LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lfb phunzilo 10 tsa. 30-tsa. 31 pala. 5
  • Kumbukilani Mkazi wa Loti

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kumbukilani Mkazi wa Loti
  • Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Mkazi Wa Loti Anayang’ana Kumbuyo
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Thandizani Ena Kulimbana na Nkhawa
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2019
  • Kumbukilani Mkazi wa Loti
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
lfb phunzilo 10 tsa. 30-tsa. 31 pala. 5
Mkazi wa Loti asanduka culu camcele pamene Loti na ana ake aakazi athaŵa kucoka mu Sodomu

PHUNZILO 10

Kumbukilani Mkazi wa Loti

Loti anali kukhala na Abulahamu, atate ake aang’ono, m’dziko la Kanani. M’kupita kwa nthawi, Abulahamu na Loti anakhala na ziweto zambili cakuti kunalibe malo okwanila odyetselako ziweto zawo. Conco, Abulahamu anauza Loti kuti: ‘Sitingapitilize kukhalila pamodzi. Sankha malo amene ungakonde kukhalako, ndipo ine ndidzapita kumbali ina.’ Abulahamu anacita zinthu mosadzikonda, si conco?

Ndiyeno, Loti anaona malo abwino ngako kufupi na mzinda wa Sodomu. Kunali madzi ambili komanso udzu wobiliŵila. Anasankha malowo na kukukila kumeneko na banja lake. Pambuyo pake, anakukila mkati mwa mzinda wa Sodomu.

Anthu a mu Sodomu, komanso a mumzinda woyandikana nawo wa Gomora, anali oipa kwambili. Ndiye cifukwa cake Yehova anaganiza zowononga mizinda imeneyo. Koma Mulungu anafuna kupulumutsa Loti na banja lake. Conco, anatuma angelo aŵili kukawacenjeza. Angelowo anati: ‘Fulumilani! Tulukani mu mzinda uno, cifukwa Yehova adzauwononga.’

Koma Loti sanacoke pa nthawi imeneyo. Anali kungowaya-waya. Pamenepo angelowo anagwila pa dzanja Loti, mkazi wake, komanso ana ake aŵili aakazi na kuwatulutsa mumzindawo. Kenako anawauza kuti: ‘Thaŵani kuti mupulumutse moyo wanu, ndipo musayang’ane kumbuyo. Mukayang’ana kumbuyo, mudzafa!’

Moto na sulufule zikugwa pa Sodomu na Gomora

Atafika ku mzinda wa Zowari, Yehova anagwetsa moto na sulufule pa Sodomu na Gomora. Mizinda iŵili imeneyo inanyekelatu. Mkazi wa Loti sanamvele Yehova. Anayang’ana kumbuyo na kusanduka culu camcele! Koma Loti na ana ake aakazi anapulumuka cifukwa comvela Yehova. Anali acisoni kwambili cifukwa mkazi wa Loti sanamvele. Titengapo phunzilo lakuti kumvela Yehova ni cinthu cofunika kwambili.

“Kumbukilani mkazi wa Loti.”—Luka 17:32

Mafunso: N’cifukwa ciani Yehova anawononga Sodomu na Gomora? N’cifukwa ciani mkazi wa Loti anasanduka culu camcele?

Genesis 13:1-13; 19:1-26; Luka 17:28, 29, 32; 2 Petulo 2:6-9

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani