CUMA COCOKELA M’MAU A MULUNGU | YESAYA 34-37
Hezekiya Anafupidwa Cifukwa ca Cikhulupililo Cake
Mfumu Senakeribu ya Asuri inatuma Rabisake ku Yerusalemu kukauza Hezekiya kuti angopeleka mzindawo. Asuri anaseŵenzetsa njila zosiya-nasiyana pofuna kuwayofya Ayuda kuti adzipeleke popanda kumenyana nawo.
Kuwapatula. Aiguputo sangakuthandizeni konse.—Yes. 36:6
Kuwakaikitsa. Yehova sadzakumenyelani nkhondo cifukwa munam’khumudwitsa.—Yes. 36:7, 10
Kuwayofya. Mwacepa kutali-tali kwa asilikali amphamvu a Asuri.—Yes. 36:8, 9
Kuwanyengelela. Mukadzipeleka kwa Asuri zinthu zidzakuyendelani bwino.—Yes 36:16, 17
Hezekiya anaonetsa cikhulupililo cosagwedela mwa Yehova
37:1, 2, 14-20, 36
Anacita zonse zotheka kuti ateteze mzinda kwa adani odzauzinga
Anapemphela kwa Yehova kuti awalanditse, ndi kulimbikitsanso anthu ake kucita cimodzi-modzi
Yehova anamufupa mwa kutumiza mngelo amene anapha asilikali acisuri 185,000 usiku umodzi cabe