LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb19 October tsa. 5
  • Khalidwe Loyela na Ulemu Waukulu Zimakopa Mtima

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Khalidwe Loyela na Ulemu Waukulu Zimakopa Mtima
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • Nkhani Zofanana
  • Dalilani Mulungu Kuti Banja Lanu Likhale Lacimwemwe
    N’zotheka Banja Lanu Kukhala Lacimwemwe
  • Khalani Okhulupilika kwa Wina ndi Mnzake
    N’zotheka Banja Lanu Kukhala Lacimwemwe
  • Mmene Mungakhalile Mwamtendele ndi Acibale Anu
    N’zotheka Banja Lanu Kukhala Lacimwemwe
  • Pambuyo Pa Tsiku La Cikwati
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
mwb19 October tsa. 5

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Khalidwe Loyela na Ulemu Waukulu Zimakopa Mtima

Khalidwe labwino la akazi okwatiwa amene anakhala okhulupilila, kambili limakopa amuna awo kubwela m’coonadi. Komabe, kucita izi kungafune kupilila mavuto kwa zaka zambili. (1 Pet. 2:21-23; 3:1, 2) Ngati mukucitilidwa zinthu zopanda cilungamo, pitilizani kugonjetsa coipa mwa kucita cabwino. (Aroma 12:21) Citsanzo canu cingakhale na zotulukapo zabwino, ndipo cingathandize mwamuna wanu kukhala na maganizo oyenela ponena za coonadi.

Yesani kuona zinthu mmene mnzanu wa m’cikwati amazionela. (Afil. 2:3, 4) Khalani acifundo, ndipo citani zonse zimene mungathe kuti muzikwanilitsa maudindo anu monga mkazi wake. Khalani mvetseli wabwino. (Yak. 1:19) Khalani woleza mtima, ndipo muzimuonetsa mnzanu wa m’cikwati kuti mumamukonda. Ngakhale kuti mnzanuyo sakucitilani zinthu mokoma mtima komanso mwaulemu, dziŵani kuti Yehova amayamikila kukhulupilika kwanu.—1 Pet. 2:19, 20.

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI YEHOVA AMATITHANDIZA PA MAVUTO, NDIYENO, YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • Kodi zinthu zinali bwanji poyamba m’cikwati ca mlongo Grace Li?

  • N’ciani cinamukopa kuti ayambe kuphunzila coonadi?

  • Kodi Mlongo Li anapilila mavuto abwanji pambuyo pobatizika?

  • Kodi mlongo Li anam’pemphelela ciani mwamuna wake?

  • Ni madalitso anji amene Mlongo Li akusangalala nawo cifukwa cokhala na khalidwe loyela ndiponso ulemu waukulu?

Mlongo akuphunzila Baibo na Grace Li; Grace akulila m’khonde; Grace na ana ake akucoka mu lesitilanti yawo na kuyenda ku misonkhano; Grace ali na banja lake

Khalidwe loyela na ulemu waukulu n’zamphamvu kwambili!

Khalidwe loyela ndiponso ulemu waukulu zingathandizenso ngati mwamuna wanu ni wobatizika koma safuna kutsogolela banja pa zinthu zauzimu. Onani vidiyo yakuti Limbikitsani Mnzanu wa M’cikwati Popanda Mawu.

Mlongo akuyang’ana mwamuna wake wozilala
    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani