LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb16 September tsa. 2
  • Mukapeza Mwana Panyumba

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mukapeza Mwana Panyumba
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
  • Nkhani Zofanana
  • Kulemekezana m’Banja
    Galamuka!—2024
  • Makolo, Kodi Mukuthandiza Ana Anu Kupita Patsogolo Kuti Akabatizike?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • Kodi Muyenela Kucita Ciyani Kuti Banja Lanu Likhale Lacimwemwe?—Mbali 2
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Msonkhano (2016)
mwb16 September tsa. 2

UMOYO WATHU WACIKHIRISTU

Mukapeza Mwana Panyumba

Alongo aŵili alalikila mayi ndi mwana wake

Tikapeza mwana panyumba, tingamuuze kuti tifuna kukambako ndi makolo ake. Kucita zimenezi kumaonetsa kuti tikulemekeza makolo ake amene ali ndi udindo womulangiza. (Miy. 6:20) Mwana akatiuza kuti tiloŵe m’nyumba, tisathamangile kulowa. Ngati makolo palibe, tingapeze nthawi ina yopitakonso.

Ngakhale mwanayo atakhala wamkulu, mwina wa zaka zapakati pa 15 ndi 19, tingacite bwino kumupempha kuti tikambe na makolo ake. Ngati makolowo palibe, tingamufunse ngati amamuvomeleza kudzisankhila zinthu zoŵelenga. Ngati amamuvomeleza, tingamugaŵile cofalitsa kapena kumuuza za webusaiti yathu ya jw.org.

Pocita ulendo wobwelelako kwa wacicepele amene waonetsa cidwi, tingamuuze kuti tifuna kuonana ndi makolo ake. Kucita zimenezi kudzatipatsa mwayi wofotokozela makolowo colinga ca ulendo wathu, ndiponso tidzatha kuwafotokozela malangizo odalilika opezeka m’Baibulo okhudza banja. (Sal. 119:86, 138) Kucitila ulemu makolo ndi kuwaganizila kudzatithandiza kukhala alaliki abwino, ndipo kudzatipatsanso mpata wina wolalikila ena m’banjalo.—1Pet 2:12.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani