LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb18 October tsa. 4
  • Akhristu Oona Amadziŵika na Cikondi—Pewani Kunyada na Mkwiyo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Akhristu Oona Amadziŵika na Cikondi—Pewani Kunyada na Mkwiyo
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Nkhani Zofanana
  • Mmene Akhristu Enieni Tingawadziŵile
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Kodi Mudziŵa Bwino Zoona Zake?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • Akhristu Oona Amadziŵika na Cikondi—Kuteteza Mgwilizano Wathu Wapadela
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Cikondi Khalidwe Lamtengo Wapatali
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2017
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
mwb18 October tsa. 4

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Akhristu Oona Amadziŵika na Cikondi—Pewani Kunyada na Mkwiyo

CIFUKWA CAKE N’KOFUNIKA: Yesu anaphunzitsa kuti ophunzila ake adzadziŵika cifukwa ca cikondi. (Yoh. 13:34, 35) Kuti tionetse cikondi monga ca Khristu, tifunika kuika zofuna za ena patsogolo na kupewa kukwiya. —1 Akor. 13:5.

MMENE TINGACITILE:

  • Ngati munthu wina wakamba kapena kucita zokukwiyitsani, yambani mwaima na kuganizila zimene zam’pangitsa kuti akambe kapena kucita zimenezo. Ganizilaninso zotulukapo za zimene mufuna kucita.—Miy. 19:11

  • Kumbukilani kuti tonse ndise opanda ungwilo, ndipo nthawi zina tingakambe kapena kucita zinthu zimene pambuyo pake tingadziimbe nazo mlandu

  • Mukasemphana maganizo, muzithetsa nkhani mwamsanga

TAMBANI VIDIYO YAKUTI “MUZIKONDANA”—PEWANI KUNYADA NDI KUCITA ZOSAYENELA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:

  • Kodi m’bale Larry anaonetsa bwanji kuti sanakondwele na lingalilo la m’bale Tom?

  • Kodi kuyamba waima kuti aganizilepo kunam’thandiza bwanji mbale Tom kuti apewe kukwiya?

  • Kodi kuyankha modekha kwa m’bale Tom kunathandiza bwanji?

Kevin, Larry, na Tom

Kodi mpingo umapindula bwanji ngati tikhalabe odekha wina akatikwiyitsa?

CITSANZO CA M’BAIBO COFUNIKA KUCISINKHA-SINKHA: Davide sanabwezele atanyozedwa na Simeyi.—2 Sam. 16:5-13.

DZIFUNSENI KUTI, ‘Ni pa zocitika ziti pamene ningafunike kudziletsa kwambili?’

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani