LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 6/14 masa. 3-4
  • “Khalani ndi Khalidwe Labwino Pakati pa Anthu a m’Dzikoli”

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • “Khalani ndi Khalidwe Labwino Pakati pa Anthu a m’Dzikoli”
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Nkhani Zofanana
  • Zikumbutso za Msonkhano wa Cigawo
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Khalidwe Limene Limalemekeza Mulungu
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
km 6/14 masa. 3-4

“Khalani ndi Khalidwe Labwino Pakati pa Anthu a m’Dzikoli”

1. N’cifukwa ciani tifunika kudzakhala ndi khalidwe labwino pa misonkhano imene ikubwela?

1 Caka ciliconse panthawi ya misonkhano ya cigawo timakopa cidwi anthu ambili, conco tifunika kuonetsa khalidwe loyenela popeza timaimila Mulungu amene timalambila. (Lev. 20:26) Khalidwe lathu labwino, kavalidwe ndi maonekedwe athu zizionetsa kuti ndife otsatila oona a Kristu. Pamene tidzapezeka pa msonkhano wa cigawo kapena wa maiko, tingadzakhale bwanji ndi khalidwe labwino pakati pa anthu a m’dzikoli kuti tidzapeleke ulemelelo kwa Atate wathu wakumwamba?—1 Pet. 2:12.

2. Pa msonkhano wa cigawo tidzakhala ndi mwai wotani woonetsa umunthu wathu wa Cikristu?

2 Onetsani Umunthu Wacikristu: Cikondi cimene timaonetsana ndi mmene timacitila zinthu ndi “anthu akunja,” zimatisiyanitsa kwambili ndi anthu amene ali ndi mzimu wa dzikoli. (Akol. 3:10; 4:5; 2 Tim. 3:1-5) Ngakhale pabuke mavuto, tiyenela kukhala okoma mtima ndi oleza mtima pocita zinthu ndi anthu ogwila nchito m’mahotelo ndi m’malesitilanti. Khalidwe labwino lidzaticititsanso kupatsako ogwila nchitowo kenakake koonetsa kuyamikila.

3. Ndi cikumbutso citi cimene makolo apatsidwa? Nanga n’cifukwa ciani?

3 Makolo, mudzakhale limodzi ndi ana anu kuti mukawasamalile bwino pamalo a msonkhano, ku malesitilanti ndi ku mahotelo. (Miy. 29:15) Manijala wa pa hotelo inayake anauza okwatilana ena kuti: “Timakukondani anthu inu. Mabanja anu ndi ana anu ndi a makhalidwe abwino ndipo ndi aulemu kwambili. Aliyense wogwila nchito pano akukamba za inu, ndipo tingakonde kuti muzibwela kudzakhala pano mlungu uliwonse ukatha.”

4. Pamene tili pamalo a msonkhano tiyenela kusamala bwanji za maonekedwe athu?

4 Kuvala Moyenela: Pa msonkhano tiyenela kuvala moyenela ndi mwaulemu, osati motengela masitaelo ofala a ku dzikoli. (1 Tim. 2:9) Ngakhale pamene tipita kukaloŵa mu hotelo kapena pamene titulukamo, tiyenela kupewa zovala zimene sizipatsa ulemu. Cimodzimodzinso panthawi yopumula misonkhano isanayambe kapena ikatha. Tikatelo tidzakhala onyadila kuvala baji ya msonkhano ndipo sitidzacita manyazi kulalikila ngati tapeza mpata. Maonekedwe athu ndi khalidwe lathu labwino tikadzapezeka pamisonkhano ikubwelayi, sizidzakopa cabe anthu a mtima wabwino kuyamba kuphunzila uthenga wa m’Baibulo wopulumutsa moyo koma zidzasangalatsanso Yehova.—Zef. 3:17.

Zikumbutso za Msonkhano wa Cigawo wa 2014

◼ Nthawi ya Misonkhano: Anthu adzayamba kuloŵa pa malo a msonkhano ndi nthawi ya 07:00 hrs. Nyimbo zamalimba zidzayamba nthawi ya 08:20 hrs masiku onse atatu. Panthawi imeneyi, ife tonse tifunika kupeza malo okhalapo kuti msonkhano wathu udzayambe mwadongosolo ndi molemekezeka. Pa tsiku loyamba ndi laciŵili, nyimbo yomaliza ndi pemphelo lomaliza tizikhala nazo nthawi ya 15:55 hrs. Ndipo pa tsiku lacitatu ndi nthawi ya 15:10 hrs.

◼ Misonkhano ya Maiko: Malo ena kudzacitika misonkhano ya maiko. Dziŵani kuti ofesi ya nthambi yaitana mipingo yosankhidwa ndi alendo ocokela ku maiko ena, pambuyo poganizila malo okhala, malo oimikako magalimoto ndi malo ogona mu mahotelo. Ngati ofalitsa angapite ku msonkhano wa maiko umene sanaitanidwe, ndiye kuti kungakhale anthu oculuka kuposa amene afunika. Ngati mungalephele kupezeka pa msonkhano wanu wa cigawo ndiye mukufuna kukapezeka ku msonkhano wina, conde musadzasankhe kukapezeka pa msonkhano wa maiko. Mufunika kutsatila malangizo a akalinde amene akuyang’anila galimoto.

◼ Koimika magalimoto: Pa malo onse a msonkhano amene tapatsidwa mphamvu zoyang’anila malo oimikako magalimoto, malo azipatsidwa kwa munthu malinga ndi nthawi imene wafika. Nthawi zambili, malo oimikako magalimoto amacepa, conco ndi bwino kuyendela m’galimoto imodzi ngati zingatheke.

◼ Kusungilana Malo: M’mawa uliwonse, nthawi yoloŵa pa malo a msonkhano ikakwana, musacite kuthamanga kuti mukapeze malo amene mumawakonda monga ngati mukupikisana ndi anzanu. Mzimu wodzimana umene umatithandiza kucitila ena zabwino umaticititsa kudziŵika kuti ndife Akristu oona ndipo anthu otiona amalimbikitsidwa kutamanda Yehova. (Yoh. 13:34, 35; 1 Akor. 13:4, 5; 1 Pet. 2:12) Mungasungile malo anthu a m’banja lanu okha, kapena amene mwabwela nao m’galimoto imodzi kapenanso maphunzilo anu a Baibulo. Pakonzedwa malo okhala a odwala ndi okalamba. Popeza malo amenewa adzakhala ocepa, munthu mmodzi kapena aŵili ndi amene angakhale pamenepo kuti azisamalila odwala kapena okalamba.

◼ Cakudya ca Masana: Conde mukanyamuliletu cakudya ca masana kuti musadzacoke pa malo a msonkhano masana n’kupita kwina kukagula cakudya. Pa misonkhano imene idzacitikila m’bwalo la maseŵela lokhala ndi mipando, munganyamulile zakudya zanu m’nswanda kapena kuti basiketi imene ingakwane munsi mwa mpando wanu. Musadzabweletse zonyamulilamo zazikulu monga za ku pikiniki ndi zinthu za galasi pa malo a msonkhano amenewa.

◼ Zopeleka: Tingaonetse kuyamikila nchito imene inagwilidwa pokonzekela msonkhanowu popeleka mwaufulu ndalama zothandiza pa nchito ya padziko lonse, ndipo tingapeleke ndalamazi pamsonkhanopo. Polemba macheke opeleka pamsonkhano wa cigawo, sonyezani kuti ndalamazo zipita ku “Watch Tower Society.”

◼ Mankhwala: Ngati mumafunika mankhwala ocita kukulembelani ku cipatala, conde tsimikizilani kuti mukanyamule okwanila cifukwa ku msonkhano sadzakhalako. Masilenje ndi nyeleti zimene odwala matenda a shuga amagwilitsila nchito, siziyenela kutayidwa mu zinthu zotayilamo zinyalala pa malo a msonkhano, kapena pa hotelo. Zinthu zimenezi muyenela kuzisunga bwinobwino ndi kukazitaya mukapita kunyumba.

◼ Kupewa Ngozi: Conde, musakacititse ngozi iliyonse poika zinthu mwacisawawa zimene zingacititse ena kukhumudwa, kapena kukoledwa nazo ndi kugwa. Caka ciliconse anthu amadzipweteka cifukwa covala nsapato zazitali kwambili. Cingakhale bwino kuvala nsapato za ulemu, zokwana bwino zimene mudzakhoza kuyenda nazo bwinobwino pa malo alionse.

◼ Mapulemu ndi Mipando Yapanja: Mungabwele ndi zinthu zimenezi pa malo osankhidwa a misonkhano ya kumadela akumidzi ndi m’nyumba za misonkhano. Ngati msonkhano udzacitikila m’bwalo la maseŵela limene lili ndi mipando kale, simuyenela kubwela ndi mapulemu ndi mipando yapanja. Komabe, mungabwele ndi mipando yoikamo ana ngati idzaiikidwa pampando umene uli pafupi ndi makolo. Funsani akulu a mumpingo wanu za malangizo a kudela lanu.

◼ Mapefyumu: Kungakhale kuonetsa cikondi ngati tingasamale kwambili ndi kuculuka kapena mtundu wa pefyumu imene tingagwilitsile nchito. Izi zili conco cifukwa cakuti fungo lamphamvu la mapefyumu limacititsa anthu ena amene ali ndi matenda ovutika kupuma kuti adwale kwambili.—1 Akor. 10:24.

◼ Fomu ya Kaonaneni ndi Wacidwi Uyu (S-43): Fomu ya Kaonaneni ndi Wacidwi Uyu tingaigwilitsile nchito pofuna kudziŵikitsa munthu amene anaonetsa cidwi pa msonkhano pamene tinali kucita ulaliki wamwai. Tingapeleke mafomu amenewa ku Cipinda ca Mabuku kapena mungadzapatsile kalembela wa mpingo wanu mukadzabwelela ku nyumba.

◼ Utumiki Wodzifunila: Aliyense amene afuna kuthandiza nchito pa msonkhano wa cigawo, angalembetse ku Dipatimenti ya Anchito Odzifunila. Ana azaka 16 kubwela pansi, angagwile nchitoyi moyang’anilidwa ndi makolo ao kapena wacikulile aliyense amene kholo lingavomeleze.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani