LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp17 na. 5 tsa. 16
  • Kodi Baibo Imakamba Ciani?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Baibo Imakamba Ciani?
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi zidzatheka kuti padzikoli pakhale mtendele?
  • Kodi n’zotheka kukhala na mtendele weni-weni wa m’maganizo lomba?
  • Kodi Baibo Imakamba Ciani?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
  • Kodi Mulungu amamvela bwanji akaona kuti muvutika?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2018
  • Mtendele Kodi Mungaupeze Bwanji?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • Kuyankha Mafunso a m’Baibo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2017
wp17 na. 5 tsa. 16
Zida zankhondo ziwonongewa

Zida zonse zankhondo zidzawonongewa

Kodi Baibo Imakamba Ciani?

Kodi zidzatheka kuti padzikoli pakhale mtendele?

Kodi mungayankhe bwanji?

  • Inde

  • Iyai

  • Kapena

Zimene Baibo imakamba

Mu ulamulilo wa Yesu Khristu, “padzakhala mtendele woculuka kwa nthawi yonse pamene mwezi udzakhalepo,” kutanthauza kwamuyaya.—Salimo 72:7.

Mfundo zina zimene Baibo imakamba

  • Anthu oipa adzacotsedwa padziko lapansi, koma anthu abwino “adzasangalala ndi mtendele woculuka.” —Salimo 37:10, 11.

  • Mulungu adzathetsa nkhondo zonse.—Salimo 46:8, 9.

Kodi n’zotheka kukhala na mtendele weni-weni wa m’maganizo lomba?

Anthu ena amakhulupilila kuti . . .

n’zosatheka kukhala na mtendele weni-weni wa m’maganizo m’dziko lino lodzala ndi mavuto na kupanda cilungamo. Nanga imwe muganiza bwanji?

Zimene Baibo imakamba

Ngakhale lomba, anthu amene ni mabwenzi a Mulungu angakhale na “mtendele wa Mulungu umene umaposa kuganiza mozama kulikonse.”—Afilipi 4:6, 7.

Mfundo zina zimene Baibo imakamba

  • Mulungu analonjeza kuti adzacotsapo mavuto na kupanda cilungamo. Adzapanga zinthu zonse kukhala zatsopano.—Chivumbulutso 21:4, 5.

  • Tingakhale na mtendele wa m’maganizo ngati tisamalila ‘zosoŵa zathu zauzimu.’—Mateyu 5:3.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 3 m’buku iyi, Zimene Baibulo Ingatiphunzitse, yofalitsidwa na Mboni za Yehova

Bukuyi ipezekanso pa webusaiti ya www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani