LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • sjj nyimbo 19
  • Mgonelo wa Ambuye

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mgonelo wa Ambuye
  • ‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
  • Nkhani Zofanana
  • Mgonero wa Ambuye
    Imbirani Yehova
  • Khalani ndi Moyo Wopambana
    Imbirani Yehova
  • Moyo Ndi Wodabwitsa
    Imbirani Yehova
  • Moyo ni Cozizwitsa
    ‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
Onaninso Zina
‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
sjj nyimbo 19

NYIMBO 19

Mgonelo wa Ambuye

Yopulinta

(Mateyu 26:26-30)

  1. 1. Atate ise tasonkhana

    Pa tsiku lopatulika.

    Imwe munasankha kuti muonetse

    Cikondi canu kwa anthu.

    Mwana wa nkhosa anadyewa,

    Kumasula anthu anu.

    Yesu modzipeleka anatifela,

    Kukwanilitsa ulosiwo.

  2. 2. Yesu anapeleka moyo

    Kuti atipulumutse.

    Tikaona vinyo na mkate tidziŵa,

    Ukulu wa mphatso iyi.

    Timakumbukila tsikuli

    Na mtima woyamikila.

    Cifukwa tidziŵa kuti mphatso iyi

    Inatimasula ku imfa.

  3. 3. Tasonkhana pamaso panu,

    Kuti’se tiyamikile,

    Cikondi cimene munationetsa

    Potumiza mwana wanu.

    Tidziŵa kuti tsiku iyi

    Imakulemekezani.

    Tikapitiliza kutsatila Yesu,

    Tidzapeza moyo wosatha.

(Onaninso Luka 22:14-20; 1 Akor. 11:23-26.)

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani