Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w12 3/1 tsamba 32
  • Kodi Yesu Mumamudziwa Kuti Ndi Ndani?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Yesu Mumamudziwa Kuti Ndi Ndani?
  • Nsanja ya Olonda—2012
Nsanja ya Olonda—2012
w12 3/1 tsamba 32

Kodi Yesu Mumamudziwa Kuti Ndi Ndani?

Kodi mukamva za Yesu mumamuganizira ali kamwana kakhanda, munthu amene akuphedwa kapena Mfumu yaulemelero?

Baibulo limanena kuti panopa Yesu ndi mfumu yamphamvu. Koma kodi zimenezi zikukukhudzani bwanji?

Anthu ambiri amakhulupirira kuti Yesu anawafera. Komabe, kodi imfa ya munthu mmodzi, yomwenso inachitika zaka pafupifupi 2,000 zapitazo, ingatikhudze bwanji masiku ano?

Tikukuitanani kuti mudzamve mayankho a m’Malemba a mafunso amenewa. Mfundo zimenezi zidzafotokozedwa pa mwambo wokumbukira imfa ya Yesu umene Mboni za Yehova zidzakhale nawo. Chaka chino mwambo umenewu udzachitika Lachinayi, pa April 5, dzuwa litalowa.

Mukafuna kudziwa nthawi komanso malo amene kudzachitikire mwambowu, funsani Mboni za Yehova za m’dera lanu.

Mlungu wotsatira, mwambo wokumbukira imfa ya Yesu utachitika, Mboni za Yehova zidzakambanso nkhani yochititsa chidwi yochokera m’Baibulo. Nkhaniyi idzakhala ya mutu wakuti: “Kodi Mapeto Ayandikiradi?” Nkhani imeneyi idzakambidwa padziko lonse lapansi ndi cholinga chothandiza anthu onse amene amakonda choonadi komanso omwe akufuna kudziwa zambiri za Yesu. Inunso mukuitanidwa kuti mudzamvetsere nkhaniyi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena