LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 10/15 tsa. 3
  • Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
km 10/15 tsa. 3

Kubweleza za m’Sukulu ya Ulaliki

Tidzakambilana mafunso otsatilawa pa Sukulu ya Ulaliki kuyambila mlungu wa October 26, 2015.

  1. Kodi nkhani yopezeka pa 2 Mafumu 13:18, 19 ikuonetsa bwanji kufunika kocita khama potumikila Mulungu? [Sept. 7, w10 4/15 tsa. 26 ndime 11]

  2. Ndani anali kulamulila mu Israeli pamene Yona anali mneneli? Nanga tingaphunzile ciani pa utumiki wa Yona tikaona zimene zili pa 2 Mafumu 14:23-25? [Sept. 7, w09 1/1 tsa. 25 ndime 4]

  3. Kodi Ahazi anaonetsa bwanji kuti sanakhulupilile mau amene Mulungu anakamba kudzela mwa mneneli Yesaya? Nanga tingadzifunse funso liti tisanapange zosankha zikuluzikulu? (2 Maf. 16:7) [Sept. 14, w13 11/15 tsa. 17 ndime 5]

  4. Kodi Rabisake anagwilitsila nchito njila iti potsutsa anthu a Mulungu imenenso anthu otsutsa masiku ano amaigwilitsila nchito? Nanga ndi khalidwe liti limene lingatithandize kukana mabodza a anthu otsutsa? (2 Maf. 18:22, 25) [Sept. 14, w10 7/15 tsa. 13 ndime 3-4]

  5. Kodi citsanzo ca Yosiya ca kudzicepetsa, cingatithandize bwanji kupindula tikamaŵelenga ndi kuphunzila Baibulo? (2 Maf. 22:19, 20) [Sept. 21, w00 3/1 tsa. 30 ndime 2]

  6. Kodi zinthu zakale zimene zinapezeka zikutsimikizila bwanji kuti mafumu aŵili ochulidwa pa 2 Mafumu 25:27-30 analikodi? [Sept. 28, w12 6/1 tsa. 5 ndime 2-3]

  7. Ndi zinthu zitatu ziti zimene Yabezi anapempha Yehova, ndipo zikutiphunzitsa ciani pankhani ya pemphelo? (1 Mbiri 4:9,10) [Oct. 5, w10 10/1 tsa. 23]

  8. Kodi zotsatilapo za nkhondo yochulidwa pa 1 Mbiri 5:18-22, zingatilimbikitse bwanji kupitiliza kumenya nkhondo ya kuuzimu? [Oct. 12, w05 10/1 tsa. 9 ndime 7]

  9. N’ciani cinathandiza Davide kumvetsa ndi kulemekeza mfundo ya m’lamulo la Yehova la kupatulika kwa magazi? Nanga citsanzo cake cingatilimbikitse kucita ciani? (1 Mbiri 11:17-19) [Oct. 19, w12 11/15 mas. 6-7 ndime 12-14]

  10. Kodi Davide sanacite ciani pamene anali kusamutsila likasa lapangano ku Yerusalemu? Nanga tingaphunzilepo ciani pankhaniyi? (1 Mbiri 15:13) [Oct. 26, w03 5/1 mas. 10-11 ndime 11-13]

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani