Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • scl tsamba 40-41
  • Kulapa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kulapa
  • Malemba Othandiza pa Moyo wa Chikhristu
Malemba Othandiza pa Moyo wa Chikhristu
scl tsamba 40-41

Kulapa

N’chifukwa chiyani munthu aliyense ayenera kulapa machimo ake komanso kupempha Yehova kuti amukhululukire?

Aro 3:23; 5:12; 1Yo 1:8

Onaninso Mac 26:20

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Lu 18:9-14​—Yesu ananena fanizo losonyeza kufunika kolapa machimo athu komanso kupemphera kwa Yehova kuti azitithandiza

    • Aro 7:15-25​—Ngakhale kuti Paulo anali mtumwi komanso munthu wachikhulupiriro cholimba, komabe ankalimbana ndi maganizo ofuna kuchita zoipa

Kodi Baibulo limanena kuti Yehova amawaona bwanji anthu amene alapa?

Eze 33:11; Aro 2:4; 2Pe 3:9

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Lu 15:1-10​—Yesu anagwiritsa ntchito fanizo posonyeza kuti Yehova ndi angelo kumwamba amasangalala munthu wochimwa akalapa

    • Lu 19:1-10​—Zakeyu, mkulu wa okhometsa msonkho komanso wachinyengo, analapa n’kusintha zochita zake, ndipo Yehova anamukhululukira komanso anakhala ndi mwayi wodzapulumutsidwa

Kodi tingasonyeze bwanji kuti talapadi mochokera pansi pa mtima?

Eze 18:21-23; Mac 3:19; Aef 4:17, 22-24; Akl 3:5-10

Onaninso 1Pe 4:1-3

Kodi kudziwa choonadi molondola kumamuthandiza bwanji munthu kuti alapedi mochokera pansi pa mtima?

Aro 12:2; Akl 3:9, 10; 2Ti 2:25

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • Mac 17:29-31​—Mtumwi Paulo anafotokozera anthu a ku Atene chifukwa chake kulambira mafano ndi chizindikiro cha umbuli, ndipo anawalimbikitsa kuti alape

    • 1Ti 1:12-15​—Mtumwi Paulo asanadziwe choonadi molondola chokhudza Yesu Khristu, anachita machimo akuluakulu mosadziwa

Kodi kulapa kuli ndi ubwino wotani?

Mko 1:14, 15; Lu 24:45-47; Mac 2:38; 17:30; 20:21

N’chifukwa chiyani sitiyenera kukayikira kuti tikalapa, Yehova angathe kutikhululukira ngakhale pamene tachimwa maulendo angapo?

Yes 1:18; Aga 6:1; 1Yo 2:1

Kodi Yehova amachita bwanji zinthu ndi anthu amene alapa machimo awo n’kusintha zochita zawo?

Sl 32:5; Miy 28:13; 1Yo 1:9

Onaninso “Chifundo”

Kodi timadziwa bwanji kuti kulapa kumaphatikizapo zambiri kuposa kungodzimvera chisoni kapena kupepesa basi?

2Mb 7:14; Miy 28:13; Eze 18:30, 31; 33:14-16; Mt 3:8; Mac 3:19; 26:20

  • Nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni:

    • 2Mb 33:1-6, 10-16​—Ngakhale kuti Mfumu Manase anachita zoipa zambiri kwa nthawi yaitali, iye anadzichepetsa n’kulapa mochokera pansi pa mtima, anapemphera mosalekeza komanso anasintha zochita zake

    • Sl 32:1-6; 51:1-4, 17​—Mfumu Davide anasonyeza kulapa pamene anaulula machimo ake, kupemphera kwa Yehova kuti amukhululukire komanso kudzimvera chisoni chifukwa cha zimene anachitazo

N’chifukwa chiyani tiyenera kukhululukira anthu amene atilakwira?

Mt 6:14, 15; 18:21, 22; Lu 17:3, 4

Onaninso “Kukhululuka”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena