LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 3/13 tsa. 1
  • Konzekelani Cikumbutso ndi Mtima Wacimwemwe

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Konzekelani Cikumbutso ndi Mtima Wacimwemwe
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Nkhani Zofanana
  • Cifukwa Cake Timacita Mgonelo wa Ambuye
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Kodi Mukukonzekela Cikumbutso?
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Yehova Amadalitsa Kuyesetsa Kwathu Kuti Ticite Cikumbutso
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
  • Kodi Mukukonzekela Cikumbutso?
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
Onaninso Zina
Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
km 3/13 tsa. 1

Konzekelani Cikumbutso ndi Mtima Wacimwemwe

1. Kodi nyengo ya Cikumbutso ndi nthaŵi yapadela yocita ciani?

1 Cikumbutso cimene cidzacitika pa Ciŵili, March 26, cidzatipatsa mwai wofunika kwambili wokhalila acimwemwe pa zimene Mulungu anaticitila kuti atipulumutse. (Yes. 61:10) Mtima wacimwemwe udzatithandiza kukhala okonzekela bwino kwambili ngakhale Cikumbutso cisanacitike. Kodi zimenezi zingatheke bwanji?

2. N’ciani cimatilimbikitsa kuti tikonzekele za Cikumbutso?

2 Kukonzekela Cikumbutso: Mgonelo wa Ambuye ndi mwambo waukulu kwambili koma wosavuta kucita. Ngakhale n’conco, pamafunika kukonzekela pasadakhale kuti tisanyalanyaze mfundo zonse zofunika kwambili. (Miy. 21:5) Muyenela kusankha nthawi ndi malo oyenelela pamene padzacitikila mwambo umenewu. Muyenela kukhala ndi ziphiphilitso zoyenela. Malo amene padzacitikila Cikumbutso ayenela kuyeletsedwa ndi kukonzedwa bwino-bwino. Mkambi ayenela kukonzekela bwino, ndipo abale opeleka ziphiphilitso komanso akalinde ayenela kukhala ndi malangizo a mmene adzacitila zimenezi. N’zosakaikitsa kuti zambili zimene tachulapa mwacita kale. Timakonzekela m’njila yotelo cifukwa cakuti timayamikila mphamvu yopulumutsa ya dipo imeneyi.—1 Pet. 1:8, 9.

3. Kodi tingakonzekeletse bwanji mitima yathu kaamba ka Mgonelo wa Ambuye?

3 Kukonzekeletsa Mitima: N’cinthu cofunika kwambili kukonzekeletsa mitima yathu kuti timvetse tanthauzo la Cikumbutso. (Ezara 7:10) Kuti ticite zimenezi tiyenela kupatula nthawi yosinkha-sinkha Malemba amene asankhidwa kuti tiŵelenge panyengo ya Cikumbutso ndi kuganizila za masiku omaliza a umoyo wa Yesu padziko lapansi. Kuganizila za mzimu wodzipeleka wa Yesu kudzatilimbikitsa kuti tim’tsatile.—Agal. 2:20.

4. Kodi ndi phindu liti maka-maka la dipo limene limakupatsani cimwemwe cacikulu?

4 Imfa ya Kristu imaonetsa kuti Yehova ndi woyenela kulamulila. Imatimasula ku ucimo ndi imfa. (1 Yoh. 2:2) Imatipatsa mwai wokhala paubwenzi wabwino ndi Mulungu komanso mwai wolandila moyo wosatha. (Akol. 1:21, 22) Imatithandizanso kuti tipitilize kucita zinthu mogwilizana ndi kudzipeleka kwathu kwa Yehova ndi kukhalabe olimba monga ophunzila a Kristu. (Mat. 16:24) Conco lekani kuti cimwemwe canu cipitilize kuonjezeka pamene mukonzekela Cikumbutso ndi kupezekapo!

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani