LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 February tsa. 4
  • Muziseŵenzentsa Zofalitsa Zanu Mwanzelu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Muziseŵenzentsa Zofalitsa Zanu Mwanzelu
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • “Ndidzatenga Mabuku Anu Mukatenga Anga”
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 February tsa. 4
Mzimayi amvetsela pamene Mboni za Yehova zimugaŵila kabuku ka Uthenga wabwino wocokela kwa Mulungu

UMOYO WACIKHRISTU

Muziseŵenzentsa Zofalitsa Zanu Mwanzelu

Yesu anaphunzitsa kuti “Munalandila kwaulele, patsani kwaulele.” (Mat. 10:8) Potsatila malangizo omveka bwino amenewa, sitigulitsa mabaibo kapena zofalitsa zathu. (2 Akor. 2:17) Koma zofalitsa zimenezi zili na coonadi camtengo wapatali ca Mau a Mulungu. Kuti zipulintidwe ndi kutumizidwa ku mipingo padziko lonse, pamacitika nchito yaikulu komanso pamawonongeka ndalama zambili. Conco, tiyenela kutenga mlingo wofunikila cabe.

Tizisamalanso pogaŵila zofalitsa kwa anthu, ngakhale pa ulaliki wapoyela. (Mat. 7:6) M’malo mongogaŵila aliyense amene wapitilapo, yesani kukambako nawo kuti muone ngati ali na cidwi. Kuti mudziŵe, onani ngati mungayankheko kuti ‘inde’ pa iliyonse ya mafunso ali pa danga lili pansili. Ngati simuonapo cidwi kweni-kweni, ni bwino kum’patsa kapepa ka uthenga. Koma ngati wacita kupempha magazini kapena cofalitsa cina, m’patseni mwacimwemwe.—Miy. 3:27, 28

KODI MUNTHUYO . . .

  • amvetsela pamene mukamba?

  • nayenso akambapo?

  • avomela kuŵelenga cofalitsa?

  • avomela kukupatsani copeleka?

  • ayamikila zimene wamvela m’Mau a Mulungu?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani