LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • gf phunzilo 3 tsa. 5
  • Mufunikila Kuphunzila za Mulungu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mufunikila Kuphunzila za Mulungu
  • Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Nkhani Zofanana
  • Mukhoza Kukhala Bwenzi la Yehova
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Mulungu Akupemphani Kuti Mukhale Mnzake
    Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Mmene Mungadziŵile Cipembedzo Coona
    Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
  • Muganiza Bwanji?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2018
Onaninso Zina
Na Imwe Mungakhale Mnzake wa Mulungu!
gf phunzilo 3 tsa. 5

Phunzilo 3

Mufunikila Kuphunzila za Mulungu

Kuti mukhale mnzake wa Mulungu, mufunikila kuphunzila za iye. Kodi anzanu dzina lanu alidziŵa, ndipo amalitomola? Inde. Naye Mulungu amafuna kuti dzina lake mulidziŵe, ndi kuti muzilitomola. Dzina lake ni Yehova. (Salmo 83:18; Mateyu 6:9) Ndiponso mufunikila kudziŵa zimene amafuna na zimene samafuna. Mufunikanso kudziŵa anzake na adani ake. Koma kudziŵa munthu kumatenga nthawi. Baibo imakamba kuti ni cinthu canzelu kupatula nthawi ya kuphunzila za Yehova.—Aefeso 5:15, 16.

Anzake a Mulungu amacita zimene zimamukondweletsa. Mwacitsanzo, tiyeni tikambe za anzanu. Ngati mumaŵavuta na kucita zinthu zimene samafuna, kodi angapitilize kukhala anzanu? Kutalitali! Ni cimodzimodzi na Mulungu. Ngati imwe mufuna kukhala mnzake, mufunikila kucita zimene iye amafuna.—Yohane 4:24.

Kodi zipembedzo zonse zingakuthandizeni kukhala mnzake wa Mulungu? Iyai. Yesu, amene ni mnzake wa Mulungu wapamtima, anaphunzitsa ponena za njila ziŵili. Ina niikulu ndipo ili ndi anthu ambili oyendamo. Njila imeneyo imapeleka ku cionongeko. Koma njila ina niing’ono ndipo anthu oyendamo ni ocepa. Njila imeneyi imapeleka ku moyo wosatha. Conco, ngati mufuna kukhala mnzake wa Mulungu, mufunikila kuphunzila mmene mungamulambilile mu njila yoyenela.—Mateyu 7:13, 14.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani