LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb16 September tsa. 3
  • “Muzitsatila Cilamulo ca Yehova”

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • “Muzitsatila Cilamulo ca Yehova”
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
  • Nkhani Zofanana
  • Salimo 37:4—“Udzikondweretsenso mwa Yehova”
    Kufotokoza Mavesi a m’Baibulo
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
mwb16 September tsa. 3

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU | SALIMO 119

“Muzitsatila Cilamulo ca Yehova”

Kutsatila cilamulo ca Yehova kutanthauza kumvela malangizo a Mulungu ndi mtima wonse. M’Baibulo muli zitsanzo zambili za anthu amene anali kutsatila ndi kudalila cilamulo ca Yehova monga mmene wamasalimo anacitila.

Wamasalimo ayenda na ndodo

Kutsatila cilamulo ca Mulungu n’kumene kumatipatsa cimwemwe ceni-ceni

119:1-8

Yoswa aŵelenga mpukutu

Yoswa anali kudalila kwambili malangizo a Yehova. Anadziŵa kuti ngati afuna kukhala wacimwemwe ndi kuti zinthu zimuyendele bwino, anafunika kukhulupilila Yehova na mtima wake wonse

Mawu a Mulungu amatithandiza kuti tikhale olimba mtima polimbana ndi ziyeso

119:33-40

Yeremiya apemphela

Yeremiya anaonetsa kuti anali wolimba mtima ndipo anadalila Yehova ngakhale kuti anakumana ndi mavuto. Anapitiliza kukhala na umoyo wosalila zambili ndi kugwila nchito imene anapatsidwa.

Kudziŵa bwino Mawu a Mulungu kumatithandiza kulalikila molimba mtima

119:41-48

Paulo alalikila Bwanamkubwa Felike

Paulo sanacite mantha kuuza aliyense uthenga wocokela kwa Mulungu. Iye anali kukhulupilila kuti Yehova adzamuthandiza kulalikila molimba mtima kwa Bwanamkubwa Felike

Wamasalimo ayenda na ndodo

Ni pa zocitika ziti pamene ningaonetse kulimba mtima polaliki ena?

  • Kusukulu

  • Kunchito

  • Kwa Acibale

  • Kwina

Salimo 119 inalembedwa motsatila alifabeti. Zimenezi ziyenela kuti zinali kuthandiza anthu kuti azikumbukila salimoli mosavuta. Buku la Masalimo lili ndi ndime 22, ndipo ndime iliyonse ili ndi mavesi 8. M’ndime iliyonse, mavesi onse 8 amayamba ndi cilembo cimodzimodzi ca Ciheberi. Popeza kuti alifabeti ya Ciheberi ili na zilembo 22, salimo imeneyi ili na mavesi 176, ndipo ndiyo salimo yaitali kwambili m’Baibulo.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani