Farao molimba mtima uthenga wochokera kwa Mulungu, anagonja kwa Aisiraeli anzakewo. (Eksodo 7:1, 2, 16) Ngakhale kuti Aroni analankhulana ndi mfumu ya Aiguputo mopanda mantha, iye analephera kulankhula molimba mtima kwa Aisiraeli anzake.

      Kodi inunso zimakuvutani kukana, ena akamakuumirizani kuchita zinthu zoipa? Inunso mutha kukana molimba mtima, anzanu akakuumirizani kuchita zimene iwo akufuna. Kuganiziratu zinthu zimene anzanu angakukakamizeni kungakuthandizeni kwambiri. Mfundo zinayi zotsatirazi zikuthandizani kuchita zimenezi.

      1. Konzekerani. (Miyambo 22:3) N’zosavuta kudziwiratu zinthu zimene anzanu angakuumirizeni kuchita. Mwachitsanzo, mukhoza kuona anzanu a kusukulu akubwera patsogolo panu akusuta fodya. Mukhoza kudziwiratu kuti akukakamizani kusuta. Koma mutakonzekereratu, sizingakuvuteni kukana.

      2. Dzifunseni. (Aheberi 5:14) Mungadzifunse kuti, ‘Ndikachita zimene anzangawa akuchita, kodi mumtima mwanga ndimva bwanji?’ Mukachita nawo zimenezo, anzanuwo angakukondeni koma kodi kenako mungamve bwanji mukakhala ndi makolo anu kapena Akhristu anzanu? Kodi mungakonde kusangalatsa anzanu a kusukulu m’malo mosangalatsa Mulungu?

      3. Sankhani zochita. (Deuteronomo 30:19) Mtumiki wa Mulungu aliyense ayenera kusankha kukhala wokhulupirika n’kupeza madalitso kapena kukhala wosakhulupirika n’kukumana ndi mavuto. Anthu monga Yosefe, Yobu ndi Yesu anasankha mwanzeru pomwe Kaini, Esau ndi Yudasi sanasankhe bwino. Inunso muyenera kusankha zoyenera kuchita.

      4. Nenani maganizo anu. Mwina mungaganize kuti kunena maganizo anu n’kovuta, komatu n’kosavuta. Ngati mwaganizira kale kuipa kwake ndipo mwasankha kale zochita, simungavutike kunena maganizo anu. (Miyambo 15:23) Sikuti mukuchita kufunikira kulalikira anzanuwo ayi. Kungonena kuti ayi kungakhale kokwanira. Kapena ngati mukufuna kuwatsimikizira kuti simusintha maganizo anu, munganene kuti:

      “Sindikufuna kuti zimenezo zindikhudze.”

      “Sindingachite zimenezo.”

      “Inunso mukudziwa kuti sindingachite zimenezo.”

      Kuyankha mwamphamvu ndiponso molimba mtima kungachititse kuti anzanu asiye kukuvutitsani. Komabe, kodi mungatani ngati anzanu akukunyozani? Bwanji ngati atakunenani kuti, “Ndiwe wamantha eti?” Akanena zimenezi musadabwe, chifukwa iwo akungofuna kukunyengererani. Koma kodi mungawayankhe bwanji? Pali njira zitatu zimene mungawayankhire.

      ● Vomerezani zimene akunenazo. (“Simukunama, ndinedi wamantha.” Kenako fotokozani mwachidule chifukwa chimene mukuchitira mantha.)

      ● Ingokanani kuti simungachite zimenezo koma osanena zambiri.

      ● Apanikizeni. Fotokozani chifukwa chimene mukukanira, ndipo asonyezeni kuti zimene akuchitazo n’zopanda nzeru. (“Ndimakuonani ngati anthu ozindikira oti simungasute fodya.”)

      Anzanuwo akapitiriza kukuvutitsani, ingochokani chifukwa mukakhalabe pomwepo zinthu zikhoza kuipa kwambiri. Dziwani kuti ngakhale mwachokapo, simunagonje chifukwa simunalole kuchita zimene iwo akufuna.

      Anzanu ena angakunyozeni kuti simutha kusankha nokha zochita. Koma zimenezo si zoona chifukwa Yehova amafuna muzindikire kuti kuchita chifuniro chake n’kofunika kwambiri. (Aroma 12:2) Ndipo musalole kuti anzanu akusandutseni kachidole. (Aroma 6:16) Choncho, yesetsani kuchita zimene mukudziwa kuti n’zolondola.

      Kunena zoona n’zosatheka kupeweratu kuvutitsidwa ndi anzanu. Komabe mutha kusankha zimene mukufuna kuchita. Muthanso kunena maganizo anu kapena kuchita zilizonse zimene mungathe kuti anzanu asamakuvutitseni. Ndipo dziwani kuti ndi udindo wanu kusankha zochita.—Yoswa 24:15.

      WERENGANI ZAMBIRI PANKHANIYI M’BUKU LOYAMBA, MUTU 9

      M’MUTU WOTSATIRA

      Kodi mumachita zinthu zinazake mwamseri? Kodi mukuganiza ndi bwino kuti makolo anu adziwe zimene mumachita mseri?

      LEMBA LOFUNIKA

      “Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: Koma mnzawo wa opusa adzapwetekedwa.”—Miyambo 13:20.

      MFUNDO YOTHANDIZA

      Kuti mukhale wolimba mtima, werengani nkhani za atumiki a Yehova a masiku ano amene akhalabe okhulupirika povutitsidwa.

      KODI MUKUDZIWA  . . . ?

      Anzanu ambiri amene mumaphunzira nawo mudzasiyana nawo mukadzamaliza sukulu. Mwinanso ena adzakuiwalani ndi dzina lomwe. Koma makolo ndi abale anu komanso Yehova Mulungu, sadzakuiwalani mpaka kalekale.—Salmo 37:23-25.

      ZOTI NDICHITE

      Pokonzekera kukana zimene anzanga akufuna kuti ndichite, ndizichita izi: ․․․․․

      Anzanga akandikakamiza kuti ndichite zinthu zoipa, ndizichita izi: ․․․․․

      Zimene ndikufuna kufunsa makolo anga pankhaniyi ndi izi: ․․․․․

      MUKUGANIZA BWANJI?

      ● Kodi njira zinayi zimene zafotokozedwa m’mutu uno, zingakuthandizeni bwanji?

      ● Kodi chingachitike n’chiyani ngati mutalolera zimene anzanu akufuna kuti muchite?

      ● Kodi mungakane bwanji ngati anzanu akukuumirizani kuchita zinthu zoipa?

      [Mawu Otsindika patsamba 131]

      “Anzanga ambiri amadziwa kuti ndine wa Mboni ndipo amandipatsa ulemu. Akafuna kukambirana zinthu zosayenera, amandiuza kuti, ‘Mike tikufuna kuyamba kukambirana zathu, ndiye ngati ukufuna, utha kuchoka.”—Anatero Mike

      [Tchati pamasamba 132, 133]

      Zimene Munalemba

      mmene mungakonzekerere Chitsanzo cha

      konzekerani

      Kodi anzanga angandikakamize kuchita chiyani? Kusuta fodya.

      Kodi zimenezi zingachitikire kuti? Kubwalo la mpira.

      ↓ ↓

      Kodi nditalola ← dzifunseni → Kodi nditakana,

      kusuta fodya, chingachitike

      chingachitike n’chiyani?

      n’chiyani?

      Yehova ndiponso makolo anga Anzanga angandigemule

      sangasangalale nazo. kapena kundinyoza.

      Ndingawononge chikumbumtima Ena sangafune kucheza nane.

      changa. Zingadzandivute Koma ndingasangalatse Yehova

      kukana nthawi ina. ndiponso ndingapitirize kukhala

      munthu wamakhalidwe abwino.

      ↓ ↓

      Ngati ← 3 Sankhani Zochita → Ndidzakana

      ndidzasute fodya, kusuta fodya

      chidzakhala chifukwa chifukwa chakuti:

      chakuti:

      Sindikukonzekera choti Ndikudziwa kuti Yehova

      ndidzachite anzanga amadana nazo ndiponso

      akadzandikakamiza kusuta kusuta kukhoza

      fodya. Kapena chifukwa kundidwalitsa.

      choti ndimaona kuti

      kukondweretsa anzanga

      n’kofunika kwambiri kuposa

      kukondweretsa Yehova.

      ↓ ↓

      ← 4 Nenani Maganizo Anu → Ndidzachita izi:

      Kukana kenako

      n’kuchokapo.

      Anzanu akamakunenani

      Anzanga akanena kuti: “Sutako pang’ono.

      Kapena ukuchita mantha eti?”

      Ndingachite izi:

      kuvomereza kukana koma kuwapanikiza

      osanena zambiri

      “Simukunama, “Musavutike kundipatsa “Sindikufuna, inetu

      sindifuna kusuta ine fodyayo.” ndimakutengani ngati

      fodya chifukwa ndinu ozindikira oti

      ndimaopa matenda simungasute fodya.”

      a khansa.”

      DZIWANI IZI: Chokani pamalopo mwamsanga. Mukakhalabe pomwepo, n’zosavuta kuti muyambe kuchita zimene iwo akufunazo. Tsopano, lembani zimene mungachite pa pepala limene lili patsamba lotsatirali.

      mmene mungakonzekerere Koperani izi:

      1 Konzekerani

      Kodi anzanga angandikakamize kuchita chiyani? ․․․․․

      Kodi zimenezi zingachitikire kuti? ․․․․․

      ↓ ↓

      Kodi nditalola, ← 2 Dzifunseni → Kodi nditakana,

      chingachitike chingachitike

      n’chiyani? n’chiyani?

      ․․․․․ ․․․․․

      ↓ ↓

      Ndikadzalolera, ← 3 Sankhani Zochita → Ndidzakana

      chidzakhala chifukwa chakuti:

      chifukwa chakuti:

      ․․․․․ ․․․․․

      ↓ ↓

      ← 4 Nenani Maganizo Anu Ndidzachita izi: →

      ․․․․․ ․․․․․

      Anzanu akamakunenani

      Mnzanga akanena kuti: ․․․․․

      Ndingachite izi:

      kuvomereza kukana koma kuwapanikiza

      osanena zambiri

      ․․․․․ ․․․․․ ․․․․․

      Yeserani ndi makolo anu kapena munthu wina wamkulu zimene mungachite.

      [Chithunzi patsamba 135]

      Mukamalolera kuchita zimene anzanu akufuna, mumakhala ngati kachidole kawo

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena