LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • kr nkhani 168-169
  • Maphunzilo a Ufumu—Kuphunzitsa Atumiki a Mfumu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Maphunzilo a Ufumu—Kuphunzitsa Atumiki a Mfumu
  • Ufumu wa Mulungu Ukulamulila
  • Nkhani Zofanana
  • Pitilizani Kulandila Maphunzilo Aumulungu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • Kuphunzitsa Atumiki a Ufumu
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila
  • Kodi a Mboni za Yehova Amaphunzitsidwa Bwanji Mmene Angacitile Utumiki Wawo?
    Mafunso Ofunsidwa Kaŵili-kaŵili pa Mboni za Yehova
Ufumu wa Mulungu Ukulamulila
kr nkhani 168-169
1. Msonkhano wa pamtetete wa Mboni za Yehova ku London mu 1945; 2. Msonkhano wa pamtetete wa Mboni za Yehova ku Malawi

Kumanzele: Msonkhano wa pamtetete ku London mu 1945; kulamanja: Msonkhano wa pamtetete ku Malawi

CIGAWO 5

Maphunzilo a Ufumu—Kuphunzitsa Atumiki a Mfumu

TAYELEKEZELANI kuti m’bale wina akukamba nkhani pa pulatifomu. Pamene mukumuyang’ana mukumwetulila. M’baleyu ndi wacinyamata ndipo ndi wa mumpingo wanu. Iye akukamba nkhani yake yoyamba pa msonkhano waukulu. Pamene mukumvetsela nkhaniyo, mukusoŵa conena mukaganizila maphunzilo amene anthu a Mulungu amalandila. Mukakumbukila mmene m’baleyu anavutikila nthawi yoyamba pamene anakamba nkhani papulatifamu, mukucita cidwi ndi mmene wapitila patsogolo. Iye wapita patsogolo kwambili pambuyo poloŵa Sukulu ya Apainiya. Posacedwapa, m’baleyu ndi mkazi wake analoŵa Sukulu ya Alengezi a Ufumu. Pamene m’baleyu akumaliza nkhani yake yolimbikitsa, mukuomba m’manja. Ndiyeno mukuyang’ana anthu amene muli nao pafupi ndi kuyamikila maphunzilo amene anthu onse a Mulungu amalandila.

Baibulo linanenelatu za nthawi pamene anthu onse a Mulungu ‘adzaphunzitsidwa ndi Yehova.’ (Yes. 54:13) Tikukhala m’nthawi imeneyo. Timaphunzitsidwa kupyolela m’zofalitsa zathu ndi pamisonkhano ya mpingo, kuphatikizapo misonkhano ikuluikulu. Timaphunzitsidwanso kudzela m’masukulu osiyanasiyana amene colinga cake ndi kutithandiza kusamalila mautumiki osiyanasiyana m’gulu la Yehova. M’cigawo cino, tidzaona mmene maphunzilo onsewa amapelekela umboni wamphamvu wakuti Ufumu wa Mulungu ukulamulila masiku ano.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani