Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 47
  • Kodi Ziwanda Zilipodi?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Ziwanda Zilipodi?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Zimene Tiyenera Kudziwa Zokhudza Angelo
    Zimene Baibulo Limaphunzitsa
  • Yesu Ali ndi Mphamvu Kuposa Ziwanda
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
  • Mmene Zochita za Angelo Komanso Ziwanda Zimakhudzira Moyo Wathu
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
  • Kodi Zochita za Angelo Ndiponso Ziwanda Zimakhudza Bwanji Anthufe?
    Nsanja ya Olonda—2012
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 47

Kodi Ziwanda Zilipodi?

Yankho la m’Baibulo

Inde zilipodi. Ziwanda ndi “angelo amene anachimwa,” ndipo anaukira Mulungu. (2 Petulo 2:4) Mngelo woyambirira amene anakhala chiwanda ndi Satana Mdyerekezi ndipo Baibulo limamutchula kuti “wolamulira ziwanda.”—Mateyu 12:24, 26.

Angelo amene sanamvere m’nthawi ya Nowa

Baibulo limanena za angelo amene sanamvere Mulungu Chigumula cha m’nthawi ya Nowa chisanachitike. Limanena kuti: “Ana a Mulungu woona anayamba kuona kuti ana aakazi a anthu anali okongola. Chotero, anayamba kudzitengera okha akazi alionse amene anawasankha.” (Genesis 6:2) Angelo oipawo “anasiya malo awo okhala” kumwamba n’kuvala matupi aumunthu n’cholinga choti achite chiwerewere ndi akazi.—Yuda 6.

Chigumula chitayamba, angelo oipawo anavula matupi aumunthu aja n’kuthawira kumwamba. Komabe Mulungu sanawalole kuti akhalenso m’gulu la angelo ake. Zitatero angelowa sanathenso kuvala matupi a anthu ndipo chimenechi chinali chilango chawo.—Aefeso 6:11, 12.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena