LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • gf phunzilo 2 tsa. 4
  • Mulungu Ndiye Angakhale Mnzanu Wabwino Kwambili

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mulungu Ndiye Angakhale Mnzanu Wabwino Kwambili
  • Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Nkhani Zofanana
  • Mukhoza Kukhala Bwenzi la Yehova
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Mulungu Akupemphani Kuti Mukhale Mnzake
    Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • “Nakuchani Mabwenzi”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2020
  • Muganiza Bwanji?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2018
Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
gf phunzilo 2 tsa. 4

Phunzilo 2

Mulungu Ndiye Angakhale Mnzanu Wabwino Kwambili

Kukhala mnzake wa Mulungu ni cinthu cabwino kuposa ciliconse cimene mungakhale naco. Iye angakuphunzitseni mmene mungapezele cimwemwe na cisungiko. Ndiponso adzakumasulani ku ziphunzitso zonama na ku vocitacita voipa. Iye adzayamba kumvela mapemphelo anu. Adzakuthandizani kukhala na mtendele wa m’maganizo na cidalilo mwa iye. (Salmo 71:5; 73:28) Panthawi ya mavuto Mulungu adzakuthandizani. (Salmo 18:18) Ndiponso Mulungu akulonjezani mphatso ya moyo wosatha.—Aroma 6:23.

Mukakhala mnzake wa Mulungu, mabwenzi ake nawo adzakhala anzanu. Ndipo iwo adzakhala monga abale na alongo anu. Adzakondwela kukuphunzitsani za Mulungu ndipo adzakulimbikitsani.

Mulungu sitilingana naye. Pamene mufuna kukhala mnzake wa Mulungu, pali mfundo ina imene muyenela kuidziwa bwino. Mfundo imeneyo ni yakuti; mukakhala mnzake wa Mulungu sindiye kuti mwalingana naye iyai. Iye wakhalapo kwa zaka zambili, ali na nzelu na mphamvu zambili kuposa ife. Iye ndiye woyenela kutilamulila. Conco ngati tifuna kukhala mnzake wa Mulungu, tifunikila kumumvela na kucita zimene amatiuza. Tikacita zimenezo, zinthu zidzatiyendela bwino.—Yesaya 48:18.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani